< Colossians 3 >
1 If yee then bee risen with Christ, seeke those thinges which are aboue, where Christ sitteth at the right hand of God.
Tsono popeza munaukitsidwa pamodzi ndi Khristu, ikani mitima yanu pa zinthu za kumwamba, kumene Khristu akukhala ku dzanja lamanja la Mulungu.
2 Set your affections on things which are aboue, and not on things which are on the earth.
Muzifunafuna zinthu za kumwamba, osati zinthu za pa dziko lapansi.
3 For ye are dead, and your life is hid with Christ in God.
Pakuti munafa, ndipo moyo wanu tsopano wabisika pamodzi ndi Khristu mwa Mulungu.
4 When Christ which is our life, shall appeare, then shall ye also appeare with him in glory.
Khristu, amene ndiye moyo wanu, akadzaonekanso, pamenepo inunso mudzaoneka naye pamodzi mu ulemerero.
5 Mortifie therefore your members which are on the earth, fornication, vncleannes, the inordinate affection, euill concupiscence, and couetousnes which is idolatrie.
Choncho, iphani zilakolako za dziko lapansi mwa inu, monga: dama, zodetsa, kulakalaka zosayenera, kukhumba zoyipa ndi umbombo, pakuti umbombo ndiko kupembedza mafano.
6 For the which things sake ye wrath of God commeth on the children of disobedience.
Chifukwa cha zimenezi, mkwiyo wa Mulungu ukubwera pa ana osamvera.
7 Wherein ye also walked once, when ye liued in them.
Inunso kale munkachita zomwezi, mʼmoyo wanu wakale uja.
8 But now put ye away euen all these things, wrath, anger, maliciousnes, cursed speaking, filthie speaking, out of your mouth.
Koma tsopano mukuyenera kuzichotsa zinthu zonsezi monga: mkwiyo, ukali, dumbo, chipongwe ndi mawu onyansa.
9 Lie not one to another, seeing that yee haue put off the olde man with his workes,
Musanamizane wina ndi mnzake, popeza munavula munthu wakale pamodzi ndi zochita zake
10 And haue put on the newe, which is renewed in knowledge after the image of him that created him,
ndipo mwavala munthu watsopano, amene nzeru zake zikukonzedwanso kuti afanane ndi Mlengi wake.
11 Where is neither Grecian nor Iewe, circumcision nor vncircumcision, Barbarian, Scythian, bond, free: But Christ is all, and in all things.
Pano palibe kusiyana pakati pa Mgriki ndi Myuda, wochita mdulidwe ndi wosachita, wosaphunzira kapena wosachangamuka, kapolo kapena mfulu, koma Khristu yekha basi ndipo amakhala mwa onse.
12 Now therfore as the elect of God holy and beloued, put on the bowels of mercies, kindnesse, humblenesse of minde, meekenesse, long suffering:
Choncho, ngati anthu osankhidwa ndi Mulungu, oyera mtima ndi okondedwa kwambiri, muvale chifundo, kukoma mtima, kudzichepetsa, kufatsa ndi kupirira.
13 Forbearing one another, and forgiuing one another, if any man haue a quarel to another: euen as Christ forgaue, euen so doe ye.
Mulezerane mtima ndipo muzikhululukirana ngati wina ali ndi chifukwa ndi mnzake. Muzikhululukirana monga Ambuye anakhululukira inu.
14 And aboue all these thinges put on loue, which is the bond of perfectnes.
Ndipo kuwonjezera pa zonsezi valani chikondi, chimene chimangirira zonsezi pamodzi mu mgwirizano wangwiro.
15 And let the peace of God rule in your hearts, to the which ye are called in one body, and be ye thankfull.
Mtendere wa Khristu ulamulire mʼmitima mwanu, popeza monga ziwalo za thupi limodzi, munayitanidwa kuti mukhale ndi mtendere. Ndipo muziyamika.
16 Let the worde of Christ dwell in you plenteously in all wisdome, teaching and admonishing your owne selues, in Psalmes, and hymnes, and spirituall songs, singing with a grace in your hearts to the Lord.
Mawu a Khristu akhazikike kwathunthu mʼmitima mwanu. Muziphunzitsana ndi kulangizana wina ndi mnzake ndi nzeru zonse pamene mukuyimba Masalimo, nyimbo zotamanda ndi nyimbo zauzimu, kuyimbira Mulungu ndi mitima yoyamika.
17 And whatsoeuer ye shall doe, in worde or deede, doe all in the Name of the Lord Iesus, giuing thankes to God euen the Father by him.
Ndipo chilichonse chimene mungachite, kaya nʼkuyankhula, kaya nʼkugwira ntchito, muchite zonse mʼdzina la Ambuye Yesu, kuyamika kwa Mulungu Atate kudzera mwa Iye.
18 Wiues, submit your selues vnto your husbands, as it is comely in the Lord.
Inu akazi, gonjerani amuna anu, monga kuyenera mwa Ambuye.
19 Husbands, loue your wiues, and be not bitter vnto them.
Inu amuna, kondani akazi anu ndipo musawapsere mtima.
20 Children, obey your parents in all thing for that is well pleasing vnto the Lord.
Inu ana, mverani makolo anu mu zonse pakuti izi zimakondweretsa Ambuye.
21 Fathers, prouoke not your children to anger, least they be discouraged.
Inu abambo, musakwiyitse ana anu, kuti angataye mtima.
22 Seruants, be obedient vnto them that are your masters according to the flesh, in all things, not with eye seruice as men pleasers, but in singlenes of heart, fearing God.
Inu antchito, mverani mabwana anu mu zonse, ndipo muzichita zimenezi osati nthawi yokhayo imene akukuonani kuti akukondeni, koma muzichite moona mtima ndi mopereka ulemu kwa Ambuye.
23 And whatsoeuer ye doe, doe it heartily, as to the Lord, and not to men,
Chilichonse mungachite, muchite ndi mtima wanu onse, monga mmene mungagwirire ntchito ya Ambuye osati ya anthu.
24 Knowing that of the Lord ye shall receiue the reward of the inheritance: for ye serue the Lord Christ.
Inu mukudziwa kuti mudzalandira mphotho monga cholowa kuchokera kwa Ambuye. Ndi Ambuye Khristu amene mukumutumikira.
25 But he that doeth wrong, shall receiue for the wrong that he hath done: and there is no respect of persons.
Aliyense amene amachita zolakwa adzalandira malipiro molingana ndi kulakwa kwake, ndipo palibe tsankho.