< Acts 6 >

1 And in those dayes, as the nomber of ye disciples grewe, there arose a murmuring of the Grecians towards ye Hebrewes, because their widowes were neglected in the dayly ministring.
Mʼmasiku amenewo pamene chiwerengero cha ophunzira chinkachuluka, Ayuda a Chihelene pakati pawo anadandaula chifukwa cha Ayuda a Chihebri chifukwa amasiye awo samawagawira chakudya cha tsiku ndi tsiku.
2 Then the twelue called the multitude of the disciples together, and sayd, It is not meete that we should leaue the worde of God to serue the tables.
Tsono Atumwi khumi ndi awiriwo anasonkhanitsa ophunzira onse pamodzi ndipo anati, “Nʼkosayenera kuti ife tisiye kulalikira Mawu a Mulungu ndi kuyangʼanira za chakudya.
3 Wherefore brethren, looke ye out among you seuen men of honest report, and full of the holy Ghost, and of wisedome, which we may appoint to this busines.
Choncho abale, sankhani pakati panu anthu asanu ndi awiri a mbiri yabwino, odzazidwa ndi Mzimu Woyera ndi anzeru. Ife tidzawapatsa udindo oyangʼanira.
4 And we will giue our selues continually to prayer, and to the ministration of the worde.
Koma ife tidzadzipereka kuti tizipemphera ndi kulalikira mawu.”
5 And the saying pleased the whole multitude: and they chose Steuen a man full of fayth and of the holy Ghost, and Philippe, and Prochorus, and Nicanor, and Timon, and Parmenas, and Nicolas a Proselyte of Antiochia,
Mawu amenewa anakondweretsa gulu lonse la anthu. Iwo anasankha, Stefano, munthu wodzazidwa ndi chikhulupiriro ndiponso Mzimu Woyera; anasankhanso Filipo, Prokoro, Nikanora, Timo, Parmena ndi Nikolao amene anatembenuka mtima ndi kulowa Chiyuda kuchokera kwa Antiokeya.
6 Which they set before the Apostles: and they prayed, and layed their hands on them.
Iwo anapereka anthuwa kwa atumwi amene anawapempherera ndi kuwasanjika manja.
7 And the worde of God increased, and the nomber of the disciples was multipled in Hierusalem greatly, and a great company of the Priests were obedient to the faith.
Ndipo Mawu a Mulungu anapitirira kufalikira. Chiwerengero cha ophunzira mu Yerusalemu chinakula mofulumira ndipo ansembe ochuluka anakhulupirira.
8 Now Steuen full of faith and power, did great wonders and miracles among the people.
Stefano, munthu wodzazidwa ndi chisomo cha Mulungu ndi mphamvu anachita zodabwitsa ndiponso zizindikiro zazikulu pakati pa anthu.
9 Then there arose certaine of the Synagogue, which are called Libertines, and Cyrenians, and of Alexandria, and of them of Cilicia, and of Asia, and disputed with Steuen.
Panauka mtsutso kuchokera kwa anthu a ku Kurene ndi a ku Alekisandriya komanso a ku dera la Silisiya ndi Asiya, otchedwa a Sunagoge ya Mfulu. Anthu amenewa anayamba kutsutsana ndi Stefano.
10 But they were not able to resist the wisdome, and the Spirit by the which he spake.
Koma iwo sanathe kumugonjetsa chifukwa iye ankayankhula ndi nzeru zimene Mzimu Woyera anamupatsa.
11 Then they suborned men, which saide, We haue heard him speake blasphemous wordes against Moses, and God.
Iwo ananyengerera anthu ena mwamseri kuti anene kuti, “Ife tinamva Stefano akuchitira chipongwe Mose ndiponso Mulungu.”
12 Thus they mooued the people and the Elders, and the Scribes: and running vpon him, caught him, and brought him to the Councill,
Motero anawutsa mitima ya anthu, akulu ndi aphunzitsi amalamulo. Anamugwira Stefano ndi kumubweretsa ku Bwalo Lalikulu.
13 And set forth false witnesses, which sayd, This man ceasseth not to speake blasphemous wordes against this holy place, and the Law.
Iwo anabweretsa mboni zonama zimene zinati, “Munthu uyu akupitirirabe kuyankhula mawu onyoza malo oyera ndi malamulo.
14 For we haue heard him say, that this Iesus of Nazareth shall destroy this place, and shall change the ordinances, which Moses gaue vs.
Pakuti tinamumva akunena kuti Yesu uja wa ku Nazareti adzawononga malo ano ndiponso kusintha miyambo imene Mose anatipatsa.”
15 And as all that sate in the Councill, looked stedfastly on him, they saw his face as it had bene the face of an Angel.
Onse amene anakhala pansi Mʼbwalo Lalikulu anamuyangʼanitsitsa Stefano, ndipo anaona kuti nkhope yake ikuwala ngati ya mngelo.

< Acts 6 >