< Zephaniah 3 >
1 What disaster is coming to corrupted, rebellious Jerusalem, you who oppress people!
Tsoka kwa mzinda wa anthu opondereza, owukira ndi odetsedwa!
2 You don't listen to anybody, you don't accept correction, you don't trust in the Lord, you don't ask for God's help.
Sumvera aliyense, sulandira chidzudzulo. Sumadalira Yehova, suyandikira pafupi ndi Mulungu wake.
3 Your leaders are as greedy as roaring lions; your judges are ravenous wolves that leave nothing behind by morning.
Akuluakulu ake ali ngati mikango yobuma, olamulira ake ndi olusa ngati mimbulu ya nthawi ya madzulo, zimene pofika mmawa sizisiya chilichonse.
4 Your prophets are arrogant, deceitful men who defile what is sacred and who openly break the law.
Aneneri ake ndi odzikuza; anthu achinyengo. Ansembe ake amadetsa malo opatulika ndipo amaphwanya lamulo.
5 But the Lord who does right is still among you, he does no wrong. Every morning he gives his judgment, every day without fail. But those who act unjustly have no shame.
Yehova amene ali pakati pawo ndi wolungama; Iye salakwa. Tsiku ndi tsiku amaweruza molungama, ndipo tsiku lililonse salephera, komabe ochita zoyipa sachita manyazi nʼkomwe.
6 I have destroyed nations. Their fortresses are deserted; their streets are empty; their cities are destroyed—there are no survivors, not one.
“Ndachotseratu mitundu ya anthu; ndagwetsa malinga awo. Ndipo sindinasiye ndi mmodzi yemwe mʼmisewu mwawo, popanda aliyense wodutsa. Mizinda yawo yawonongedwa; palibe aliyense adzatsalemo.
7 I told myself, “Surely they will respect me now and accept my correction. Then their homes would not be destroyed to teach them a lesson.” But instead you're just as eager to go on doing evil.
Ndinati, ‘Ndithudi, anthu a mu mzindawu adzandiopa ndi kumvera kudzudzula kwanga!’ Ndipo sindidzawononga nyumba zawo, kapena kuwalanganso. Koma iwo anali okonzeka kuchita mwachinyengo zinthu zonse zimene amachita.
8 You just wait, declares the Lord. The day is coming when I will rise to give evidence. For I have decided to gather together all the nations and kingdoms and to pour out on them my anger, my fury and my rage. The whole earth will be burned up by the fire of my jealous anger.
Choncho mundidikire,” akutero Yehova, “chifukwa cha tsiku limene ndidzaperekera umboni. Ndatsimikiza kusonkhanitsa pamodzi mitundu ya anthu, kusonkhanitsa maufumu ndi kutsanulira ukali wanga pa iwo; mkwiyo wanga wonse woopsa. Dziko lonse lidzatenthedwa ndi moto wa mkwiyo wa nsanje yanga.
9 For then I will give the nations pure speech so they can all pray and worship the Lord together.
“Pamenepo ndidzayeretsa milomo ya anthu a mitundu yonse kuti anthu onsewo ayitane dzina la Yehova ndi kumutumikira Iye pamodzi.
10 From beyond the rivers of Ethiopia my scattered people, my worshipers, will come to bring their offerings to me.
Kuchokera kutsidya kwa mitsinje ya ku Kusi anthu anga ondipembedza, omwazikana, adzandibweretsera zopereka.
11 On that day you won't be ashamed because of what you did in rebelling against me, for I will remove from among you those who are proud and boastful. Never again will you be conceited on my holy mountain.
Tsiku limenelo simudzachita manyazi chifukwa cha zoyipa zonse munandichitira, popeza ndidzachotsa onse mu mzinda uwu amene amakondwera chifukwa cha kunyada kwawo. Simudzakhalanso odzikuza mʼphiri langa lopatulika.
12 I will leave among you those who are meek and humble, those who trust in the name of the Lord.
Koma ndidzasiya pakati panu anthu ofatsa ndi odzichepetsa, amene amadalira dzina la Yehova.
13 The people of Israel who remain will not act wickedly nor will they tell lies. They will not deceive one another. They will be able to eat in peace and sleep in safety for there will be nothing to frighten them.
Aisraeli otsala sadzachitanso zolakwika; sadzayankhulanso zonama, ngakhale chinyengo sichidzatuluka mʼkamwa mwawo. Adzadya ndi kugona ndipo palibe amene adzawachititse mantha.”
14 Sing out, Jerusalem! Shout aloud, Israel! Jerusalem, be happy and celebrate with all your heart!
Imba, iwe mwana wamkazi wa Ziyoni; fuwula mokweza, iwe Israeli! Sangalala ndi kukondwera ndi mtima wako wonse, iwe mwana wamkazi wa Yerusalemu!
15 For the Lord has turned aside from punishing you, and he has turned back your enemies. The Lord, the king of Israel, is with you, and you will never again have to fear disaster.
Yehova wachotsa chilango chako, wabweza mdani wako. Yehova, Mfumu ya Israeli, ali pakati pako; sudzaopanso chilichonse.
16 On that day the message to the people of Jerusalem will be, “Don't be afraid; don't be discouraged!”
Pa tsiku limenelo adzanena kwa Yerusalemu kuti, “Usaope, iwe Ziyoni; usafowoke.
17 The Lord your God is among you as a mighty warrior who saves. He will be so happy with you. He will renew his love for you. He will celebrate over you with loud singing.
Yehova Mulungu wako ali pakati pako, ali ndi mphamvu yopulumutsa. Adzakondwera kwambiri mwa iwe, adzakukhalitsa chete ndi chikondi chake, adzayimba mokondwera chifukwa cha iwe.”
18 I will gather those of you who mourn for the religious festivals—you will no longer have to bear the disgrace.
“Ndidzakuchotserani zowawa za pa zikondwerero zoyikika; nʼzolemetsa ndi zochititsa manyazi.
19 Look at what I am going to do! At that time I am going to deal with all those who have oppressed you. I will save those who are helpless and bring back those who were scattered, and I will turn their shame into praise, and all the world will respect them.
Taonani, nthawi imeneyo ndidzathana ndi onse amene anakuponderezani; ndidzapulumutsa olumala ndi kusonkhanitsa amene anamwazika. Ndidzawayamikira ndi kuwachitira ulemu mʼdziko lililonse mmene anachititsidwa manyazi.
20 At that time I will bring you home, gathering you together. I will give you a good reputation, and you will be praised by all the peoples of the earth when I restore your status before your very eyes, says the Lord.
Pa nthawi imeneyo ndidzakusonkhanitsani; pa nthawi imeneyo ndidzakubweretsani ku mudzi kwanu. Ndidzakuyamikirani ndi kukuchitirani ulemu pakati pa mitundu ya anthu a dziko lapansi pamene ndidzabwezeretsa mtendere wanu inu mukuona,” akutero Yehova.