< Song of Solomon 5 >
1 I enter my garden, my sister, my bride! I gather myrrh with my spice. I eat my honeycomb with my honey. I drink wine with my milk. Let us eat our fill of love! Let us be drunk with love!
Ndalowa mʼmunda mwanga, iwe mlongo wanga, iwe mkwatibwi wanga; ndasonkhanitsa mure wanga ndi zokometsera zakudya zanga. Ndadya uchi wanga pamodzi ndi zisa zake zomwe; ndamwa vinyo wanga ndi mkaka wanga. Abwenzi Idyani abwenzi anga, imwani; Inu okondana, imwani kwambiri.
2 Though I was asleep, my mind was racing. I heard my love knocking, and calling out, “Please open the door, my sister, my darling, my dove, my perfect love. My head is soaked with dew, my hair is wet from the night mist.”
Ndinagona tulo koma mtima wanga unali maso. Tamverani, bwenzi langa akugogoda: “Nditsekulire, mlongo wanga, bwenzi langa, nkhunda yanga, wangwiro wanga. Mutu wanga wanyowa ndi mame, tsitsi langa lanyowa chifukwa cha nkhungu ya usiku.”
3 I replied, “I've already got undressed. I don't have to get dressed again, do I? I've already washed my feet. I don't have to make them dirty again, do I?”
Ndavula kale zovala zanga, kodi ndizivalenso? Ndasamba kale mapazi anga kodi ndiwadetsenso?
4 My love thrust his hand into the opening. Deep inside I longed for him.
Bwenzi langa anapisa dzanja lake pa chibowo cha pa chitseko; mtima wanga unagunda chifukwa cha iye.
5 I got up to let my love in. My hands dripped with myrrh, my fingers with liquid myrrh, as I grabbed the handles of the bolt.
Ndinanyamuka kukamutsekulira wachikondi wangayo, ndipo manja anga anali noninoni ndi mure, zala zanga zinali mure chuchuchu, pa zogwirira za chotsekera.
6 I opened up to my love, but he had left—he was gone! I was crushed as a result. I looked for him but I couldn't find him. I called him but he didn't answer.
Ndinamutsekulira wachikondi wanga, koma nʼkuti wachikondi wangayo atachoka; iye anali atapita. Mtima wanga unafumuka chifukwa cha kuchoka kwake. Ndinamuyangʼanayangʼana koma sindinamupeze. Ndinamuyitana koma sanandiyankhe.
7 The watchmen found me as they went through the city. They beat me, they hurt me, and stole my cloak, those watchmen of the walls.
Alonda anandipeza pamene ankayendera mzindawo. Anandimenya ndipo anandipweteka; iwo anandilanda mwinjiro wanga, alonda a pa khoma aja!
8 Women of Jerusalem, promise me if you find my love and wonder what you should tell him, tell him I am weak with love.
Inu akazi a ku Yerusalemu ndithu ndikukupemphani, mukapeza wokondedwa wangayo, kodi mudzamuwuza chiyani? Muwuzeni kuti ine ndadwala nacho chikondi.
9 Why is the one you love better than any other, most beautiful of women? In what way is the one you love better than any other that we should promise you that?
Iwe wokongola kuposa akazi onsewa, kodi wokondedwa wakoyo ndi wopambana wina aliyense bwanji? Kodi wokondedwa wakoyo ndi wopambana ena onse chotani kuti uzichita kutipempha motere?
10 My love has dazzling good looks and is very fit—better than ten thousand others!
Wokondedwa wangayo ndi wowala kwambiri ndi wathanzi pakati pa anthu 1,000.
11 His head is like the finest gold, his hair is wavy and black as the raven.
Mutu wake ndi golide woyengeka bwino; tsitsi lake ndi lopotanapotana, ndiponso lakuda bwino ngati khwangwala.
12 His eyes are like doves beside springs of water, washed with milk and mounted like sparkling jewels.
Maso ake ali ngati nkhunda mʼmbali mwa mitsinje ya madzi, ngati nkhunda zitasamba mu mkaka, zitayima ngati miyala yamtengowapatali.
13 His cheeks are like a flowerbed of spices that produces fragrance. His lips are like lilies, dripping with liquid myrrh.
Masaya ake ali ngati timinda ta mbewu zokometsera zakudya zopatsa fungo lokoma. Milomo yake ili ngati maluwa okongola amene akuchucha mure.
14 His arms are round bars of gold inlaid with jewels. His abdomen is like carved ivory inlaid with lapis lazuli.
Manja ake ali ngati ndodo zagolide zokongoletsedwa ndi miyala yamtengowapatali. Thupi lake ndi losalala ngati mnyanga wanjovu woyikamo miyala ya safiro.
15 His legs are columns of alabaster set on bases of gold. He looks strong, like the mighty cedars of Lebanon.
Miyendo yake ili ngati mizati yamwala, yokhazikika pa maziko a golide. Maonekedwe ake ali ngati Lebanoni, abwino kwambiri ngati mkungudza.
16 His mouth is the sweetest ever; he is totally desirable! This is my love, my friend, women of Jerusalem.
Milomo yake ndi yosangalatsa kwambiri; munthuyo ndi wokongola kwambiri! Uyu ndiye wachikondi wanga ndi bwenzi langa, inu akazi a ku Yerusalemu.