< Proverbs 15 >
1 A kind reply wards off anger, but hurtful words make people mad.
Kuyankha kofatsa kumathetsa mkwiyo, koma mawu ozaza amautsa ukali.
2 What wise people say makes knowledge attractive, but stupid people talk a lot of nonsense.
Munthu wanzeru amayankhula zinthu za nzeru, koma pakamwa pa zitsiru pamatulutsa za uchitsiru.
3 The Lord sees everywhere, watching the evil and the good.
Maso a Yehova ali ponseponse, amayangʼana pa oyipa ndi abwino omwe.
4 Gentle words are a source of life, but telling lies does a lot of damage.
Kuyankhula kodekha kuli ngati mtengo wopatsa moyo, koma kuyankhula kopotoka kumapweteka mtima.
5 Only a foolish son despises his father's instruction, but one who accepts correction is sensible.
Chitsiru chimanyoza mwambo wa abambo ake, koma wochenjera amasamala chidzudzulo.
6 There's plenty of treasure where good people live, but the income of the wicked brings them trouble.
Munthu wolungama amakhala ndi chuma chambiri, zimene woyipa amapindula nazo zimamugwetsa mʼmavuto.
7 Wise people share their knowledge, but stupid people don't think like that.
Pakamwa pa anthu anzeru pamafalitsa nzeru; koma mitima ya zitsiru sitero.
8 The Lord hates the sacrifices of the wicked, but he loves the prayers of the good.
Nsembe za anthu oyipa zimamunyansa Yehova, koma amakondwera ndi pemphero la anthu owona mtima.
9 The Lord hates the ways of the wicked, but he loves those who do what is right.
Ntchito za anthu oyipa zimamunyansa Yehova koma amakonda amene amafunafuna chilungamo.
10 If you leave the right path you will be severely disciplined; anyone who hates correction will die.
Amene amasiya njira yabwino adzalangidwa koopsa. Odana ndi chidzudzulo adzafa.
11 Those already dead have no secrets from the Lord—how much more does he know our thoughts! (Sheol )
Manda ndi chiwonongeko ndi zosabisika pamaso pa Yehova, nanji mitima ya anthu! (Sheol )
12 Scoffers don't like to be corrected, so they don't go to the wise for advice.
Wonyoza sakonda kudzudzulidwa; iye sapita kwa anthu anzeru.
13 If you're happy inside, you'll have a cheerful face, but if you're sad, you look crushed.
Mtima wokondwa umachititsa nkhope kukhala yachimwemwe, koma mtima wosweka umawawitsa moyo.
14 An insightful mind looks for knowledge, but stupid people feed on foolishness.
Mtima wa munthu wozindikira zinthu umafunafuna nzeru, koma pakamwa pa zitsiru pamadya uchitsiru wawo.
15 The life of poor people is hard, but if you stay cheerful, it's a continual feast.
Munthu woponderezedwa masiku ake onse amakhala oyipa, koma mtima wachimwemwe umakhala pa chisangalalo nthawi zonse.
16 It's better to respect the Lord and only have a little than to have plenty of money and the trouble that comes with it.
Kuli bwino kukhala ndi zinthu pangʼono nʼkumaopa Yehova, kusiyana ndi kukhala ndi chuma chambiri uli pamavuto.
17 Better a dinner of vegetables where there's love than eating meat with hatred.
Kuli bwino kudyera ndiwo zamasamba pamene pali chikondi, kusiyana ndi kudyera nyama yangʼombe yonenepa pamene pali udani.
18 Short-tempered people stir up trouble, but those slow to anger calm things down.
Munthu wopsa mtima msanga amayambitsa mikangano, koma munthu woleza mtima amathetsa ndewu.
19 The way of lazy people is overgrown with thorns, but the path of the good is an open highway.
Njira ya munthu waulesi ndi yowirira ndi mtengo waminga, koma njira ya munthu wolungama ili ngati msewu waukulu.
20 A wise son makes his father happy, but a stupid man despises his mother.
Mwana wanzeru amakondweretsa abambo ake, koma mwana wopusa amanyoza amayi ake.
21 Stupidity makes people with no sense happy, but sensible people do what is right.
Uchitsiru umakondweretsa munthu wopanda nzeru, koma munthu womvetsa zinthu amayenda mowongoka.
22 Plans fall apart without good advice, but with plenty of advisors they're successful.
Popanda uphungu zolinga zako munthu zimalephereka, koma pakakhala aphungu ambiri zolinga zimatheka.
23 A good answer makes people happy—it's great to say the right thing at the right moment!
Munthu amakondwera ndi kuyankha koyenera, ndipo mawu onena pa nthawi yake ndi okoma.
24 Life's path for the wise leads upwards, so that they can avoid the grave below. (Sheol )
Munthu wanzeru amatsata njira yopita ku moyo kuti apewe malo okhala anthu akufa. (Sheol )
25 The Lord pulls down the house of the proud, but he protects the boundaries of the widow's property.
Yehova amapasula nyumba ya munthu wonyada koma amasamalira malo a mkazi wamasiye.
26 The Lord hates the thoughts of the wicked, but he honors the words of the pure.
Maganizo a anthu oyipa amamunyansa Yehova, koma mawu a anthu oyera mtima amamusangalatsa.
27 People greedy for ill-gotten gains make trouble for their families, but those who hate bribes will live.
Munthu wofuna phindu mwachinyengo amavutitsa banja lake, koma wodana ndi ziphuphu adzakhala ndi moyo.
28 Good people think how best to answer questions, but stupid people say all kinds of evil things.
Munthu wolungama amaganizira za mmene ayankhire, koma pakamwa pa munthu woyipa pamatulutsa mawu oyipa.
29 The Lord keeps his distance from the wicked, but he hears the prayers of the good.
Yehova amakhala kutali ndi anthu oyipa, koma amamva pemphero la anthu olungama.
30 Bright eyes make you happy, and good news makes you feel good.
Kuwala kwa maso kumasangalatsa mtima ndipo uthenga wabwino umalimbitsa munthu.
31 If you pay attention to positive advice you'll be one of the wise.
Womvera mawu a chidzudzulo amene apatsa moyo adzakhala pakati pa anthu anzeru.
32 If you ignore instruction you have no self-esteem, but if you listen to correction you gain understanding.
Amene amanyoza mwambo amadzinyoza yekha, koma womvera mawu a chidzudzulo amapeza nzeru zomvetsa zinthu.
33 Respect for the Lord teaches wisdom; humility goes before honor.
Kuopa Yehova kumaphunzitsa munthu nzeru, ndipo kudzichepetsa ndi ulemu chili patsogolo ndi kudzichepetsa.