< Leviticus 5 >

1 If you sin by not giving the evidence you have about a legal case, whether you saw something yourself or heard about it, you bear responsibility for your guilt.
“‘Ngati munthu anayitanidwa ku bwalo kuti akachitire umboni pa zimene anaziona kapena kuzimva koma iye nʼkukana kuchitira umboni, munthu ameneyo wachimwa ndipo ayenera kulangidwa.
2 If you touch anything unclean such as the dead body of any unclean wild animal or farm animals or vermin, even if you're unaware of it, you become unclean and guilty.
“‘Munthu akakhudza chinthu chilichonse chodetsedwa, monga nyama yakufa ya mʼthengo, kapena chiweto chakufa kapenanso chokwawa chakufa, ngakhale iyeyo wachikhudza mosadziwa, wasanduka wodetsedwa ndipo wachimwa.
3 If you touch something unclean from someone else who is unclean, even if you're unaware of it, you become guilty.
“‘Munthu akakhudza choyipitsa munthu cha mtundu uliwonse, ndipo pochikhudzapo ndi kuyipitsidwa nacho mosadziwa, munthuyo adzakhala wopalamula akangodziwa chimene wachitacho.
4 If you foolishly swear to do something, (whether good or bad, and in whatever way people impulsively swear an oath), even if you're unaware of it being wrong, when you eventually realize it, you are guilty.
“‘Munthu akalumbira mofulumira kapena mosasamala kuti adzachita chinthu, choyipa kapena chabwino, ngakhale kuti wachita izi mosadziwa kuti nʼkulakwa, pamene wazindira kulakwa kwake, iye adzakhalabe wopalamula akangodziwa chimene wachitacho.
5 If you become guilty in one of these ways, you must confess your sin,
“‘Pamene munthu wazindikira kuti wachimwa motere, awulule tchimo limene wachitalo.
6 and you must take your guilt offering of a female lamb or goat to the Lord as a sin offering for your sin. The priest will make your sin right.
Pambuyo pake, munthuyo abwere kwa Yehova ndi mwana wankhosa wamkazi kapena mbuzi kuti ikhale chopereka chopepesera tchimo ndipo wansembe achite mwambo wopepesera tchimo lomwe wachitalo. Tsono wansembe achite mwambo wopepesera tchimo la munthuyo.
7 If you can't afford a lamb, you may offer to the Lord as compensation for your sin two turtledoves or two young pigeons, one as a sin offering and one as a burnt offering.
“‘Ngati munthuyo alibe mwana wankhosa, abweretse njiwa ziwiri kapena nkhunda ziwiri kwa Yehova ngati chopereka chopepesera tchimo lake. Imodzi ikhale nsembe yopepesera tchimo, ndipo inayo ikhale nsembe yopsereza.
8 You are to take them to the priest, who shall present the first one as the sin offering. He is to wring its head from the neck without removing it completely.
Tsono abwere nazo kwa wansembe, ndipo wansembeyo ayambe wapereka mbalame imodzi ngati yopepesera tchimo. Apotole khosi koma osayidula mutu,
9 Then he is to sprinkle some of the blood of the sin offering on the side of the altar while the rest of the blood is poured out at the bottom of the altar. It is a sin offering.
kenaka awaze magazi a chopereka chopepesera tchimocho mʼmbali mwa guwa. Magazi ena onse awathire pa tsinde la guwa. Imeneyi ndi nsembe yopepesera tchimo.
10 The priest must then prepare the second bird as a burnt offering according to the regulations. In this way the priest will make you right for your sin, and you will be forgiven.
Pambuyo pake wansembe apereke mbalame inayo kuti ikhale chopereka chopsereza potsata mwambo wake. Wansembe atatha kupereka nsembe yopepesera tchimo limene munthu uja wachita, wochimwayo adzakhululukidwa.
11 If you can't afford two turtledoves or two young pigeons you may bring a tenth of an ephah of the best flour as a sin offering. Don't put olive oil or frankincense on it, because it is a sin offering.
“‘Koma ngati munthuyo alibe njiwa ziwiri kapena nkhunda ziwiri, abweretse ufa wosalala wokwanira kilogalamu imodzi kuti ukhale chopereka chopepesera tchimo limene wachita. Asathiremo mafuta kapena lubani chifukwa ndi chopereka chopepesera tchimo.
12 Take it to the priest, who shall take a handful as a ‘reminder part’ and burn it on the altar on top of the burnt offerings to the Lord. It is a sin offering.
Abweretse ufawo kwa wansembe ndipo wansembeyo atapeko dzanja limodzi kuti ukhale ufa wachikumbutso ndi kuwutentha pa guwa pamodzi ndi chopereka chopsereza kwa Yehova. Imeneyi ndi nsembe yopepesera tchimo.
13 This is how the priest will make right any of these sins you have committed, and you will be forgiven. The rest of the offering will belong to the priest, just like the grain offering.”
Umu ndi mmene wansembe adzachitire mwambo wopepesera machimo ena aliwonse amene munthu wachita, ndipo munthuyo adzakhululukidwa. Zopereka zonse zotsala zidzakhala za wansembeyo monga momwe amachitira ndi chopereka chachakudya.’”
14 The Lord told Moses,
Yehova anawuza Mose kuti,
15 “If any of you neglects unintentionally all that the Lord has declared belong to him and are holy, you must bring your guilt offering to the Lord: a ram without defects from your herd or but one of equivalent value in silver shekels (according to the sanctuary shekel standard). It is a guilt offering.
“Munthu akachita zinthu mosakhulupirika, nachimwa mosadziwa posapereka zinthu zopatulika zofunika kwa Yehova, munthuyo apereke kwa Yehova nsembe yopepesera machimo ake. Nsembeyo ikhale nkhosa yayimuna yopanda chilema ndipo mtengo wake ukhale wokwana masekeli oyenera a siliva pakawerengedwe ka ku Nyumba ya Mulungu. Imeneyi ndi nsembe yopepesera kupalamula.
16 As regards any holy requirement you failed to contribute, you must pay compensation by adding a fifth of its value to it and then give it to the priest, who will make it right with the ram as a guilt offering, and you will be forgiven.
Munthuyo ayenera kubweza zinthu zopatulika zimene sanaperekezo. Awonjezepo chimodzi mwa zigawo zisanu zilizonse ndi kuzipereka zonsezo kwa wansembe amene adzachita mwambo wopepesera machimo a munthuyo, popereka nkhosa yayimuna ija ngati nsembe yopepesera ndipo wochimwayo adzakhululukidwa.
17 If you sin and break any of the Lord's commandments, even if you are unaware of it, you are still guilty and bear responsibility for your guilt.
“Ngati munthu wachimwa mosadziwa pochita chilichonse chimene Yehova salola, munthuyo ndi wopalamula ndithu, ndipo ayenera kulangidwa.
18 You must take to the priest a ram without defects of the appropriate value from the flock as a guilt offering. Then the priest will make right for you the wrong you did in ignorance, and you will be forgiven.
Abwere kwa wansembe ndi chopereka chopepesera kupalamula kwake. Chopereka chikhale nkhosa yayimuna yopanda chilema ndipo mtengo wake ukhale woyenera nsembe yopepesera kupalamula kumene anachimwa mosadziwako, ndipo munthuyo adzakhululukidwa.
19 It is a guilt offering because you were guilty as far as the Lord was concerned.”
Imeneyi ndi nsembe yopepesera kupalamula popeza munthuyo wapezeka wolakwa pamaso pa Yehova.”

< Leviticus 5 >