< Leviticus 2 >
1 When you bring a grain offering to the Lord, your offering be of the best flour. Pour olive oil on it and put frankincense on it,
“‘Munthu wina aliyense akabwera ndi nsembe ya chakudya kwa Yehova, chopereka chake chizikhala ufa wosalala. Ufawo ausakanize ndi mafuta ndi lubani,
2 and take it to Aaron's sons the priests. The priest shall take a handful of the flour and olive oil mixture, as well as all the frankincense, and burn this as a ‘reminder part’ on the altar, a food offering, to be accepted by the Lord.
ndipo apite nawo kwa ansembe, ana a Aaroni. Atapeko modzazitsa dzanja ufa wosalala uja kuti ukhale wachikumbutso pamodzi ndi mafuta ndi lubani ndipo atenthe zonsezi pa guwa lansembe kuti zilandiridwe ndi Yehova mʼmalo mwa chopereka chonse. Iyi ndi nsembe yotentha pa moto ndiponso fungo lokomera Yehova.
3 The rest of the grain offering is for Aaron and his sons; it is a most holy part of the offerings given to the Lord as food offerings.
Zotsala za nsembe ya chakudyazo ndi za Aaroni pamodzi ndi ana ake. Chimenechi ndi chigawo chopatulika kwambiri chifukwa chatapidwa pa chopereka chotentha pa moto cha Yehova.
4 If your offering is of grain baked in an oven, it must be made from fine flour without using yeast. It can be cakes mixed with olive oil or wafers with olive oil spread on them.
“‘Ukabweretsa nsembe ya chakudya chophika mu uvuni, ikhale ya buledi wa ufa wosalala wopanda yisiti koma wosakaniza ndi mafuta, kapena timitanda ta buledi topyapyala, topanda yisiti koma topaka mafuta.
5 If your offering is a grain offering cooked on a griddle, it must be made of fine flour mixed with olive oil without using yeast.
Ngati nsembe yako yachakudya ndi yophika pa chitsulo chamoto, ikhale ya buledi wa ufa wosalala wopanda yisiti koma wosakaniza ndi mafuta.
6 Break it up and pour olive oil over it; it is a grain offering.
Umuduledule bulediyo ndi kumupaka mafuta; imeneyo ndi nsembe yachakudya.
7 If your offering is a grain offering cooked in a pan, it must be made of fine flour with olive oil.
Ngati nsembe yako yachakudya ndi yophikidwa pa chiwaya, ikhale ya buledi wa ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta.
8 Bring to the Lord the grain offering made in whichever of these ways. Present it to the priest, and who will take it to the altar.
Munthu azibwera ndi nsembe za chakudya zimene wapanga ndi zinthu zimenezi. Atachipereka kwa wansembe, iyeyu adzipita nacho ku guwa.
9 The priest is to take the ‘reminder part’ from the grain offering and burn it on the altar as a food offering, to be accepted by the Lord.
Wansembeyo atengeko gawo lina la nsembeyo kukhala ufa wachikumbutso kuti ilandiridwe ndi Yehova mʼmalo mwa nsembe yonse ndipo ayitenthe pa moto monga nsembe yopsereza ya fungo lokomera Yehova.
10 The rest of the grain offering is for Aaron and his sons; it is a most holy part of the food offerings given to the Lord.
Zotsala za nsembe ya chakudyayo zikhale za Aaroni ndi ana ake. Chimenechi ndi chigawo chopatulika kwambiri chifukwa chatapidwa pa chopereka chotentha pa moto cha Yehova.
11 No grain offering that you give to the Lord may be made using yeast. Don't burn any yeast or honey as a food offering to the Lord.
“‘Nsembe ya chakudya chilichonse imene ubweretsa kwa Yehova ikhale yopanda yisiti, pakuti suyenera kupereka kwa Yehova nsembe yotentha pa moto imene ili ndi yisiti kapena uchi.
12 You may give them to the Lord when you present your offerings of firstfruits, but they are not to be offered on the altar to be to be accepted by the Lord.
Ziwirizi ungathe kubwera nazo kwa Yehova ngati chopereka cha zokolola zoyambirira. Koma usazitenthe pa guwa kuti zikhale fungo lokomera Yehova.
13 All of your grain offerings are to be seasoned with salt. Don't leave the salt of God's agreement out of your grain offering. Add salt to all of your offerings.
Zopereka zako zonse zachakudya uzithire mchere. Usayiwale kuthira mchere pa chopereka chako popeza mcherewo ukusonyeza pangano pakati pa iwe ndi Mulungu wako. Tsono uzinthira mchere pa chopereka chako chilichonse.
14 When you bring a grain offering of firstfruits to the Lord, offer crushed heads of new grain roasted on the fire.
“‘Mukamapereka kwa Yehova chopereka cha chakudya choyamba kucha, choperekacho chikhale cha chipatso chatsopano chokazinga pa moto ndi chopunthapuntha.
15 Put olive oil and frankincense on it; it is a grain offering.
Uchithire mafuta ndi lubani pakuti ndi chopereka cha chakudya.
16 The priest will burn the ‘reminder part’ of the crushed grain and olive oil, as well as all its frankincense, as a food offering to the Lord.”
Tsono wansembe atenthe gawo la chopereka chopunthapuntha chija kuti chikhala ufa wachikumbutso ndi cha mafuta pamodzi ndi lubani yense kuti Yehova alandire mʼmalo mwa zopereka zonse. Ichi ndi chopereka chotentha pa moto cha Yehova.