< Lamentations 3 >
1 I am the man who has experienced suffering under the rod of God's anger.
Ine ndine munthu amene ndaona masautso ndi ndodo ya ukali wake.
2 He has driven me away, forcing me to walk in darkness instead of the light.
Wandipititsa kutali ndipo wandiyendetsa mu mdima osati mʼkuwala;
3 In fact he hits me again and again all day long.
zoonadi anandikantha ndi dzanja lake mobwerezabwereza tsiku lonse.
4 He has worn me out; he has broken me in pieces.
Wakalambitsa khungu langa ndi mnofu wanga, ndipo waphwanya mafupa anga.
5 He has besieged me, surrounding me with bitterness and misery.
Wandizinga ndi kundizungulira ndi zowawa ndi zolemetsa.
6 He has forced me to live in darkness like those long dead.
Wandikhazika mu mdima ngati amene anafa kale.
7 He has built a wall around me so I can't escape; he has bound me with heavy chains.
Wandimangira khoma kotero kuti sindingathawe, wandimanga ndi maunyolo.
8 Even when I keep on crying out for help, he refuses to listen to my prayer.
Ngakhale pamene ndifuwula kapena kupempha chithandizo, amakana pemphero langa.
9 He has put stone blocks in my way and sends me down crooked paths.
Wanditsekera njira yanga ndi miyala yosema; ndipo wakhotetsa tinjira tanga.
10 He is a bear that lies in wait for me, a lion in hiding ready to attack,
Wandidikirira ngati chimbalangondo, wandibisalira ngati mkango.
11 He dragged me from my path and ripped me to pieces, leaving me helpless.
Wandikokera pambali ndi kundingʼambangʼamba, ndipo wandisiya wopanda thandizo.
12 He loaded his bow with an arrow and used me as his target,
Wakoka uta wake ndipo walunjikitsa mivi yake pa ine.
13 He shot me in my kidneys with his arrows.
Walasa mtima wanga ndi mivi ya mʼphodo mwake.
14 Now everyone laughs at me, singing songs that mock me all day long.
Ndinakhala choseketsa cha anthu anga onse; amandinyodola mʼnyimbo zawo tsiku lonse.
15 He has filled me with bitterness; he has filled me up with bitter wormwood.
Wandidyetsa zowawa ndipo wandimwetsa ndulu.
16 He has broken my teeth with grit; he has trampled me in the dust.
Wathyola mano anga ndi miyala; wandiviviniza mʼfumbi;
17 Peace has been torn away from me; I've forgotten all that's good in life.
Wandichotsera mtendere; ndayiwala kuti kupeza bwino nʼchiyani.
18 That's why I say, “My expectation of a long life is gone, along with all that I hoped for from Lord.
Choncho ndikuti, “Ulemerero wanga wachoka ndi zonse zimene ndimayembekeza kwa Yehova.”
19 Don't forget everything I've suffered in my wandering, as bitters as wormwood and poison.
Kukumbukira masautso anga ndi kusowa pokhala, zili ngati zowawa ndi ndulu.
20 I certainly haven't forgotten. I remember it all too well, so I sink into depression.
Ine ndikuzikumbukira bwino izi, ndipo moyo wanga wathedwa mʼkati mwanga.
21 But I still hope when I think about this:
Komabe ndimakumbukira zimenezi, nʼchifukwa chake ndili ndi chiyembekezo.
22 It's because of the Lord's trustworthy love that our lives are not finished, for through his merciful actions he never lets us down.
Ife sitinawonongekeretu chifukwa chikondi cha Yehova ndi chachikulu, ndi chifundo chake ndi chosatha.
23 He renews them every morning. How wonderfully trustworthy you are, Lord!
Zimaoneka zatsopano mmawa uliwonse; kukhulupirika kwanu nʼkwakukulu.
24 The Lord is all I need,” I tell myself, “so I will put my hope in him.”
Mu mtima mwanga ndimati, “Yehova ndiye zanga zonse; motero ndimamuyembekezera.”
25 The Lord is good to those who trust in him, to anyone who seeks to follow him.
Yehova ndi wabwino kwa amene amayembekezera Iye, kwa munthu amene amafunafuna Iyeyo;
26 It is good to wait quietly for the Lord's salvation.
nʼkwabwino kudikira chipulumutso cha Yehova modekha.
27 It is good for people to learn to patiently bear discipline while they're still young.
Nʼkwabwino kuti munthu asenze goli pamene ali wamngʼono.
28 They should sit by themselves in silence, because it's God who has disciplined them.
Akhale chete pa yekha, chifukwa Yehova wamusenzetsa golilo.
29 They should bow low with their faces to the ground, for there may still be hope.
Abise nkhope yake mʼfumbi mwina chiyembekezo nʼkukhalapobe.
30 They should turn a cheek to someone who wants to slap them; they should take the insults of others.
Apereke tsaya lake kwa iye amene angamumenye, ndipo amuchititse manyazi.
31 For the Lord won't abandon us forever.
Chifukwa Ambuye satayiratu anthu nthawi zonse.
32 Even though he may bring sadness, he shows us mercy because his trustworthy love is so great.
Ngakhale amabweretsa zowawa, Iye adzawachitira chifundo, chifukwa chikondi chake ndi chosatha.
33 For he doesn't willingly hurt people, or cause them grief.
Pakuti sabweretsa masautso mwadala, kapena zowawa kwa ana a anthu.
34 Whether it's mistreating all the prisoners of the land,
Kuphwanya ndi phazi a mʼndende onse a mʼdziko,
35 Or denying someone their rights as the Most High watches,
kukaniza munthu ufulu wake pamaso pa Wammwambamwamba,
36 Or cheating someone in their legal case—these things the Lord doesn't approve of.
kumana munthu chiweruzo cholungama— kodi Ambuye saona zonsezi?
37 Who spoke and it came into existence? Wasn't it the Lord who commanded it?
Kodi ndani angayankhule zinthu nʼkuchitika ngati Ambuye sanavomereze?
38 When the Most High speaks it can be a disaster or a blessing.
Kodi zovuta ndi zabwino sizituluka mʼkamwa mwa Wammwambamwamba?
39 Why should any human being complain about the results of their sins?
Kodi nʼchifukwa chiyani munthu aliyense wamoyo amadandaula akalangidwa chifukwa cha machimo ake?
40 We should look at ourselves, examine what we're doing, and return to the Lord.
Tiyeni tisanthule ndi kuyesa njira zathu, ndipo tiyeni tibwerere kwa Yehova.
41 Let's not just hold up our hands to God in heaven, but our minds as well, saying,
Tiyeni tikweze mitima yathu ndi manja athu kwa Mulungu kumwamba ndipo tinene kuti:
42 “We are the ones who sinned; we are the ones who rebelled; and you haven't forgiven us!”
“Ife tachimwa ndi kuwukira ndipo inu simunakhululuke.
43 You have wrapped yourself in anger and chased us down, killing without mercy. You have killed without pity.
“Mwadzikuta ndi mkwiyo ndi kutilondola ndipo mwatitha mopanda chifundo.
44 You have wrapped yourself with a cloud that no prayer can penetrate.
Mwadzikuta mu mtambo kotero mapemphero athu sakukufikani.
45 You have made us waste and refuse to the nations around.
Mwatisandutsa zinyatsi ndi zinyalala pakati pa mitundu ya anthu.
46 All our enemies open their mouths to criticize us.
“Adani anthu atitsekulira pakamwa.
47 We're terrified and trapped, devastated and destroyed.
Ife tadzazidwa ndi mantha pakuti tagwa mʼdzenje, tapasuka ndi kuwonongedwa.”
48 Tears stream from my eyes over the death of my people.
Misozi mʼmaso mwanga ikungoti mbwembwembwe chifukwa anthu anga akuwonongedwa.
49 My eyes overflow with tears all the time. They won't stop
Misozi idzatsika kosalekeza, ndipo sidzasiya,
50 Until the Lord looks down from heaven and sees what's going on.
mpaka Yehova ayangʼane pansi kuchokera kumwamba ndi kuona.
51 What I've seen torments me because of what's happened to all the women in my city.
Mtima wanga ukupweteka poona zimenezi chifukwa cha akazi onse a mu mzinda.
52 For no reason my enemies trapped me like a bird.
Akundisaka ngati mbalame, amene anali adani anga, popanda chifukwa.
53 They tried to kill me by tossing me into a pit and throwing stones at me.
Ayesa kundipha pondiponya mʼdzenje ndi kundiponya miyala;
54 Water flooded over my head, and I thought I was going to die.
madzi anamiza mutu wanga ndipo ndinkaganiza kuti imfa yayandikira.
55 I called out for you, Lord, from deep inside the pit.
Ndinayitana dzina lanu Inu Yehova, kuchokera mʼdzenje lozama.
56 You heard me when I prayed, “Please don't ignore my cry for help.”
Inu munamva kudandaula kwanga. “Mundimvere kulira kwanga kopempha thandizo.”
57 You came to me when I called you, and you told me, “Don't be afraid!”
Munafika pafupi pamene ndinakuyitanani, ndipo munati, “Usaope.”
58 You have taken my case and defended me; you have saved my life!
Inu Ambuye munandiwombola ku mlandu wanga; munapulumutsa moyo wanga.
59 Lord, you have seen the injustices done to me; please vindicate me!
Yehova, mwaona zoyipa zimene andichitira. Mundiweruzire ndinu!
60 You have observed how vengeful they are and how often they've plotted against me.
Mwaona kuzama kwa kubwezera kwawo, chiwembu chawo chonse pa ine.
61 Lord, you have heard how they've insulted me, and what they've plotted against me,
Inu Yehova mwamva kunyoza kwawo, chiwembu chawo chonse pa ine,
62 How my enemies talk against me and complain about me all the time!
manongʼonongʼo a adani anga ondiwukira ine tsiku lonse.
63 Just look! Whether they're sitting down and or standing up, they go on making fun of me in their songs.
Tawaonani! Kaya ali pansi kapena kuyimirira, akundinyoza mu nyimbo zawo.
64 Pay them back as they deserve, Lord, for all they've done!
Inu Yehova, muwabwezere chowayenera, chifukwa cha zimene manja awo achita.
65 Give them a covering for their minds! May your curse be on them!
Phimbani mitima yawo, ndipo matemberero anu akhale pa iwo!
66 Chase them down in your anger, Lord, and get rid of them from the earth!
Muwalondole mwaukali ndipo muwawonongeretu pa dziko lapansi.