< Judges 2 >

1 The angel of the Lord went from Gilgal to Bokim and told the people, “I led you out of the land of Egypt and brought you to this land that I promised to your forefathers, and I said I would never break the agreement I made with you.
Mngelo wa Yehova anapita ku Bokimu kuchokera ku Giligala ndipo anati kwa Aisraeli, “Ndinakutulutsani mʼdziko la Igupto ndikukulowetsani mʼdziko limene ndinalumbira kwa makolo anu. Ndinati ‘Sindidzaswa pangano langa ndi inu,
2 I also told you not to make any agreements with the people living in the land and to tear down their altars. But you refused to obey what I said. Why did you do this?
ndipo inu musadzachite pangano ndi anthu a dziko lino, koma mudzaphwanye maguwa awo ansembe.’ Koma inu simunamvere lamulo langa. Chifukwa chiyani mwachita zimenezi?
3 I also warned you, ‘I will not drive them out before you, and they will be snares for you, and their gods will be traps for you.’”
Ndikukuwuzani tsopano kuti sindithamangitsa nzikazo pamene inu mukufika. Ndidzawasandutsa kukhala adani anu ndipo milungu yawo idzakhala ngati msampha kwa inu.”
4 After the angel of the Lord had explained this to all the Israelites, the people wept out loud.
Mngelo wa Mulungu atayankhula izi kwa Aisraeli, onse analira mokweza,
5 That's why they named the place Bokim, and they presented sacrifices there to the Lord.
ndipo anatcha malowo kuti Bokimu (kutanthauza kuti Olira). Pamenepo anapereka nsembe kwa Yehova.
6 After Joshua had dismissed the people, the Israelites went to take possession of the land, each to their allotted land.
Yoswa atawuza Aisraeli kuti achoke, iwo anapita kukatenga dzikolo, aliyense dera lake.
7 The people continued to worship the Lord throughout Joshua's life, and throughout the lifetimes of the elders who outlived him, those who had seen all the wonderful things that the Lord had done for Israel.
Anthuwo anatumikira Yehova masiku onse a moyo wa Yoswa. Atamwalira Yoswa, Aisraeli anatumikirabe Yehova nthawi yonse ya moyo wa akuluakulu amene anaona zazikulu zimene Yehova anawachitira.
8 Joshua, son of Nun, servant of the Lord, died at the age of one hundred and ten.
Yoswa mwana wa Nuni, mtumiki wa Yehova, anamwalira ali ndi zaka 110.
9 They buried him in Timnath-heres in the hill country of Ephraim, north of Mount Gaash, the land he had been allocated.
Ndipo anamuyika mʼmanda a mʼdziko lake, ku Timnati-Heresi mʼdziko la mapiri la Efereimu, kumpoto kwa phiri la Gaasi.
10 Once that generation had passed away, the generation that followed did not know the Lord, or what he had done for Israel.
Mʼbado onse utapita kukakhala ndi anthu a mtundu awo, kenaka panauka mʼbado wina umene sunadziwe Yehova ngakhale ntchito zazikulu zimene Yehova anachitira Aisraeli.
11 The Israelites did what was evil in the Lord's sight, and they worshiped the Baals.
Choncho Aisraeli anayamba kuchita zinthu zoyipa pamaso pa Yehova ndipo anatumikira Abaala.
12 They deserted the Lord, the God of their forefathers, who had led them out of Egypt. They followed other gods, bowing down in worship to the gods of the peoples around them, making the Lord angry.
Iwo anasiya Yehova Mulungu wa makolo awo, amene anawatulutsa ku Igupto. Ndipo anatsatira ndi kupembedza milungu yosiyanasiyana ya anthu amene anawazungulira. Motero Aisraeli anakwiyitsa Yehova.
13 They deserted the Lord and worshiped Baal and Ashtaroth idols.
Iwo anasiya Yehova ndi kumatumikira Baala ndi Asiteroti.
14 Because the Lord was angry with Israel he handed them over to invaders who plundered them. He sold them to their enemies all around—enemies they could no longer resist.
Yehova anapsera mtima Aisraeli ndipo anawapereka mʼmanja mwa anthu ofunkha amene ankasakaza zinthu zawo. Ndipo analola kuti adani awo owazungulira amene sanathenso kulimbana nawo, awagonjetse.
15 Whenever Israel went into battle, the Lord fought against them and defeated them, just as he had warned them and as he had vowed he would do. They were in a great deal of trouble.
Nthawi zonse Aisraeli ankati akapita ku nkhondo, Yehova amalimbana nawo kuti agonjetsedwe, monga ananenera molumbira kuti zidzaterodi. Choncho iwo anali pa mavuto aakulu.
16 Then the Lord provided them with judges, who saved them from their invaders.
Choncho Yehova anawawutsira atsogoleri amene ankawapulumutsa mʼmanja mwa anthu amene ankasakaza zinthu zawo.
17 But even so, they refused to listen to their judges, and prostituted themselves by following other gods, bowing down in worship to them. They quickly abandoned the way their forefathers had followed, and they did not obey the Lord's commandments as their forefathers had.
Komabe iwo sanawamvere atsogoleri awowo popeza ankapembedza milungu ina ndi kumayigwadira. Iwo anapatuka msangamsanga mu njira imene ankayendamo makolo awo. Iwo aja ankamvera malamulo a Yehova, koma mʼbado uwu ayi.
18 When the Lord provided Israel with judges over Israel, he was with each judge and saved the people from their enemies during that judge's lifetime, because the Lord felt sorry for his people, who groaned under their oppressors and persecutors.
Nthawi zonse Yehova akawautsira mtsogoleri, Iye amakhala naye, ndipo mtsogoleriyo ankawapulumutsa Aisraeliwo mʼmanja mwa adani awo mʼnthawi imene anali moyo. Yehova ankawamvera chisoni Aisraeli pamene ankabuwula chifukwa cha anthu owazunza ndi kuwasautsa.
19 But when the judge died, the people relapsed, and did worse things even than their forefathers, following other gods and worshiping them. They refused to give up what they were doing and held to their stubborn ways.
Koma nthawi zonse mtsogoleri akamwalira, Aisraeli ankabwerera mʼmbuyo. Iwo amadzisandutsa oyipa kupambana makolo awo popeza ankatsata milungu ina, kuyitumikira ndi kumayigwadira. Anakana kusiya makhalidwe awo oyipa ndi njira zawo zamakani.
20 As a result the Lord became angry with Israel and he told them, “Because this nation has broken the agreement I ordered their forefathers to obey, and has not paid attention to what I said,
Choncho Yehova anawapsera mtima Aisraeli ndipo anati, “Chifukwa mtundu uwu waswa pangano limene ndinakhazikitsa ndi makolo awo ndipo sanandimvere,
21 from now on I won't drive out before them any of the nations Joshua left when he died.
Inenso sindidzapirikitsanso mtundu uli wonse wa anthu amene Yoswa anawasiya pomwalira.
22 This is in order to use them to test Israel to see if they will keep the way of the Lord and follow it as their forefathers did.”
Ndidzatero kuti ndiwayese Aisraeli ndi kuona ngati adzasamala kuyenda mʼnjira ya Ine Yehova monga momwe ankachitira makolo awo.”
23 This is the reason why the Lord allowed those nations to remain, and didn't immediately drive them out by handing them over to Joshua.
Choncho Yehova anayileka mitundu imeneyi ndipo sanayithamangitse kapena kuyipereka mʼmanja mwa Yoswa.

< Judges 2 >