< Job 37 >
1 At this my heart trembles, beating rapidly within me!
“Mtima wanga ukulumphalumpha pa chimenechinso ndipo ukuchoka mʼmalo mwake.
2 Listen carefully to God's thunderous voice that rumbles as he speaks.
Tamverani! Tamverani kubangula kwa liwu lake, kugunda kumene kukuchokera mʼkamwa mwake.
3 He sends it across the heaven; his lightning flashes to the ends of the earth.
Iye amaponya chingʼaningʼani chake pansi pa thambo lonse ndipo amachitumiza ku dziko lapansi.
4 Then comes the roar of thunder, his majestic voice holding nothing back when he speaks.
Pambuyo pake kubangula kwake kumamveka. Iye amabangula ndi liwu lake laulemerero. Pamene wabangula, palibe chimene amalephera kuchita.
5 God's thunderous voice is wonderful! We can't comprehend the great things he does!
Liwu la Mulungu limabangula mʼnjira zambiri zodabwitsa Iye amachita zinthu zazikulu zimene sitingathe kuzimvetsa.
6 He tells the snow to fall and the rain to pour down on the earth.
Amalamula chisanu chowundana kuti, ‘Igwa pa dziko lapansi,’ ndipo amalamulanso mvula yamawawa kuti, ‘Khala mvula yamphamvu.’
7 By this he stops people working so that everyone can understand what he does.
Kuti anthu onse amene anawalenga athe kuzindikira ntchito yake. Iye amalepheretsa anthu kugwira ntchito zawo.
8 Even the animals take shelter and remain in their dens.
Zirombo zimakabisala ndipo zimakhala mʼmaenje mwawo.
9 The south wind blows in storms, while the north wind blows in cold weather.
Mphepo yamkuntho imatuluka ku malo ake, kuzizira kumatuluka mʼmphepo yamkunthoyo.
10 God's breath produces ice, freezing the surface of water solid.
Mpweya wa Mulungu umawunditsa madzi ndipo madzi a mʼnyanja amawuma kuti gwaa.
11 He fills the clouds with moisture; he scatters his lightning from them.
Iye amadzaza mitambo ndi madzi a mvula, amabalalitsa zingʼaningʼani zake kuchokera mʼmitambomo.
12 They swirl around under his control; they move over all the earth as he commands.
Mulungu amayendetsa mitamboyo mozungulirazungulira dziko lonse lapansi kuti ichite zonse zimene Iye akufuna pa dziko lapansi.
13 He does this to accomplish his will, either to discipline or to show his goodness.
Iye amagwetsa mvula kuti alange anthu, kapena kubweretsa chinyontho pa dziko lapansi kuti aonetse chikondi chake.
14 Listen to this, Job! Stop for a moment and consider the wonderful things God does.
“Abambo Yobu, tamvani izi; imani ndipo muganizire ntchito zodabwitsa za Mulungu.
15 Do you know how God controls the clouds, or makes his lightning flash from them?
Kodi mukudziwa momwe Mulungu amayendetsera mitambo ndi kuchititsa kuti kukhale zingʼaningʼani?
16 Do you know how clouds float in the sky—the wonderful work of him who knows everything.
Kodi mukudziwa momwe Mulungu amayalira mitambo, ntchito zodabwitsa za Iye amene ndi wanzeru zangwiro?
17 You know how your clothes drip with sweat when the south wind brings air that is hot and heavy.
Inu amene mʼzovala zanu mumatuluka thukuta pamene kunja kwatentha chifukwa cha mphepo yakummwera,
18 Can you hammer out the sky so it becomes like a molten mirror, as he does?
kodi mungathe kuthandizana naye kutambasula thambo limene ndi lolimba ngati chitsulo?
19 So why don't you teach us what to tell God? We cannot make our case because we are in the dark!
“Tiwuzeni ife zoti tikanene kwa Iye; sitingathe kufotokoza mlandu wathu chifukwa cha mdima umene uli mwa ife.
20 Should God be told that I want to speak? Anyone who wanted to would be destroyed!
Kodi nʼkofunika kumudziwitsa Mulungu kuti ndili naye mawu? Kodi kutero sikuchita ngati kupempha kuti ndiwonongeke?
21 After all, we can't look at the sun when it blazes brightly in the sky, after the wind has cleared away the clouds.
Tsopano munthu sangathe kuyangʼana dzuwa, ndi kunyezimira mlengalenga, kuwomba kwa mphepo kutachotsa mitambo yonse.
22 Out of the north God comes shining like gold, surrounded in awesome majesty.
Kuwala kwake kumaonekera cha kumpoto; Mulungu amabwera ndi ulemerero woopsa.
23 We cannot approach the Almighty for he is far beyond us in power and justice, and doing right.
Wamphamvuzonse sitingathe kumufikira pafupi ndi wa mphamvu zoposa; pa chiweruzo chake cholungama ndi mʼchilungamo chake chachikulu Iye sapondereza anthu ozunzika.
24 He does not act like a tyrant—no wonder people are in awe of him, though he does not value those who think they're wise.”
Nʼchifukwa chake anthu amamuopa kwambiri, kodi saganizira za onse amene amaganiza kuti ndi anzeru?”