< Isaiah 21 >

1 A message about the desert by the sea. Like storm winds passing through the Negev, something is coming from the desert, from a land of terror—
Uthenga wonena za chipululu cha mʼmbali mwa Nyanja. Ankhondo a ku Elamu ndi Mediya adzabwera ngati kamvuluvulu amene akuwomba modutsa mʼmbali ya nyanja, kuchokera ku chipululu, dziko lochititsa mantha.
2 a horrifying vision that has been explained to me. The betrayer still betrays; the destroyer still destroys. Elamites and Medes, go ahead, attack and lay siege to Babylon, for I'm putting a stop to all the pain it has caused.
Ine ndaona zinthu zoopsa mʼmasomphenya: Wonyenga akunyenga, wofunkha akufunkha komanso owononga akuwononga. Elamu, yambani nkhondo! Mediya, zingani mzinda! Ine ndidzathetsa mavuto onse amene anayambitsa Ababuloni.
3 As a result my body is filled with agony. I'm overwhelmed with pain, like the pain of a woman giving birth. I am confused by what I hear; I am distressed by what I see.
Chifukwa cha zimenezi thupi langa likunjenjemera ndi mantha, ndikumva ululu ngati wa mayi amene akubereka; ndikuvutika kwambiri ndi zimene ndikumva, ndathedwa nzeru ndi zimene ndikuziona.
4 My mind falters; I shake in panic. The night I looked forward to has become terrifying.
Mtima wanga ukugunda, ndipo ndikunjenjemera ndi mantha; chisisira chimene ndakhala ndikuchifuna chasanduka chinthu choopsa kwa ine.
5 They set the table, they spread out the rugs, they eat and drink… “Get up, officers! Prepare your shields for battle!”
Ankhondo a ku Elamu ndi Mediya akukonza matebulo, akuyala mphasa, akudya komanso kumwa! Mwadzidzidzi anamva mawu akuti, “Dzukani inu ankhondo, pakani mafuta zishango zanu!”
6 This is what the Lord told me: “Go! Have a lookout keep watch, and make sure he reports what he sees.
Zimene Ambuye akunena kwa ine ndi izi; “Pita, kayike mlonda kuti azinena zimene akuziona.
7 When he sees chariots coming pulled by pairs of horses, riders on donkeys and on camels, he should watch very carefully, paying close attention.”
Taonani, anthu akubwera ali pa akavalo ndipo akuyenda awiriawiri, okwera pa bulu kapena okwera pa ngamira, mlondayo akhale tcheru kwambiri.”
8 Then the lookout shouted “Sir, I've stood here on the watchtower day after day; night after night I've remained at my post.
Ndipo mlondayo anafuwula kuti, “Ambuye anga, tsiku ndi tsiku ndimakhala pa nsanja yolondera; Usiku uliwonse ndimakhala pa malo anga olondera.
9 Now look! A man in a chariot with a pair of horses is coming.” Then he said, “Babylon has fallen, has fallen! All the idols of its gods lie smashed on the ground!”
Taonani, uyo munthu akubwera atakwera pa galeta ali ndi gulu la akavalo. Mmodzi wa iwo akuti, ‘Babuloni wagwa, wagwa! Mafano onse a milungu yake agwa pansi ndipo aphwanyika!’”
10 My poor downtrodden people, so badly mistreated, I have told you what I have heard from the Lord Almighty, the God of Israel.
Inu anthu anga opunthidwa ndi kupetedwa ngati tirigu, ine ndikukuwuzani zimene ndamva ndikukuwuzani Uthenga wochokera kwa Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli.
11 A message about Edom. A voice is calling to me from Seir, asking, “Watchman, what time of night is it? Watchman, what time of night is it?”
Uthenga wonena za Duma: Munthu wina akundiyitana kuchokera ku Seiri kuti, “Iwe mlonda, usikuwu utha liti? Iwe mlonda, utha liti kodi usikuwu?”
12 The watchman replies, “Morning is coming, but the night is coming again soon. If you want to ask again, then come back and ask.”
Mlonda akuyankha kuti, “Kukucha, koma kudanso. Ngati ukufuna kufunsa, funsa tsopano; ndipo ubwerenso udzafunse.”
13 A message about Arabia. Caravans from Dedan, spend the night in the bushes.
Uthenga wonena za Arabiya: Inu anthu amalonda a ku Dedani, amene usiku mumagona mʼzithukuluzi za ku Arabiya,
14 People of Tema, take water to the thirsty, meet the refugees with food.
perekani madzi kwa anthu aludzu. Inu anthu a ku Tema perekani chakudya kwa anthu othawa nkhondo.
15 They're running away from a fierce battle, from swords, drawn swords, from bows and arrows.
Iwo akuthawa malupanga, lupanga losololedwa, akuthawa uta wokokakoka ndiponso nkhondo yoopsa.
16 This is what the Lord told me: “Within one year, just as a contract worker precisely counts years, all the glory of Kedar will be gone.
Zimene Ambuye akunena kwa ine ndi izi: “Chaka chimodzi chisanathe, potsata mmene amawerengera munthu waganyu, ulemerero wonse wa Kedara udzatheratu.
17 There will only be a few left of the archers, the warriors of Kedar.” The Lord, the God of Israel, has spoken.
Mwa anthu okoka uta, ankhondo a ku Kedara opulumuka adzakhala owerengeka.” Wayankhula ndi Yehova Mulungu wa Israeli.

< Isaiah 21 >