< Deuteronomy 27 >

1 Moses and the Israelite elders of Israel gave these instructions to the people: Keep all the commandments I am giving you today.
Mose ndi akuluakulu a Israeli analamula anthu kuti, “Sungani malamulo onse amene ndikukupatsani lero lino.
2 The day you cross the Jordan into the country the Lord your God is giving you, set up some large stones and paint them with whitewash.
Mukawoloka mtsinje wa Yorodani kulowa mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani, muyimiritse miyala ingapo ikuluikulu ndi kuyikulungiza.
3 Then write all these laws on them once you've crossed over to enter the country that the Lord your God is giving you, a land flowing with milk and honey, just as the Lord, the God of your forefathers, promised you.
Mulembepo mawu onse a malamulo amenewa pamene muwoloka kulowa mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani, dziko loyenda mkaka ndi uchi, monga momwe Yehova Mulungu wa makolo anu anakulonjezerani.
4 After you've crossed the Jordan, you are to set up these stones on Mount Ebal, having painted them with whitewash, as I've ordered you to do today.
Ndipo mukawoloka Yorodani muyimike miyala iyi pa Phiri la Ebala monga momwe ndikukulamulirani lero lino ndipo muyikulungize.
5 Also build a stone altar there to the Lord your God, an altar of stones. Don't use any stone tools in its construction.
Pamenepo mumange guwa lansembe la miyala la Yehova Mulungu wanu. Musagwiritse ntchito chida chilichonse chachitsulo pa miyalapo.
6 Build the altar of the Lord your God with uncut stones and sacrifice burnt offerings on it to the Lord your God.
Mumange guwa lansembe la Yehova Mulungu wanu ndi miyala yakutchire ndi kuperekerapo nsembe yopsereza kwa Yehova Mulungu wanu.
7 That is also where you are to sacrifice and eat your peace offerings, celebrating in the presence of the Lord your God.
Muperekerepo nsembe zopereka za chiyanjano, muzidye ndi kukondwera pamaso pa Yehova Mulungu wanu.
8 Write all these laws clearly on the stones.
Ndipo pa miyalapo mudzalembepo mawu onse a malamulo ndi malemba akuluakulu.”
9 Moses and the Levitical priests gave these orders to all the Israelites: “Be quiet, people of Israel, and listen! Today you have become the people of the Lord your God.
Kenaka Mose ndi ansembe, amene ndi Alevi anati kwa Aisraeli onse, “Khalani chete Aisraeli inu ndipo mumvetsere! Tsopano inu ndinu anthu a Yehova Mulungu wanu.
10 So obey what the Lord your God tells you, and follow commandments and regulations that I'm giving you today.”
Muzimvera Yehova Mulungu wanu ndi kutsata malamulo ake ndi malangizo ake omwe ndikukupatsani lero lino.”
11 That day Moses gave these orders to the people:
Tsiku lomwelo Mose analamula anthu kuti:
12 After you've crossed the Jordan, the following tribes are to stand on Mount Gerizim to bless the people: Simeon, Levi, Judah, Issachar, Joseph, and Benjamin.
Mukawoloka Yorodani, mafuko awa akayimirire pa Phiri la Gerizimu ndi kudalitsa anthu: Simeoni, Levi, Yuda, Isakara, Yosefe ndi Benjamini.
13 The following tribes are to stand on Mount Ebal for the curse: Reuben, Gad, Asher, Zebulun, Dan, and Naphtali.
Ndipo mafuko awa akayimirire pa Phiri la Ebala ndi kutchula matemberero: Rubeni, Gadi, Aseri, Zebuloni, Dani ndi Nafutali.
14 Then the Levites will shout in a loud voice so Israelite can hear:
Alevi adzayankhula mokweza kwa Aisraeli onse kuti:
15 “A curse on anyone who makes a carved image or a metal idol and worships it in secret. It's only an object that someone made, and it's offensive to the Lord!” Everyone says “Amen!”
“Ndi wotembereredwa munthu amene asema chifanizo kapena kupanga fano, ndi kuchiyika mobisa, pakuti chimenechi ndi chinthu chodetsedwa pamaso pa Yehova, ntchito za manja a anthu.”
16 “A curse on anyone who dishonors their father or mother.” Everyone says “Amen!”
“Ndi wotembereredwa munthu amene sachitira ulemu abambo ake kapena amayi ake.”
17 “A curse on anyone who moves their neighbor's boundary stone!” Everyone says “Amen!”
“Ndi wotembereredwa munthu amene amasuntha mwala wa malire wa mnzake.”
18 “A curse on anyone who allows a blind man to wander in the road!” Everyone says “Amen!”
“Ndi wotembereredwa munthu amene amasocheretsa munthu wosaona pa msewu.”
19 “A curse on anyone who doesn't treat foreigners, the orphans, and widows fairly!” Everyone says “Amen!”
“Ndi wotembereredwa munthu amene sachitira chilungamo mlendo, ana amasiye kapena mkazi wamasiye.”
20 “A curse on any man who sleeps with his father's wife, for he has disgraced his father!” Everyone says “Amen!”
“Ndi wotembereredwa munthu amene agonana ndi mkazi wa abambo ake pakuti iye sachitira ulemu pogona pa abambo ake.”
21 “A curse on anyone who has sex with any animal!” Everyone says “Amen!”
“Ndi wotembereredwa munthu amene achita chigololo ndi nyama ya mtundu uli wonse.”
22 “A curse on any man who sleeps with his sister, the daughter of his father or the daughter of his mother!” Everyone says “Amen!”
“Ndi wotembereredwa munthu amene agonana ndi mlongo wake, mwana wamkazi wa abambo ake kapena mwana wamkazi wa amayi ake.”
23 “A curse on any man who sleeps with his mother-in-law!” Everyone says “Amen!”
“Ndi wotembereredwa munthu amene agonana ndi apongozi ake.”
24 “A curse on anyone who secretly attacks his neighbor!” Everyone says “Amen!”
“Ndi wotembereredwa munthu amene apha mnzake mwachinsinsi.”
25 “A curse on anyone who accepts a bribe to kill someone who's innocent!” Everyone says “Amen!”
“Ndi wotembereredwa munthu amene alandira chiphuphu kuti aphe munthu wosalakwa.”
26 “A curse on anyone who doesn't carefully obey all these laws by keeping them!” Everyone says “Amen!”
“Ndi wotembereredwa aliyense amene sachita kapena sasunga mawu a malamulo awa.”

< Deuteronomy 27 >