< Deuteronomy 11 >

1 Love the Lord your God and do everything he says—his rules, regulations, and commandments.
Muzikonda Yehova Mulungu wanu ndipo nthawi zonse muzitsata zimene Iyeyo anakulamulani, malangizo, zikhazikitso ndi malamulo ake.
2 You should realize that it's not your children who have experienced the Lord your God's discipline. It was you who saw his greatness, his power and strength;
Lero kumbukirani kuti si ana anu amene anaona ndi kulawa chilango cha Yehova Mulungu wanu: ukulu wake, dzanja lake lamphamvu, mkono wake wotambasuka;
3 and his miracles. You saw what he did to Pharaoh king of Egypt and his whole country.
zizindikiro zozizwitsa zimene anazionetsa ndi zinthu zimene anazichita mʼkati mwa Igupto, Farao mfumu ya Igupto ndi kwa dziko lake lonse;
4 You saw what he did to the Egyptian army and its horses and chariots when he swept them away in the Red Sea, drowning them as they chased after you. The story hasn't changed!
zimene Iye anachita kwa gulu lankhondo la Aigupto, kwa akavalo ndi magaleta awo, mmene Iye anawamizira ndi madzi a mu Nyanja Yofiira pamene amakuthamangitsani, ndi mmene Yehova anawagonjetsera kufikira lero.
5 You saw what he did for you in the desert until you arrived here.
Si ana anu amene anaona zimene Iye anakuchitirani mʼchipululu kufikira pamene munafika pa malo anu,
6 You saw what he did, right there among you, to Dothan and Abiram, the sons of Eliab of the tribe of Reuben, when the earth split open and swallowed them down—their families, their tents, and all their animals.
ndi zimene anachitira Datani ndi Abiramu, ana aamuna a Eliabu mwana wa Rubeni, pamene nthaka inatsekula pakamwa pake pakati pa Aisraeli onse ndi kuwameza pamodzi ndi katundu wawo, matenti awo ndi chilichonse chawo.
7 You saw with your own eyes all the amazing things that the Lord has done.
Koma ndinuyo amene munaona ntchito zonse zikuluzikulu zimenezi Yehova anakuchitirani.
8 So you must keep every commandment I am giving you today That way you will have the strength to enter and take over the country that you are crossing the Jordan to have as your own,
Tsono muzisunga malamulo onse amene ndikukupatsani lero kuti mukhale ndi mphamvu ndi kuti mupite kukalanda mʼdziko limene mwakhala pangʼono kulowamo mukawoloka Yorodani,
9 You will also have long lives in the country that the Lord promised to give your forefathers and their descendants, a land flowing with milk and honey.
ndiponso kuti mukhalitse mʼdziko limene Yehova analumbira kupatsa makolo anu ndi zidzukulu zawo, lomwe ndi dziko loyenda mkaka ndi uchi.
10 The country you're entering to occupy isn't like the country of Egypt that you've come from. There you had to sow your seed and work hard irrigating the ground, like taking care of a vegetable garden.
Dziko limene mukukalanda ndi kulowamo silokhala ngati dziko la ku Igupto kumene mukuchokera ayi, kuja mumadzala mbewu ndi kumathirira ndi mapazi anu ngati ku dimba.
11 But here in the country that you are crossing the Jordan to take over is a land of mountains and valleys that receives plenty of rain
Koma dziko limene mukalande mukawoloka Yorodani ndi dziko la mapiri ndi zigwa, dziko limene limalandira mvula kuchokera kumwamba.
12 It is a land that the Lord your God takes care of. The Lord your God it is always watching over it, all year long.
Ili ndi dziko limene Yehova Mulungu wanu amalisamalira. Maso a Yehova Mulungu wanu amaliyangʼanira nthawi zonse kuchokera ku mayambiriro a chaka mpaka kumapeto kwake.
13 So if you pay careful attention to keep the commandments I'm giving you today, if you love the Lord your God and to worship with all your mind and with all your being,
Choncho mukasunga mokhulupirika malamulo amene ndikukupatsani lero lino, kukonda Yehova Mulungu wanu ndi kumutumikira Iyeyo ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse,
14 then I will send rain for your land at the right time, rain in autumn and spring, so that you can harvest your grain, new wine, and olive oil.
pamenepo ndidzatumiza mvula mʼdziko mwanu pa nthawi yake mʼnyengo ya dzinja ndi chilimwe, kuti mudzakolole tirigu wambiri ndi kuti mudzakhale ndi vinyo watsopano ndi mafuta.
15 I will also provide grass in the fields for your livestock. You will have more than enough to eat.
Ndidzakupatsani udzu mʼminda mwanu woti muzidzadyetsera ngʼombe zanu ndipo inuyo mudzadya ndi kukhuta.
16 But make sure you're not that you're not fooled into worshiping and bowing down to other gods,
Dzisamalireni nokha, kuopa kuti mungakopeke mtima ndi kubwerera mʼmbuyo kuyamba kutumikira milungu ina ndi kumayigwadira.
17 or the Lord will become angry with you. He won't send any rain, and the land won't produce any crops, and you will soon die, even in the good land that the Lord is giving you.
Mukatero Yehova Mulungu wanu adzakukwiyirani kwambiri, nadzaletsa thambo kuti lisabweretsenso mvula ndipo dziko silidzapereka zokolola. Choncho mudzawonongeka msanga mʼdziko limene Yehova akukupatsani.
18 Focus your minds on the words that I'm saying. Tie them on your hands as reminders and put them on your foreheads as well.
Sungani mawu amenewa mu mtima mwanu ndi mʼmaganizo mwanu, muwamangirire pa mikono yanu ndipo muwayike pamphumi panu.
19 Teach them to your children and talk about them when you're at home and when you're traveling, when you lie down and when you get up.
Mawuwa muziphunzitsa ana anu, muzikamba za iwo pamene mukhala pansi mʼnyumba zanu, pamene mukuyenda mʼnjira, pamene mugona ndi pamene mukudzuka.
20 Write them on the doorposts of your homes and on your gates,
Muwalembe pa mphuthu za nyumba zanu ndi pa zipata zanu,
21 so that as long as the earth lasts, you and your children may have long lives in the country the Lord promised to give your forefathers.
kuti inu ndi ana anu mukhale mʼdziko limene Yehova analumbira kupatsa makolo anu mpaka kalekale monga umakhalira mlengalenga pamwamba pa dziko.
22 If you are careful to keep all these commandments I am giving you to follow, if you love the Lord your God and follow all his ways, and hold onto him,
Mukatsatira mosamalitsa malamulo amene ndikukupatsaniwa, kukonda Yehova Mulungu wanu, kuyenda mʼnjira zake zonse ndi kumugwiritsitsa Iye
23 then the Lord will drive out all these nations ahead of you, and you will take over the country from nations that are greater and stronger than you.
Yehova adzapirikitsa mitundu ina yonseyi inu musanafike ndipo mudzagonjetsa mitundu ikuluikulu ndi yamphamvu kuposa inu.
24 Everywhere you walk will belong to you. Your territory will extend from the desert all the way to Lebanon, and from the Euphrates River to the Mediterranean Sea.
Malo aliwonse amene mudzaponda adzakhala anu: dziko lanu lidzachokera ku chipululu mpaka ku Lebanoni, ndi ku Mtsinje wa Yufurate mpaka ku nyanja ya kumadzulo.
25 No one will be able to withstand you; the Lord your God will make everyone living there absolutely terrified of you wherever you go, just as he promised you.
Palibe munthu amene adzalimbana nanu. Monga analonjezera, Yehova adzachititsa kuti anthu onse mʼdziko limene mukupitalo adzachite nanu mantha ndi kukuopani.
26 Look! Today I'm placing before you both a blessing and a curse.
Taonani, lero ndikuyika dalitso ndi temberero pakati panu,
27 You will receive a blessing if you obey the commandments of the Lord your God that I'm giving you today.
dalitso ngati mumvera malamulo a Yehova Mulungu wanu amene ndikukupatsani lero.
28 But you will receive a curse if you disobey the commandments of the Lord your God and don't keep to the path I'm ordering you to follow today by worshiping some other unknown gods.
Temberero ngati simumvera malamulo a Yehova Mulungu wanu ndi kupatuka pa njira imene ndikulamulirani lero potsata milungu ina imene simunayidziwe.
29 When the Lord your God takes you into the country you are going in to occupy, announce the blessing on Mount Gerizim and the curse on Mount Ebal.
Yehova Mulungu wanu akakakufikitsani mʼdziko mukukalandalo kuti mulowemo mukanene za madalitso pa Phiri la Gerizimu, ndi za matemberero pa Phiri la Ebala.
30 (These mountains are to the west of the Jordan, in the country of the Canaanites who live in the Arabah near Gilgal, beside the oaks of Moreh.)
Monga mudziwa, mapiriwa ali kutsidya kwa Yorodani, kumadzulo kolowera dzuwa, kufupi ndi mitengo ya thundu ya More, mʼdziko la Akanaani aja okhala ku Araba moyangʼanana ndi Giligala.
31 Shortly you're going to cross the Jordan to enter and occupy the country the Lord your God is giving you. When you take it over and settle there,
Mwatsala pangʼono kuwoloka Yorodani kuti mulowe ndi kutenga dziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani. Mukadzalitenga dzikolo ndi kukhalamo,
32 make sure you follow all the rules and regulations that I'm giving you today.
mudzaonetsetse kuti mukumvera malangizo ndi malamulo amene ndikukuwuzani lero.

< Deuteronomy 11 >