< 1 Kings 14 >

1 It was at that time that Abijah, Jeroboam's son, fell ill.
Pa nthawi imeneyo Abiya mwana wa Yeroboamu anayamba kudwala,
2 So Jeroboam told his wife, “Please go and disguise yourself so nobody will know you're Jeroboam's wife. Then go to Shiloh and look for Ahijah the prophet. He was the one who told me I would become king over this people.
ndipo Yeroboamu anati kwa mkazi wake, “Nyamuka ndipo udzibise kuti usadziwike kuti ndiwe mkazi wa Yeroboamu, ndipo upite ku Silo. Kumeneko kuli mneneri Ahiya amene anandiwuza kuti ndidzakhala mfumu ya anthu awa.
3 Take with you ten loaves of bread, some cakes, and a jar of honey for him. He will explain to you what will happen to the boy.”
Utenge buledi khumi, makeke ndiponso botolo la uchi ndipo upite kwa mneneriyo. Iye adzakuwuza zimene zidzamuchitikire mwanayu.”
4 Jeroboam's wife did as she was told. She got up and went to Ahijah's house in Shiloh. Ahijah could not see—he had become blind because of his age.
Choncho mkazi wa Yeroboamu anadzibisa ndipo anapita ku nyumba ya Ahiya ku Silo. Tsono Ahiya sankatha kupenya bwino. Ankangoona kuti mbuu chifukwa cha ukalamba.
5 But the Lord had told Ahijah, “Look, Jeroboam's wife is coming to ask you about her son, because he's ill. This is what you are to tell her, because she'll come in disguise.”
Koma Yehova nʼkuti atamuwuza Ahiya kuti, “Taona, mkazi wa Yeroboamu akubwera kudzafunsa iwe za mwana wake pakuti akudwala, ndiye udzamuyankhe zakutizakuti mkaziyo. Iye akafika, adzadzibisa.”
6 So as soon as Ahijah heard her footsteps at the door, he called out, “Come in, wife of Jeroboam! Why do you bother coming in disguise? I have been given some bad news for you.
Tsono Ahiya atamva mgugu wa mapazi ake pa khomo, anati, “Lowa, iwe mkazi wa Yeroboamu. Bwanji ukudzibisa? Ine ndatumidwa kuti ndikuwuze nkhani yoyipa.
7 Go and tell Jeroboam this is what the Lord, the God of Israel, says: I picked you from the masses and I made you ruler over my people Israel.
Pita, kamuwuze Yeroboamu kuti Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ine ndinakukweza pakati pa anthu ndipo ndinakuyika kukhala mtsogoleri wa anthu anga Aisraeli.
8 I took the kingdom from the house of David and gave it to you. But you were not like my servant David, who kept my commandments and was totally committed to following me, only doing what was right in my sight.
Ndinachotsa ufumu ku nyumba ya Davide ndi kuwupereka kwa iwe, koma iwe sunafanane ndi mtumiki wanga Davide, amene ankasunga malamulo anga ndi kunditsata Ine ndi mtima wake wonse, kuchita zolungama zokhazokha pamaso panga.
9 You have done more evil than all those who lived before you. You have gone and made other gods for yourself, idols made of molten metal that made me angry. You have tossed me aside.
Ndipo iwe wachita zoyipa kupambana onse amene analipo kale. Wadzipangira milungu ina, mafano a zitsulo. Iweyo wandikwiyitsa ndipo wandiwukira.
10 Now pay attention, because as a result of this I am going to bring disaster on the house of Jeroboam. I will totally exterminate every one of your descendants in Israel, whether slave or free. I will burn the house of Jeroboam like a man burning refuse until it's all gone.
“‘Choncho taona, ndidzabweretsa masautso pa nyumba ya Yeroboamu. Ndipo ndidzawononga munthu wamwamuna aliyense wa pa banja lako, kapolo pamodzi ndi mfulu yemwe mʼdziko la Israeli. Ndidzatentha nyumba ya Yeroboamu monga mmene munthu amatenthera ndowe mpaka yonse kutheratu.
11 Those of Jeroboam's family who die in the town will be eaten by dogs, and those who die in the countryside will be eaten by birds. For the Lord has spoken.
Agalu adzadya aliyense wa banja la Yeroboamu amene adzafere mu mzinda, ndipo mbalame zamlengalenga zidzadya iwo amene adzafere ku thengo, pakuti Yehova watero!’
12 As for you, get up and go home. As soon as you arrive in the city, the child will die.
“Ndipo iwe nyamuka, bwerera ku nyumba kwako. Phazi lako likadzangoponda mu mzindamo, mwanayo adzamwalira.
13 All of Israel will mourn for him, and they will bury him. He alone of Jeroboam's family will be buried in a tomb because only in him has the Lord, the God of Israel found anything good—of the whole family of Jeroboam.
Aisraeli onse adzalira maliro ake ndi kumuyika mʼmanda. Ndi yekhayo wa banja la Yeroboamu amene adzayikidwe mʼmanda, pakuti ndi mwa iye yekha mmene Yehova Mulungu wa Israeli wapezamo kanthu kabwino.
14 The Lord will choose for himself a king to rule over Israel who will destroy the house of Jeroboam. This is starting to happen even now!
“Koma Yehova adzadzisankhira yekha mfumu yolamulira Israeli imene idzawononga banja la Yeroboamu. Tsiku lake ndi lero! Ndati chiyani? Inde, ndi lero lomwe lino.
15 The Lord will strike Israel like a reed jerked to and fro by the water. He will pull up Israel by the roots from this good land that he gave their forefathers and scatter them beyond the Euphrates, because they have made their pagan Asherah poles, making the Lord angry.
Ndipo Yehova adzakantha Israeli, kotero kuti adzakhala ngati bango logwedera pa madzi. Iye adzazula Israeli mʼdziko labwino limene analipereka kwa makolo ake ndi kuwamwazira kutsidya kwa mtsinje wa Yufurate, chifukwa anakwiyitsa Yehova pamene anapanga mafano a Asera.
16 He will abandon Israel because of the sins of Jeroboam, those that he committed himself, and those he made Israel commit.”
Ndipo Iye sadzasamalanso Israeli chifukwa cha machimo amene anachita Yeroboamu ndi kuchimwitsa nawo Israeli.”
17 Jeroboam's wife got up and left for Tirzah. As soon as she stepped through the doorway of her home, the boy died.
Tsono mkazi wa Yeroboamu anayimirira nachoka kupita ku Tiriza. Atangoponda pa khonde la nyumba yake, mwana uja anamwalira.
18 All of Israel buried him and mourned for him, just as the Lord had said through his servant Ahijah the prophet.
Aisraeli anamuyika mʼmanda, ndipo onse analira maliro ake, monga momwe Yehova ananenera kudzera mwa mtumiki wake, mneneri Ahiya.
19 The rest of what Jeroboam did, how he engaged in warfare and how he reigned, they are recorded in the Book of Chronicles of the Kings of Israel.
Ntchito zina pa nthawi ya ulamuliro wa Yeroboamu, nkhondo zake ndi mmene ankalamulirira zinalembedwa mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli.
20 Jeroboam reigned for twenty-two years, and then he died. His son Nadab succeeded him as king.
Iye analamulira zaka 22 ndipo anamwalira nayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake. Ndipo Nadabu mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
21 Rehoboam, son of Solomon, reigned in Judah. He was forty-one when he became king, and he reigned seventeen years in Jerusalem, the city the Lord had chosen from all the tribes of Israel where he would be honored. The name of his mother was Naamah the Ammonite.
Rehobowamu mwana wa Solomoni anali mfumu ya ku Yuda. Iye analowa ufumu ali ndi zaka 41, ndipo analamulira zaka 17 ku Yerusalemu, mzinda umene Yehova anawusankha pakati pa mafuko a Israeli kuti ayikemo Dzina lake. Amayi ake anali Naama, wa ku Amoni.
22 Judah did what was evil in the Lord's sight, and because of the sins they committed they made his jealous anger even greater than all their fathers had done.
Anthu a ku Yuda anachita zoyipa pamaso pa Yehova kupambana mmene anachitira makolo awo ndipo Yehova anawakwiyira.
23 They also set up for themselves high places, sacred pillars, and Asherah poles on every high hill and under every green tree.
Iwonso anadzipangira malo opembedzerapo mafano pa chitunda chilichonse ndi kuyimika miyala ya chipembedzo ndi mitengo ya Asera pa mtengo uliwonse wa masamba ambiri.
24 There were even cult prostitutes in the land. They followed all the disgusting practices of the nations that the Lord had driven out before the Israelites.
Mʼdzikomo munalinso amuna ochita zachiwerewere mwa chipembedzo. Anthu ankachita zonyansa zonse za anthu a mitundu ina imene Yehova anayipirikitsa asanafike Aisraeli.
25 In the fifth year of King Rehoboam's reign, Shishak, king of Egypt, attacked Jerusalem.
Chaka chachisanu cha ufumu wa Rehobowamu, Sisaki, mfumu ya Igupto, anadzathira nkhondo Yerusalemu.
26 He took the treasures of the Lord's Temple and the royal palace. He took everything, including all the gold shields Solomon had made.
Ananyamula chuma cha ku Nyumba ya Yehova ndiponso chuma cha ku nyumba ya mfumu. Anatenga chilichonse, ngakhalenso zishango zonse zagolide zimene Solomoni anapanga.
27 So King Rehoboam made bronze shields to replace them and handed them over to the captains of the guard to look after. They stood on duty at the entrance to the royal palace.
Ndipo Mfumu Rehobowamu anapanga zishango zamkuwa mʼmalo mwake, nazipereka mʼmanja mwa olamulira alonda a pa khomo pa nyumba ya mfumu.
28 Whenever the king went to the Lord's Temple, the guards would carry the shields. Afterwards they returned them to the guardroom.
Nthawi zonse mfumu ikamapita ku Nyumba ya Yehova, alonda ankanyamula zishangozo, kenaka ankazisunga mʼchipinda cha alonda.
29 The rest of what happened in Rehoboam's reign and everything that he did are recorded in the Book of Chronicles of the Kings of Judah.
Tsono ntchito zina za Rehobowamu ndi zina zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
30 Rehoboam and Jeroboam were always at war with each other.
Panali nkhondo zosalekeza pakati pa Rehobowamu ndi Yeroboamu.
31 Rehoboam died and was buried with his ancestors in the City of David. The name of his mother was Naamah the Ammonite. His son Abijam succeeded him as king.
Ndipo Rehobowamu anamwalira nayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu mzinda wa Davide. Amayi ake anali Naama wa ku Amoni. Ndipo Abiya analowa ufumu mʼmalo mwa abambo ake.

< 1 Kings 14 >