< Jeremia 48 >

1 To kuom Moab: Ma e gima Jehova Nyasaye Maratego, ma Nyasach Israel wacho: “Mano kaka nobed malit ne Nebo, nimar enokethe. Kiriathaim nokuod wiye kendo enomake; kar pondogi nobed kama inyiero kendo nomuke.
Ponena za Mowabu: Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, “Tsoka kwa mzinda wa Nebo, chifukwa wawonongedwa. Mzinda wa Kiriyataimu wachititsidwa manyazi ndipo wagonjetsedwa; linga lichititsidwa manyazi ndipo lagumulidwa.
2 Pak mar Moab ok nobedi kendo; ji nochan kethruokne ei Heshbon kagiwacho kama: ‘Biuru, watiek pinyni.’ Yaye joma odak Madmen, un bende ligangla nolawu mulingʼ thii.
Palibenso amene akutamanda Mowabu; ku Hesiboni anthu anamupanganira zoyipa: ‘Bwerani, tiyeni timuwonongeretu kuti asakhalenso mtundu wa anthu.’ Inunso anthu a ku Madimena, adzakukhalitsani chete; ankhondo adzakupirikitsani.
3 Winj ywak moa Horonaim, ywak mar duwruok maduongʼ gi kethruok.
Tamvani mfuwu wa anthu a ku Horonaimu. Iwo akulira kuti, ‘Kusakazika ndi kuwonongeka kwakukulu.’
4 Moab nokethi; nyithinde matindo noywagre.
Mowabu wawonongeka; ana ake angʼonoangʼono akulira kwambiri.
5 Giidho ka giluwo yo madhi Luhith, gi ywak malit ka gidhi; e yo maridore kadhi Horonaim kendo ywak malit mar kethruok winjore.
Anthu akukwera chikweza cha ku Luhiti, akulira kwambiri pamene akupita. Kulira chifukwa cha chiwonongeko kukumveka pa njira yotsikira ku Horonaimu.
6 Ringuru! Ringuru ukony ngimau; muchal gi bungu manie thim!
Thawani! Dzipulumutseni; khalani ngati mbidzi ya mʼchipululu.
7 Nikech ugeno kuom timbeu kod mwandu mau, un bende nomaku, kendo Kemosh noter e twech, kanyakla gi jodolo mage kod jotelo mage.
Popeza inu munkadalira ntchito zanu ndi chuma chanu, nanunso mudzatengedwa ukapolo, ndipo Kemosi adzapita ku ukapolo, pamodzi ndi ansembe ake ndi akuluakulu ake.
8 Jaketh gik moko nobi e dala ka dala kendo onge dala ma notony. Holo noum kendo got mar mesa nomuki, nikech Jehova Nyasaye osewacho.
Wowononga adzabwera ndi kusakaza mzinda uliwonse, ndipo palibe mzinda umene udzapulumuke. Chigwa chidzasanduka bwinja ndipo malo athyathyathya a pamwamba pa phiri adzawonongedwa monga Yehova wayankhulira.
9 Ket chumbi kuom Moab, nimar enotieke; miechgi nodongʼ gunda, maonge ngʼama nodagi eigi.
Mtsineni khutu Mowabu chifukwa adzasakazika; mizinda yake idzasanduka mabwinja, wopanda munthu wokhalamo.
10 “Okwongʼ ngʼat mayom yom e tich Jehova Nyasaye! Okwongʼ ngʼat ma okano liganglane ma ok ochwerogo remo!
“Wotembereredwa munthu amene amagwira ntchito ya Yehova monyinyirika! Wotembereredwa munthu amene amaletsa lupanga lake kupha anthu!
11 “Moab oseyweyo chakre tin-ne, ka divai mowe mos e aguche, ma ok ool koa ei agulu achiel kiloko machielo kendo pod ok odhi e twech. Omiyo ndhathe pod nikare, kendo tik mare ok olokore.”
“Mowabu wakhala pa mtendere kuyambira ubwana wake, ngati vinyo wokhazikika pa masese ake, osapungulidwa kuchoka mu mtsuko wina kuthira mu mtsuko wina; iye sanatengedwepo ukapolo. Nʼchifukwa chake kukoma kwake nʼkomwe kuja ndipo fungo lake silinasinthe.
12 Jehova Nyasaye wacho niya, “Kinde biro, ma anaor ji manopuke oko, kendo gini ole oko; giniwe agulni mage nono kendo toyo agulni mage.
Nʼchifukwa chake masiku akubwera,” akutero Yehova, “pamene ndidzatuma anthu amene amakhuthula vinyo mʼmitsuko ndipo adzamukhutula; adzakhuthula vinyo yense mitsuko yake pambuyo pake nʼkuphwanya mitsukoyo.
13 Eka Moab wiye nokuodi gi Kemosh, mana kaka od Israel wiye nokuot, kane gin-gi geno kuom Bethel.
Pamenepo Mowabu adzachita manyazi ndi Kemosi, monga momwe Aisraeli anachitira manyazi ndi Beteli amene ankamukhutulira.
14 “Ere kaka inyalo wacho ni, ‘Wan jokedo, ji mathuondi maroteke e lweny’?”
“Kodi munganene bwanji kuti, ‘Ife ndife asilikali. Ife ndife ngwazi, anthu amphamvu pa nkhondo?’
15 Ruoth, ma nyinge Jehova Nyasaye Maratego wacho niya, “Moab nokethi kendo mier mage nomonji; yawuote mabeyo noter e kar nek.
Owononga Mowabu ndi mizinda yake abwera ndipo ankhondo adzalowa mʼmidzi yake; anyamata ake okongola apita kukaphedwa,” ikutero Mfumu, imene dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.
16 Podho mar Moab osechopone; masichene nobi mapiyo.
Kugwa kwa Mowabu kuli pafupi; masautso ake akubwera posachedwa.
17 Ywageuru, un jogo duto modak machiegni kode, un jogo duto mongʼeyo humbe; wachuru ni, ‘Mano kaka otur odunga mar loch maratego, mano kaka otur ludh duongʼ!’
Mulireni kwambiri, inu nonse amene mwamuzungulira, inu nonse amene mumadziwa za kutchuka kwake; nenani kuti, “Taonani momwe yathyokera ndodo yamphamvu yaufumu ija, taonani momwe ndodo yaulemu yathyokera!”
18 “Auru malo e duongʼu ulor piny kendo ubedi e lowo motwo, yaye jodak mar Nyar Dibon, nimar ngʼama oketho Moab nobi mondo oked kodu, kendo otiek miechu madongo mochiel motegno gohinga.
“Tsikani pa ulemerero wanu ndipo khalani pansi powuma, inu anthu okhala ku Diboni, pakuti wowononga Mowabu wabwera kudzamenyana nanu, wasakaza mizinda yanu yotetezedwa.
19 Chunguru e bath yo kendo ungʼi, un joma odak Aroer. Penj dichwo maringo kod dhako maringo, ni, Angʼo mosetimore?
Inu amene mumakhala ku Aroeri, imani mʼmbali mwa msewu ndi kumaonerera. Funsani mwamuna amene akuthawa ndiponso mkazi amene wapulumuka, afunseni kuti, ‘Kodi chachitika nʼchiyani?’”
20 Okuod wi Moab, nimar ongʼinje matindo tindo. Dengi kendo iywag matek! Land e Arnon ni Moab okethi.
Iwo adzayankha kuti, “Mowabu wachititsidwa manyazi, pakuti wasakazika. Lirani mwachisoni ndipo fuwulani! Lengezani ku mtsinje wa Arinoni kuti Mowabu wawonongedwa.
21 Ngʼado bura osebiro e got mar mesa kuom Holon, Jaza kod Mefath,
Chiweruzo chabwera ku mizinda ya ku mapiri, ndiyo Holoni, Yaza, Mefaati,
22 kuom Dibon, Nebo kod Beth Diblathaim,
Diboni, Nebo, Beti-Dibilataimu,
23 kuom Kiriathaim, Beth Gamul kod Beth Mion,
Kiriyataimu, Beti-Gamuli, Beti-Meoni,
24 kuom Kerioth gi Bozra, kuom mier duto mag Moab, man mabor kod mago man machiegni.
Keriyoti ndi Bozira ndi mizinda yonse ya Mowabu, yakutali ndi yapafupi yomwe.
25 Tung Moab ongʼad oko; bade otur,” Jehova Nyasaye ema owacho.
Mphamvu za Mowabu zawonongeka; mkono wake wathyoka,” akutero Yehova.
26 “Kete omer, nimar osetamore winjo Jehova Nyasaye. We Moab odwanyre e ngʼokne; we obed gima ijaro.
“Muledzeretseni Mowabu, chifukwa anadzikuza powukira Yehova. Mulekeni Mowabu avivinizike mʼmasanzi ake; mulekeni akhale chinthu chomachiseka.
27 Donge Israel ema ne ijaro? Bende nomake e dier jokwoge, ma itengʼone wiyi gi achaya sa moro amora miwuoyo kuome?
Kodi suja Israeli anali kwa iwe ngati chinthu chomachiseka? Kodi Israeli anapezeka pakati pa akuba kuti nthawi zonse poyankhula za iye, iwe uzimupukusira mutu momunyoza?
28 Jwangʼuru miechu kendo udagi e kind lwendni, un joma odak Moab. Chaluru ka akuch odugla maloso ode e dho rogo.
Inu amene mumakhala ku Mowabu, siyani mizinda yanu ndi kukakhala pakati pa matanthwe. Khalani ngati nkhunda imene imamanga chisa chake pa khomo la phanga.
29 “Wasewinjo sunga mar Moab, sungane mokadhore gi miriambo, sunga mare gi jendeke mare kod ngʼayi mar chunye.”
“Tamva za kunyada kwa Mowabu, kunyada kwake nʼkwakukulu. Ndi wodzitama, wonyada ndi wodzitukumula. Ali ndi mtima wodzikweza.
30 Jehova Nyasaye wacho niya, “Angʼeyo mirimbe to oonge tiende, kendo ngʼayi mage ok nyal gimoro.
Ine ndikuzidziwa ntchito zake, akutero Yehova. Ntchitozo ndi nʼzosapindulitsa kanthu.
31 Emomiyo aywak kadengo kuom Moab, nimar kuom Moab duto aywak, aywago jo-Kir Hareseth.
Nʼchifukwa chake ndidzamulira Mowabu, ine ndikulira chifukwa cha anthu onse a ku Mowabu, ndikubuwula chifukwa cha anthu a ku Kiri Heresi.
32 Aywagou, kaka Jazer ywak, yaye mzabibu mag Sibma. Bedeni kar machopo e nam; negichopo nyaka e nam mar Jazer. Jaketh gik moko osepodho e olembegi mochiek kod olemo mar mzabibu.
Ndikukhetsa misozi chifukwa cha inu, kupambana momwe ndinalirira Yazeri. Inu anthu a ku Sibina muli ngati mipesa imene nthambi zake zatambalala mpaka ku Nyanja; zafika mpaka ku nyanja ya Yazeri. Wowononga wasakaza zipatso zake zachilimwe ndi mpesa.
33 Ilo gi mor orumo e puoth olembe kod puothe mag Moab. Asechungo chwer mar divai koa e kuonde mibiyogie; onge ngʼama nyonogi gi koko mar ilo. Kata obedo ni nitiere koko, ok gin koko mar ilo.
Chimwemwe ndi chisangalalo zatha ku minda ya zipatso ya ku Mowabu. Ndaletsa kuchucha kwa vinyo mopsinyira mphesa; palibe amene akufuwula mokondwa akamapsinya mphesa. Ngakhale kufuwula kulipo, koma sikufuwula kwa chimwemwe.
34 “Dwond ywak mag-gi winjore koa Heshbon nyaka Eleale gi Jahaz, koa Zoar nyaka chop Horonaim gi Eglath Shelishiya, nimar kata pige mag Nimrim bende osetwo.
“A ku Hesiboni ndi Eleali akulira ndipo mfuwu wawo ukumveka mpaka ku Yahazi, kuchokera ku Zowari mpaka ku Horonaimu ndi ku Egilati Selisiya. Ngakhale madzi a ku Nimurimu aphwa.
35 E Moab anatiek jogo matimo misengini e kuonde motingʼore gi malo, kendo ma wangʼo ubani ne nyisechegi,” Jehova Nyasaye ema owacho.
Ndidzawaletsa anthu a ku Mowabu kupereka nsembe mʼmalo awo opembedzera ndi kufukiza lubani kwa milungu yawo,” akutero Yehova.
36 “Omiyo chunya ywagorene Moab ka asili; oywagore ka asili ne jo-Kir Hareseth. Mwandu mane giyudo oserumo.
“Nʼchifukwa chake mtima wanga ukulirira Mowabu ngati chitoliro. Mtima wanga ukulirira anthu a ku Kiri Heresi ngati chitoliro chifukwa chuma chimene anachipata chatha.
37 Wich ka wich oliel kendo yie tik ka yie tik ongʼad oko; lwedo ka lwedo otongʼ oko kendo nungo ka nungo oum gi law ywak.
Aliyense wameta mutu wake ndi ndevu zake; manja a munthu aliyense ndi ochekacheka, ndipo munthu aliyense wavala chiguduli mʼchiwuno mwake.
38 Ewi tat udi duto man Moab kendo e laru mar galamoro onge gimoro makmana ywak, nimar aseketho Moab ka agulu motore maonge ngʼama dwaro,” Jehova Nyasaye ema owacho.
Pa madenga onse a ku Mowabu ndiponso mʼmisewu yake anthu akungolira, pakuti ndaphwanya Mowabu ngati mtsuko wopanda ntchito,” akutero Yehova.
39 “Mano kaka otieke! Mano kaka gidengo! Mano kaka Moab loko ngʼeye kopondo nikech wichkuot! Moab osebedo gir ajara, gima bwogo ji duto man bute.”
“Taonani mmene waphwanyikira! Tamvani momwe akulirira! Taonani momwe Mowabu wachititsidwira manyazi. Mowabu wasanduka chinthu chonyozeka, chinthu chochititsa mantha kwa onse amene amuzungulira.”
40 Ma e gima Jehova Nyasaye wacho: “Ne! Otenga fuyo kochiko piny, oyaro bwombene ewi Moab.
Yehova akuti, “Mtundu wina udzachita kuwuluka nʼkugwera pa Mowabu ngati chiwombankhanga chimene chatambalitsa mapiko ake.
41 Kerioth nomaki kendo kuondegi mag pondo nokaw. E odiechiengno chunje mag jolwenj Moab nochal gi chuny dhako mamuoch kayo.
Mizinda idzagwidwa ndipo malinga adzalandidwa. Pa tsiku limenelo mitima ya ankhondo a ku Mowabu idzakhala ngati mtima wa mayi pa nthawi yake yochira.
42 Moab notieki kaka oganda nikech ne otamore winjo Jehova Nyasaye.
Mowabu sudzakhala mtundu wa anthu chifukwa unadzikuza powukira Yehova.
43 Masira maduongʼ gi bur matut kod otegu ritou, yaye jo-Moab,” Jehova Nyasaye ema owacho.
Zoopsa, dzenje ndi msampha zikudikira inu anthu a ku Mowabu,” akutero Yehova.
44 “Ngʼatno manotem tony nikech masira nolwar e bur matut, ngʼatno manotem kawuok ei bur matut, nomak gi obadho; nimar anakel magi kuom Moab e higa mar kum,” Jehova Nyasaye ema owacho.
“Aliyense wothawa zoopsa adzagwera mʼdzenje, aliyense wotuluka mʼdzenje adzakodwa mu msampha. Ndigwetsa zimenezi pa Mowabu pa nthawi ya chilango chake,” akutero Yehova.
45 “E tipo mar Heshbon joma noringo odongʼ ka ok nyal, nimar mach osemoko liel Heshbon kendo ligek mach osewuok e dier Sihon; owangʼo lela wangʼ Moab, kod choke wich mag jongʼayigo!
“Anthu othawa nkhondo ayima pa mthunzi wa Hesiboni chifukwa chotopa. Koma moto wayaka kuchokera ku Hesiboni, malawi a moto abuka kuchokera ku nyumba ya mfumu Sihoni. Motowo ukuwononga mapiri a ku Mowabu, dziko la anthu onyada.
46 Mano kaka inine malit, yaye Moab! Jo-Kemosh otieki; yawuoti oter e twech, kendo nyigi oket wasumbini.
Tsoka kwa iwe Mowabu! Anthu opembedza Kemosi awonongeka. Ana ako aamuna ndi aakazi atengedwa ukapolo.
47 “Kata kamano anaduog gweth mag Moab e ndalo mabiro,” Jehova Nyasaye ema owacho. Ma e giko mar ngʼadone Moab bura.
“Komabe masiku akutsogolo ndidzabwezeranso Mowabu chuma chake,” akutero Yehova. Chiweruzo cha Mowabu chathera pamenepa.

< Jeremia 48 >