< Ordsprogene 24 >
1 Misund ej onde Folk, hav ikke lyst til at være med dem;
Usachitire nsanje anthu oyipa, usalakalake kuti uzikhala nawo,
2 thi deres Hjerte pønser på Vold, deres Læbers Ord volder Men.
pakuti mitima yawo imalingalira chiwawa, ndipo pakamwa pawo pamayankhula zoyambitsa mavuto.
3 Ved Visdom bygges et Hus, ved Indsigt holdes det oppe,
Nyumba imamangidwa ndi anthu anzeru, ndipo imakhazikika ndi anthu odziwa zinthu;
4 ved Kundskab fyldes kamrene med alskens kosteligt, herligt Gods.
Munthu wodziwa zinthu angathe kudzaza zipinda zake ndi chuma chamtengowapatali ndiponso chabwino.
5 Vismand er større end Kæmpe, kyndig Mand mer end Kraftkarl.
Munthu wodziwa zinthu ali ndi mphamvu yayikulu kuposa munthu wanyonga zambiri, ndipo munthu wachidziwitso amaposa munthu wamphamvu.
6 Thi Krig skal du føre efter modent Overlæg, vel står det til, hvor mange giver Råd.
Pafunika malangizo kuti ukamenye nkhondo. Pakakhala aphungu ambiri kupambana kumakhalapo.
7 Visdom er Dåren for høj, han åbner ej Munden i Porten.
Nzeru ndi chinthu chapatali kwambiri kwa chitsiru; chilibe choti chiyankhule pabwalo la milandu pa chipata.
8 Den, der har ondt i Sinde, kaldes en rænkefuld Mand.
Amene amakonzekera kuchita zoyipa adzatchedwa mvundulamadzi.
9 Hvad en Dåre har for, er Synd, en Spotter er Folk en Gru.
Kukonzekera kuchita za uchitsiru ndi tchimo, ndipo munthu wonyoza amanyansa anthu.
10 Taber du Modet på Trængslens Dag, da er din Kraft kun ringe.
Ngati utaya mtima nthawi ya mavuto ndiye kuti mphamvu yako ndi yochepadi!
11 Frels dem, der slæbes til Døden, red dem, der vakler hen for at dræbes.
Uwapulumutse amene akutengedwa kuti akaphedwe; uwalanditse amene akuyenda movutika kupita kokaphedwa.
12 Siger du: "Se, jeg vidste det ikke" - mon ej han, der vejer Hjerter, kan skønne? Han, der tager Vare på din Sjæl, han ved det, han gengælder Mennesker, hvad de har gjort.
Ukanena kuti, “Koma ife sitinadziwe kanthu za izi,” kodi Iye amene amasanthula mtima sazindikira zimenezi? Kodi Iye amene amateteza moyo wako sazidziwa zimenezi? Kodi Iye sadzalipira munthu malingana ndi ntchito zake?
13 Spis Honning, min Søn, det er godt, og Kubens Saft er sød for din Gane;
Mwana wanga, uzidya uchi popeza ndi wabwino; uchi wochokera mʼchisa cha njuchi ndi wokoma ukawulawa.
14 vid, at så er og Visdom for Sjælen! Når du finder den, har du en Fremtid, dit Håb bliver ikke til intet.
Udziwe kuti nzeru ndi yoteronso pa moyo wako; ngati uyipeza nzeruyo, zinthu zidzakuyendera bwino mʼtsogolo, ndipo chiyembekezo chako sichidzapita pachabe.
15 Lur ej på den retfærdiges Bolig, du gudløse, ødelæg ikke hans Hjem;
Usachite zachifwamba nyumba ya munthu wolungama ngati munthu woyipa. Usachite nayo nkhondo nyumba yake;
16 thi syv Gange falder en retfærdig og står op, men gudløse styrter i Fordærv.
paja munthu wolungama akagwa kasanu nʼkawiri amadzukiriranso. Koma woyipa adzathedwa tsoka likadzawafikira.
17 Falder din Fjende, så glæd dig ikke, snubler han, juble dit Hjerte ikke,
Usamakondwera ndi kugwa kwa mdani wako. Mtima wako usamasangalale iye akapunthwa.
18 at ikke HERREN skal se det med Mishag og vende sin Vrede fra ham.
Kuopa kuti Yehova ataziona zimenezi nayipidwa nazo, angaleke kukwiyira mdaniyo.
19 Græm dig ej over Ugerningsmænd, misund ikke de gudløse;
Usavutike mtima chifukwa cha anthu ochita zoyipa kapena kuchitira nsanje anthu oyipa,
20 thi den onde har ingen Fremtid, gudløses Lampe går ud.
paja munthu woyipa alibe tsogolo. Moyo wa anthu oyipa adzawuzimitsa ngati nyale.
21 Frygt HERREN og Kongen, min Søn, indlad dig ikke med Folk, som gør Oprør;
Mwana wanga, uziopa Yehova ndi mfumu, ndipo usamagwirizana ndi anthu owachitira mwano,
22 thi brat kommer Ulykke fra dem, uventet Fordærv fra begge.
awiri amenewa amagwetsa tsoka mwadzidzidzi. Ndani angadziwe mavuto amene angagwetse?
23 Også følgende Ordsprog er af vise Mænd. Partiskhed i Retten er ilde.
Malangizo enanso a anthu anzeru ndi awa: Kukondera poweruza mlandu si chinthu chabwino:
24 Mod den, som kender en skyldig fri, er Folkeslags Banden, Folkefærds Vrede;
Aliyense amene amawuza munthu wolakwa kuti, “Iwe ndi munthu wosalakwa,” anthu a mitundu yonse adzamutemberera, ndi mitundu ya anthu idzayipidwa naye.
25 men dem, der dømmer med Ret, går det vel, dem kommer Lykkens Velsignelse over.
Koma olanga anthu oyipa zinthu zidzawayendera bwino ndipo madalitso ochuluka adzakhala pa iwo.
26 Et Kys på Læberne giver den, som kommer med ærligt Svar.
Woyankhula mawu owona ndiye amaonetsa chibwenzi chenicheni.
27 Fuldfør din Gerning udendørs, gør dig færdig ude på Marken og byg dig siden et Hus!
Ugwiriretu ntchito zako zonse, makamaka za ku munda ndipo pambuyo pake uyambe kumanga nyumba.
28 Vidn ikke falsk mod din Næste, vær ikke letsindig med dine Læber;
Usakhale mboni yotsutsa mnzako popanda chifukwa, kapena kugwiritsa ntchito pakamwa pako kunena zachinyengo.
29 sig ikke: "Jeg gør mod ham, som han gjorde mod mig, jeg gengælder hver hans Gerning."
Usanene kuti, “Ine ndidzamuchitira iye monga momwe wandichitira ine; ndidzamubwezera munthu ameneyo zimene anandichitira.”
30 Jeg kom forbi en lad Mands Mark og et uforstandigt Menneskes Vingård;
Ndinkayenda mʼmbali mwa munda wa munthu waulesi ndinadutsa munda wamphesa wa munthu wopanda nzeru.
31 se, den var overgroet af Tidsler, ganske skjult af Nælder; Stendiget om den lå nedbrudt.
Ndinapeza kuti paliponse mʼmundamo munali mutamera minga, mʼnthaka imeneyo munali mutamera khwisa, ndipo mpanda wake wamiyala unali utawonongeka.
32 Jeg skued og skrev mig det bag Øre, jeg så og tog Lære deraf:
Tsono nditaona ndinayamba kuganizira mu mtima mwanga ndipo ndinatolapo phunziro ili:
33 Lidt Søvn endnu, lidt Blund, lidt Hvile med samlagte Hænder:
Ukati, “Bwanji ndigone pangʼono,” kapena “Ndiwodzereko pangʼono,” kapenanso “Ndipinde manja pangʼono kuti ndipumule,”
34 Som en Stimand kommer da Fattigdom over dig, Trang som en skjoldvæbnet Mand.
umphawi udzafika pa iwe ngati mbala ndipo usiwa udzakupeza ngati munthu wachifwamba.