< 4 Mosebog 7 >

1 Og det skete paa den Dag, der Mose var færdig med at oprejse Tabernaklet og salvede det og helligede det og alt Redskabet dertil og Alteret og alt Redskabet dertil og salvede dem og helligede dem,
Mose atamaliza kuyimika chihema chija, anachidzoza mafuta ndi kuchipatula pamodzi ndi ziwiya zake zonse. Anadzozanso guwa lansembe ndi kulipatula pamodzi ndi ziwiya zake zonse.
2 da ofrede Israels Fyrster, som vare Øverster for deres Fædrenehuse, de, som vare Stammernes Fyrster, de, som forestode de talte.
Kenaka atsogoleri a Aisraeli, akuluakulu a mabanja omwe ankayangʼanira mafuko a anthu omwe anawawerenga aja, anachita chopereka.
3 Og de førte deres Offer frem for Herrens Ansigt: Seks bedækkede Vogne og tolv Øksne, en Vogn for to Fyrster og en Okse for hver en, og de førte dem frem foran Tabernaklet.
Anabweretsa zopereka zawo pamaso pa Yehova: ngolo zophimbidwa zisanu ndi imodzi ndiponso ngʼombe zothena khumi ndi ziwiri. Mtsogoleri mmodzi ngʼombe yothena imodzi ndipo atsogoleri awiri ngolo imodzi. Izi anazipereka ku chihema.
4 Og Herren talede til Mose og sagde:
Yehova anawuza Mose kuti,
5 Tag disse af dem, at de kunne være til at gøre Tjeneste ved Forsamlingens Paulun, og du skal give dem til Leviterne, hver efter sin Tjenestes Beskaffenhed.
“Ulandire zimenezi kwa iwo kuti zigwire ntchito ku tenti ya msonkhano. Uzipereke kwa Alevi, aliyense monga mwa ntchito yake.”
6 Da tog Mose Vognene og Øksnene og gav dem til Leviterne.
Choncho Mose anatenga ngolo ndi ngʼombe zothenazo nazipereka kwa Alevi.
7 Han gav Gersons Børn to Vogne og fire Øksne efter deres Tjenestes Beskaffenhed.
Anapereka ngolo ziwiri ndi ngʼombe zothena zinayi kwa Ageresoni monga mwantchito yawo
8 Og han gav Merari Børn fire Vogne og otte Øksne efter deres Tjenestes Beskaffenhed, under Tilsyn af Ithamar, Præsten Arons Søn.
ndiponso anapereka ngolo zinayi ndi ngʼombe zothena zisanu ndi zitatu kwa Amerari molingananso ndi ntchito yawo. Onsewa ankawayangʼanira anali Itamara mwana wa Aaroni wansembe.
9 Men Kahaths Børn gav han ingen, fordi Tjenesten med de hellige Ting, som skulde bæres paa Skuldrene, paalaa dem.
Koma Mose sanapereke zimenezi kwa Akohati chifukwa zinthu zawo zopatulika zomwe ankayangʼanira zinali zoti azinyamula pa mapewa awo.
10 Og Fyrsterne ofrede til Alterets Indvielse, paa den Dag det blev salvet, ja, Fyrsterne ofrede deres Offer foran Alteret.
Guwa la nsembe litadzozedwa, atsogoleri anabweretsa zopereka zawo zopatulira guwa nazipereka paguwapo.
11 Og Herren sagde til Mose: Lad een Fyrste hver Dag, ja, een Fyrste hver Dag ofre sit Offer til Alterets Indvielse.
Pakuti Yehova anawuza Mose kuti, “Tsiku lililonse mtsogoleri mmodzi azibweretsa chopereka chake chopatulira guwa lansembe.”
12 Og den, som ofrede sit Offer paa den første Dag, var Nahesson, Amminadabs Søn, Judas Stammes Fyrste.
Amene anabweretsa chopereka chake tsiku loyamba anali Naasoni mwana wa Aminadabu wa fuko la Yuda.
13 Og hans Offer var eet Sølvfad, dets Vægt var hundrede og tredive Sekel, een Sølvskaal paa halvfjerdsindstyve Sekel efter Helligdommens Sekel; de vare begge fulde af Mel, blandet med Olie, til et Madoffer;
Chopereka chake chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi, ndi beseni lasiliva limodzi lowazira, lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo wopatulika ndipo zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta ngati chopereka chachakudya;
14 een Røgelseskaal paa ti Sekel Guld, fuld af Røgelse;
mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
15 een ung Okse, een Væder, eet Lam, aargammelt, til et Brændoffer;
mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa wamwamuna mmodzi wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza;
16 een Gedebuk til et Syndoffer;
mbuzi yayimuna imodzi, nsembe ya machimo;
17 og to Øksne, fem Vædre, fem Bukke, fem Lam, aargamle, til et Takoffer. Dette var Nahessons, Amminadabs Søns, Offer.
ndi ngʼombe zothena ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa asanu a chaka chimodzi kuti zikhale za nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Naasoni mwana wa Aminadabu.
18 Paa den anden Dag ofrede Nethaneel, Zuars Søn, Isaskars Fyrste.
Pa tsiku lachiwiri, Natanieli mwana wa Zuwara, mtsogoleri wa Isakara, anabweretsa chopereka chake.
19 Han ofrede sit Offer: Eet Sølvfad, dets Vægt var hundrede og tredive Sekel, een Sølvskaal paa halvfjerdsindstyve Sekel efter Helligdommens Sekel; de vare begge fulde af Mel, blandet med Olie, til et Madoffer;
Chopereka chomwe anabwera nacho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, molingana ndi muyeso wa ku malo opatulika. Mbale zonse zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka cha chakudya.
20 en Røgelseskaal paa ti Sekel Guld, fuld af Røgelse;
Mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110 yodzaza ndi lubani;
21 een ung Okse, een Væder, eet Lam, aargammelt, til et Brændoffer;
mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza:
22 een Gedebuk til et Syndoffer;
mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yotetezera machimo;
23 og to Øksne, fem Vædre, fem Bukke, fem Lam, aargamle, til et Takoffer. Dette var Nethaneels, Zuars Søns, Offer.
ndi ngʼombe ziwiri, nkhosa zazimuna ziwiri, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa asanu a chaka chimodzi, nsembe ya chiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Netanieli mwana wa Zuwara.
24 Paa den tredje Dag ofrede Sebulons Børns Fyrste, Eliab, Helons Søn.
Pa tsiku lachitatu, Eliabu mwana wa Heloni, mtsogoleri wa Azebuloni, anabweretsa chopereka chake.
25 Hans Offer var eet Sølvfad, dets Vægt var hundrede og tredive Sekel, een Sølvskaal paa halvfjerdsindstyve Sekel efter Helligdommens Sekel; de vare begge fulde af Mel, blandet med Olie, til et Madoffer;
Chopereka chake chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, ndi beseni limodzi lasiliva lowazira lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika, mbale zonse zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, chopereka cha chakudya;
26 een Røgelseskaal paa ti Sekel Guld, fuld af Røgelse;
mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
27 een ung Okse, een Væder, eet Lam, aargammelt, til et Brændoffer;
mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa wamwamuna mmodzi wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza;
28 een Gedebuk til et Syndoffer;
mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
29 og to Øksne, fem Vædre, fem Bukke, fem Lam, aargamle, til et Takoffer. Dette var Eliabs, Helons Søns, Offer.
ndi ngʼombe ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Eliabu mwana wa Heloni.
30 Paa den fjerde Dag ofrede Rubens Børns Fyrste, Elizur, Sedeurs Søn.
Tsiku lachinayi linali la Elizuri mwana wa Sedeuri, mtsogoleri wa fuko la Rubeni, anabweretsa chopereka chake.
31 Hans Offer var eet Sølvfad, dets Vægt var hundrede og tredive Sekel, een Sølvskaal paa halvfjerdsindstyve Sekel efter Helligdommens Sekel; de vare begge fulde af Mel, blandet med Olie, til et Madoffer;
Chopereka chake chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, chopereka chachakudya.
32 een Røgelseskaal paa ti Sekel Guld, fuld af Røgelse;
Mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
33 een ung Okse, een Væder, eet Lam, aargammelt, til et Brændoffer;
mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza;
34 een Gedebuk til et Syndoffer;
mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
35 og to Øksne, fem Vædre, fem Bukke, fem Lam, aargamle, til et Takoffer. Dette var Elizurs, Sedeurs Søns, Offer.
ndi ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna ziwiri, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Elizuri mwana wa Sedeuri.
36 Paa den femte Dag ofrede Simeons Børns Fyrste, Selumiel, Zurisaddai Søn.
Pa tsiku lachisanu Selumieli mwana wa Zurisadai, mtsogoleri wa fuko la Simeoni, anabweretsa chopereka chake.
37 Hans Offer var eet Sølvfad, dets Vægt var hundrede og tredive Sekel, een Sølvskaal paa halvfjerdsindstyve Sekel efter Helligdommens Sekel; de vare begge fulde af Mel, blandet med Olie, til et Madoffer;
Chopereka chake chinali mbale yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka ndi beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika. Zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
38 een Røgelseskaal paa ti Sekel Guld, fuld af Røgelse;
mbale yagolide imodzi yolemera 110, yodzaza ndi lubani;
39 een ung Okse, een Væder, eet Lam, aargammelt, til et Brændoffer;
mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi ndi mwana wankhosa mmodzi wamwamuna wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza;
40 een Gedebuk til et Syndoffer;
mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
41 og to Øksne, fem Vædre, fem Bukke, fem Lam, aargamle, til et Takoffer. Dette var Selumiels, Zurisaddai Søns, Offer.
ngʼombe ziwiri, nkhosa zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Selumieli mwana wa Zurisadai.
42 Paa den sjette Dag ofrede Gads Børns Fyrste, Eliasaf, Deuels Søn.
Pa tsiku lachisanu ndi chimodzi, Eliyasafu mwana wa Deuweli, mtsogoleri wa fuko la Gadi, anabweretsa chopereka chake.
43 Hans Offer var eet Sølvfad, dets Vægt var hundrede og tredive Sekel, een Sølvskaal paa halvfjerdsindstyve Sekel efter Helligdommens Sekel; de vare begge fulde af Mel, blandet med Olie, til et Madoffer;
Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
44 en Røgelseskaal paa ti Sekel Guld, fuld af Røgelse;
mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
45 een ung Okse, een Væder, eet Lam, aargammelt, til et Brændoffer;
mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa wamwamuna mmodzi wa chaka chimodzi, chopereka cha nsembe yopsereza:
46 een Gedebuk til et Syndoffer;
mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
47 og to Øksne, fem Vædre, fem Bukke, fem Lam, aargamle, til et Takoffer. Dette var Eliasafs, Deuels Søns, Offer.
ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Eliyasafu mwana wa Deuweli.
48 Paa den syvende Dag ofrede Efraims Børns Fyrste, Elisama, Ammihuds Søn.
Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri Elisama mwana wa Amihudi, mtsogoleri wa fuko la Efereimu, anabweretsa chopereka chake.
49 Hans Offer var eet Sølvfad, dets Vægt var hundrede og tredive Sekel, een Sølvskaal paa halvfjerdsindstyve Sekel efter Helligdommens Sekel; de vare begge fulde af Mel, blandet med Olie, til et Madoffer;
Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, ndi beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonsezi monga mwa muyeso wa ku malo opatulika, zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
50 een Røgelseskaal paa ti Sekel Guld, fuld af Røgelse;
mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
51 een ung Okse, een Væder, eet Lam, aargammelt, til et Brændoffer;
mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa wamwamuna mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza;
52 een Gedebuk til et Syndoffer;
mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
53 og to Øksne, fem Vædre, fem Bukke, fem Lam, aargamle, til et Takoffer. Dette var Elisamas, Ammihuds Søns, Offer.
ngʼombe ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Elisama mwana wa Amihudi.
54 Paa den ottende Dag ofrede Manasse Børns Fyrste, Gamliel, Pedazurs Søn.
Pa tsiku lachisanu ndi chitatu Gamalieli mwana wa Pedazuri, mtsogoleri wa fuko Manase, anabweretsa chopereka chake.
55 Hans Offer var eet Sølvfad, dets Vægt var hundrede og tredive Sekel, een Sølvskaal paa halvfjerdsindstyve Sekel efter Helligdommens Sekel; de vare begge fulde af Mel, blandet med Olie, til et Madoffer;
Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, ndi beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
56 een Røgelseskaal paa ti Sekel Guld, fuld af Røgelse;
mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani,
57 een ung Okse, een Væder, eet Lam, aargammelt, til et Brændoffer;
mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza;
58 een Gedebuk til et Syndoffer;
mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
59 og to Øksne, fem Vædre, fem Bukke, fem Lam, aargamle, til et Takoffer. Dette var Gamliels, Pedazurs Søns, Offer.
ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Gamalieli mwana wa Pedazuri.
60 Paa den niende Dag ofrede Benjamins Børns Fyrste, Abidan, Gideoni Søn.
Pa tsiku lachisanu ndi chinayi Abidani mwana wa Gideoni mtsogoleri wa fuko la Benjamini, anabweretsa chopereka chake.
61 Hans Offer var eet Sølvfad, dets Vægt var hundrede og tredive Sekel, een Sølvskaal paa halvfjerdsindstyve Sekel efter Helligdommens Sekel; de vare begge fulde af Mel, blandet med Olie, til et Madoffer;
Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka ndi beseni limodzi lowazira lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka cha zakudya;
62 een Røgelseskaal paa ti Sekel Guld, fuld af Røgelse;
mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
63 een ung Okse, een Væder, eet Lam, aargammelt, til et Brændoffer;
mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza;
64 een Gedebuk til et Syndoffer;
mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
65 og to Øksne, fem Vædre, fem Bukke, fem Lam, aargamle, til et Takoffer. Dette var Abidans, Gideoni Søns, Offer.
ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu, ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Abidani mwana wa Gideoni.
66 Paa den tiende Dag ofrede Dans Børns Fyrste, Ahieser, Ammisaddai Søn.
Pa tsiku lakhumi Ahiyezeri mwana wa Amisadai, mtsogoleri wa fuko la Dani anabweretsa chopereka chake.
67 Hans Offer var eet Sølvfad, dets Vægt var hundrede og tredive Sekel, een Sølvskaal paa halvfjerdsindstyve Sekel efter Helligdommens Sekel; de vare begge fulde af Mel, blandet med Olie, til et Madoffer;
Chopereka chake chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika, zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
68 een Røgelseskaal paa ti Sekel Guld, fuld af Røgelse;
mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
69 een ung Okse, een Væder, eet Lam, aargammelt, til et Brændoffer;
mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza;
70 een Gedebuk til et Syndoffer;
mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
71 og to Øksne, fem Vædre, fem Bukke, fem Lam, aargamle, til et Takoffer. Dette var Ahiesers, Ammisaddai Søns, Offer.
ndi ngʼombe ziwiri zazimuna, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu, ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Ahiyezeri mwana wa Amisadai.
72 Paa den ellevte Dag ofrede Asers Børns Fyrste, Pagiel, Okrans Søn.
Pa tsiku la khumi ndi chimodzi, Pagieli mwana wa Okirani, mtsogoleri wa fuko la Aseri, anabweretsa chopereka chake.
73 Hans Offer var eet Sølvfad, dets Vægt var hundrede og tredive Sekel, een Sølvskaal paa halvfjerdsindstyve Sekel efter Helligdommens Sekel; de vare begge fulde af Mel, blandet med Olie, til et Madoffer;
Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
74 een Røgelseskaal paa ti Sekel Guld, fuld af Røgelse;
mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
75 een ung Okse, een Væder, eet Lam, aargammelt, til et Brændoffer;
mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza;
76 een Gedebuk til et Syndoffer;
mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo;
77 og to Øksne, fem Vædre, fem Bukke, fem Lam, aargamle, til et Takoffer. Dette var Pagiels, Okrans Søns, Offer.
ngʼombe ziwiri zazimuna, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu, ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Pagieli mwana wa Okirani.
78 Paa den tolvte Dag ofrede Nafthali Børns Fyrste, Ahira, Enans Søn.
Pa tsiku la khumi ndi chimodzi Ahira mwana wa Enani, mtsogoleri wa fuko la Nafutali, anabweretsa chopereka chake.
79 Hans Offer var eet Sølvfad, dets Vægt var hundrede og tredive Sekel, een Sølvskaal paa halvfjerdsindstyve Sekel efter Helligdommens Sekel; de vare begge fulde af Mel, blandet med Olie, til et Madoffer;
Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lowazira lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika, zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya;
80 een Røgelseskaal paa ti Sekel Guld, fuld af Røgelse;
mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani;
81 een ung Okse, een Væder, eet Lam, aargammelt, til et Brændoffer;
mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza;
82 een Gedebuk til et Syndoffer;
mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yopepesera machimo;
83 og to Øksne, fem Vædre, fem Bukke, fem Lam, aargamle, til et Takoffer. Dette var Ahiras, Enans Søns, Offer.
ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu, ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Ahira mwana wa Enani.
84 Dette er Alterets Indvielse af Israels Fyrster, paa den Dag det blev salvet: Tolv Sølvfade, tolv Sølvskaaler, tolv Guldrøgelseskaaler;
Zopereka za atsogoleri a Israeli zopatulira guwa lansembe pamene linadzozedwa zinali izi: mbale khumi ndi ziwiri zasiliva, mabeseni owazira asiliva khumi ndi awiri ndi mbale zagolide khumi ndi ziwiri.
85 hvert Fad var paa hundrede og tredive Sekel Sølv, og hver Skaal paa halvfjerdsindstyve Sekel, alt Sølvet af Karrene beløb sig til to Tusinde og fire Hundrede Sekel efter Helligdommens Sekel.
Mbale iliyonse yasiliva inkalemera kilogalamu imodzi ndi theka, ndipo beseni lililonse lowazira linkalemera magalamu 800. Pamodzi, mbale zonse zasiliva zinkalemera makilogalamu 27 monga mwa muyeso wa ku malo opatulika.
86 Tolv Guldrøgelseskaaler, fulde af Røgelse, hver Røgelseskaal paa ti Sekel efter Helligdommens Sekel; alt Guldet af de Røgelseskaaler beløb sig til hundrede og tyve Sekel.
Mbale khumi ndi ziwiri zagolide zodzaza ndi lubanizo zinkalemera magalamu 110 iliyonse, monga mwa muyeso wa ku malo opatulika. Pamodzi, mbale zagolide zinkalemera kilogalamu imodzi ndi theka.
87 Alt stort Kvæg til Brændofret var tolv Okser, tolv Vædre, tolv Lam, aargamle, og deres Madoffer, og tolv Gedebukke til Syndoffer.
Chiwerengero cha nyama zonse za nsembe yopsereza chinali motere: ngʼombe zazimuna khumi ndi ziwiri, nkhosa zazimuna khumi ndi ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi awiri a chaka chimodzi pamodzi ndi chopereka chachakudya. Mbuzi zazimuna khumi ndi ziwiri zinali za nsembe yopepesera machimo.
88 Og alt stort Kvæg til Takofret var fire og tyve Okser, tresindstyve Vædre, tresindstyve Bukke, tresindstyve Lam, aargamle. Dette er Alterets Indvielse, efter at det var salvet.
Chiwerengero cha nyama zonse za nsembe yachiyanjano chinali motere: ngʼombe zothena 24, nkhosa zazimuna 60, mbuzi zazimuna 60 ndi ana ankhosa aamuna a chaka chimodzi 60. Zimenezi ndi zimene zinali zopereka zopatulira guwa lansembe litadzozedwa.
89 Og naar Mose kom til Forsamlingens Paulun for at tale med ham, da hørte han Røsten tale til sig ovenfra Naadestolen, som var paa Vidnesbyrdets Ark, midt ud fra de to Keruber; og han talede til ham.
Mose atalowa mu tenti ya msonkhano kukayankhula ndi Yehova, anamva mawu kuchokera pakati pa Akerubi awiri amene anali pamwamba pa chivundikiro cha bokosi la umboni. Ndipo anayankhula naye.

< 4 Mosebog 7 >