< Skutky Apoštolů 1 >
1 První zajisté knihu sepsalť jsem, ó Teofile, o všech věcech, kteréž začal Ježíš činiti a učiti,
Mʼbuku langa loyamba, ndinakulembera iwe Teofilo zonse zimene Yesu anayamba kuchita ndi kuphunzitsa,
2 Až do toho dne, v kterémžto dav přikázání apoštolům, kteréž byl skrze Ducha svatého vyvolil, vzhůru vzat jest.
mpaka tsiku limene anatengedwa kupita kumwamba, mwamphamvu ya Mzimu Woyera, atawalangiza atumwi amene anawasankha.
3 Kterýmžto i zjevoval sebe samého živého po svém umučení ve mnohých jistých důvodích, za čtyřidceti dnů ukazuje se jim a mluvě o království Božím.
Zitatha zowawa zake Yesu anadzionetsa kwa ophunzira ake, ndi kuonetsanso maumboni ambiri kuti anali wamoyo. Iye anadzionetsera kwa iwo ndi kuwaphunzitsa za ufumu wa Mulungu pa masiku makumi anayi.
4 A shromáždiv se s nimi, přikázal jim, aby z Jeruzaléma neodcházeli, ale aby očekávali zaslíbení Otcova, o kterémž jste prý slyšeli ode mne.
Nthawi ina atasonkhana nawo pamodzi, Yesu analamulira ophunzira ake kuti, “Musachoke mu Yerusalemu, koma mudikire mphatso imene Atate anga analonjeza yomwe ndinakuwuzani.
5 Nebo Jan zajisté křtil vodou, ale vy pokřtěni budete Duchem svatým po nemnohých těchto dnech.
Pakuti Yohane anakubatizani ndi madzi, koma posachedwapa inu mudzabatizidwa ndi Mzimu Woyera.”
6 Oni pak sšedše se, otázali se ho, řkouce: Pane, v tomto-li času napravíš království Izraelské?
Atumwi atasonkhana pamodzi, iwo anamufunsa Iye kuti, “Ambuye, kodi nthawi ino mubwezeretsa ufumu kwa Israeli?”
7 I řekl jim: Neníť vaše věc znáti časy anebo příhodnosti časů, kteréžto Otec v moci své položil.
Yesu anawawuza kuti, “Sikofunika kuti mudziwe za nthawi kapena masiku amene Atate ayika mwa ulamuliro wawo.
8 Ale přijmete moc Ducha svatého, přicházejícího na vás, a budete mi svědkové, i v Jeruzalémě, i ve všem Judstvu, i v Samaří, a až do posledních končin země.
Koma mudzalandira mphamvu Mzimu Woyera akadzafika pa inu; ndipo mudzakhala mboni zanga mu Yerusalemu, ku Yudeya konse ndi ku Samariya, mpaka ku malekezero a dziko lapansi.”
9 A to pověděv, ani na to hledí, vzhůru vyzdvižen jest, a oblak vzal jej od očí jejich.
Atatha kuyankhula zimenezi, Yesu anatengedwa kupita kumwamba ophunzira ake akuona, ndipo anabisika mʼmitambo.
10 A když za ním v nebe jdoucím pilně hleděli, aj, dva muži postavili se podle nich v rouše bílém,
Yesu akukwera kumwamba, ophunzira ake anayangʼanitsitsa ndi chidwi mʼmitambo. Mwadzidzidzi anaona anthu awiri ovala zoyera atayimirira pambali pawo.
11 A řekli: Muži Galilejští, co stojíte, hledíce do nebe? Tento Ježíš, kterýž vzhůru vzat jest od vás do nebe, takť přijde, jakž jste spatřili způsob jeho jdoucího do nebe.
Iwo anati, “Inu, anthu a ku Galileya, chifukwa chiyani mukuyima ndi kumayangʼana mʼmitambo? Yesu amene wachotsedwa pakati panu ndi kupita kumwamba, adzabweranso mʼnjira yomweyi mwamuona akupita kumwamba.”
12 Tedy navrátili se do Jeruzaléma od hory, jenž slove Olivetská, kteráž jest blízko Jeruzaléma, vzdálí cesty jednoho dne svátečního.
Pamenepo atumwi anabwerera ku Yerusalemu kuchokera ku phiri la Olivi, mtunda wosakwana kilomita kuchokera mu mzindamo.
13 A když přišli domů, vstoupili do vrchního příbytku domu, kdež přebývali, i Petr i Jakub, i Jan a Ondřej, Filip a Tomáš, Bartoloměj a Matouš, Jakub Alfeův a Šimon Zelótes a Judas bratr Jakubův.
Atafika mu mzindamo, analowa mʼchipinda chammwamba kumene amakhala. Amene analipo anali awa: Petro, Yohane, Yakobo ndi Andreya; Filipo ndi Tomasi, Bartumeyu ndi Mateyu; Yakobo mwana wa Alifeyo ndi Simoni Zelote ndi Yuda mwana wa Yakobo.
14 Ti všickni byli trvajíce jednomyslně na modlitbě a pokorné prosbě s ženami a s Marijí, matkou Ježíšovou, i s bratřími jeho.
Onsewa ndi mtima umodzi anapitiriza kupemphera pamodzi ndi amayi, ndi Mariya amayi ake a Yesu, ndiponso abale ake a Yesu.
15 V těch pak dnech povstav Petr uprostřed učedlníků, řekl (a byl zástup lidí spolu shromážděných okolo sta a dvadcíti):
Pa nthawi imeneyo Petro anayimirira pakati pa okhulupirira (gulu la anthu pafupifupi 120).
16 Muži bratří, musilo se naplniti Písmo to, kteréž předpověděl Duch svatý skrze ústa Davidova o Jidášovi, kterýž byl vůdce těch, jenž jímali Ježíše.
Iye anati, “Abale anga, Malemba anayenera kukwaniritsidwa omwe Mzimu Woyera anayankhula kalekale kudzera mwa Davide za Yudasi, amene anatsogolera amene anamugwira Yesu.
17 Nebo byl přičten k nám, a byl došel losu přisluhování tohoto.
Iye anali mmodzi wa gulu lathu ndipo anatumikira pamodzi ndi ife.”
18 Ten zajisté obdržel pole ze mzdy nepravosti, a oběsiv se, rozpukl se na dvé, i vykydla se všecka střeva jeho.
(Yudasi anagula munda ndi ndalama zimene anazipeza pochita zoyipa zija; kumeneko, iye anagwa chamutu, naphulika pakati ndipo matumbo ake wonse anakhuthuka.
19 A to známé jest učiněno všechněm přebývajícím v Jeruzalémě, takže jest nazváno pole to vlastním jazykem jejich Akeldama, to jest pole krve.
Aliyense mu Yerusalemu anamva zimenezi, kotero anatcha mundawo mʼchiyankhulo chawo kuti Akeledama, kutanthauza, Munda wa Magazi).
20 Psáno jest zajisté v knihách Žalmů: Budiž příbytek jeho pustý, a nebuď, kdo by přebýval v něm, a opět: Biskupství jeho vezmi jiný.
Petro anati, “Pakuti kwalembedwa mʼbuku la Masalimo kuti, “Nyumba yake isanduke bwinja, ndipo pasakhale wogonamo. Ndiponso, “Wina atenge ntchito yake yautsogoleri.
21 Protož musíť to býti, aby jeden z těch mužů, kteříž jsou s námi bývali po všecken čas, v němž přebýval mezi námi Pán Ježíš,
Chifukwa chake ndi kofunika kusankha mmodzi wa anthu amene akhala nafe nthawi yonse imene Ambuye Yesu ankayenda nafe,
22 Počav od křtu Janova až do dne toho, v kterémžto vzhůru vzat jest od nás, byl svědkem spolu s námi vzkříšení jeho.
kuyambira pa nthawi ya ubatizo wa Yohane mpaka nthawi imene Yesu anatengedwa pakati pathu. Pakuti mmodzi wa anthu awa ayenera kukhala mboni pamodzi ndi ife zakuuka kwake.”
23 Tedy postavili dva, Jozefa, jenž sloul Barsabáš, kterýž měl příjmí Justus, a Matěje.
Pamenepo anasankha anthu awiri, Yosefe wotchedwa Barsaba (wodziwikanso kuti Yusto) ndi Matiyasi.
24 A modléce se, řekli: Ty, Pane, všech srdcí zpytateli, ukažiž, kterého jsi vyvolil z těchto dvou,
Kenaka iwo anapemphera nati, “Ambuye mukudziwa mtima wa aliyense. Tionetseni amene mwamusankha mwa awiri awa
25 Aby přijal los přisluhování tohoto a apoštolství, z něhož jest vypadl Jidáš, aby odšel na místo své.
kuti atenge ntchito iyi ya utumwi, imene Yudasi anasiya napita kumalo womuyenera.”
26 I dali jim losy. Spadl pak los na Matěje, i připojen jest z společného snešení k jedenácti apoštolům.
Tsono anachita maere, ndipo maerewo anagwera Matiyasi. Tsono iye anawonjezedwa pa gulu la atumwi khumi ndi mmodziwo.