< Psalmi 8 >

1 Zborovođi. Po napjevu “Tijesci”. Psalam. Davidov. Jahve, Gospode naš, divno je ime tvoje po svoj zemlji, veličanstvom nebo natkriljuješ!
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa gititi. Salimo la Davide. Inu Yehova Ambuye athu, dzina lanu ndi la lamphamvudi pa dziko lonse lapansi! Inu mwakhazikitsa ulemerero wanu mʼmayiko onse akumwamba.
2 U ustima djece i dojenčadi hvalu si spremio protiv neprijatelja, da postidiš mrzitelja, zlotvora.
Kuchokera mʼkamwa mwa ana ndi makanda, Inu mwakhazikitsa mphamvu chifukwa cha adani anu, kukhazikitsa bata adani ndi anthu obwezera zoyipa.
3 Gledam ti nebesa, djelo prstiju tvojih, mjesec i zvijezde što ih učvrsti -
Pamene ndilingalira za mayiko anu akumwamba, ntchito ya zala zanu, mwezi ndi nyenyezi, zimene mwaziyika pa malo ake,
4 pa što je čovjek da ga se spominješ, sin čovječji te ga pohodiš?
munthu ndani kuti Inu mumamukumbukira, ndi mwana wa munthu kuti inu mumacheza naye?
5 Ti ga učini malo manjim od Boga, slavom i sjajem njega okruni.
Inu munamupanga kukhala wocheperapo kusiyana ndi zolengedwa zakumwamba ndipo mwamuveka ulemerero ndi ulemu.
6 Vlast mu dade nad djelima ruku svojih, njemu pod noge sve podloži:
Inu munamuyika wolamulira ntchito ya manja anu; munayika zinthu zonse pansi pa mapazi ake;
7 ovce i svakolika goveda, i zvijeri poljske k tome,
nkhosa, mbuzi ndi ngʼombe pamodzi ndi nyama zakuthengo,
8 ptice nebeske i ribe morske, i što god prolazi stazama morskim.
mbalame zamlengalenga ndi nsomba zamʼnyanja zonse zimene zimayenda pansi pa nyanja.
9 Jahve, Gospode naš, divno je ime tvoje po svoj zemlji!
Inu Yehova, Ambuye athu, dzina lanu ndi lamphamvudi pa dziko lonse lapansi!

< Psalmi 8 >