< Psalmi 18 >
1 Učitelju zbora. Od Jahvina sluge Davida koji Jahvi ispjeva ovu pjesmu u onaj dan kad ga Jahve oslobodi iz ruku neprijatelja Ljubim te, Jahve, kreposti moja!
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide mtumiki wa Yehova. Iye anayimbira Yehova nyimbo iyi pamene Yehovayo anamupulumutsa mʼdzanja la adani ake onse ndiponso mʼdzanja la Sauli. Davide anati: Ine ndimakukondani Inu Yehova, mphamvu zanga.
2 Jahve, hridino moja, utvrdo moja spase moj; Bože moj, pećino moja kojoj se utječem, štite moj, snago spasenja moga, tvrđavo moja!
Yehova ndiye thanthwe langa, chitetezo changa ndi mpulumutsi wanga; Mulungu wanga ndi thanthwe langa mʼmene ndimathawiramo. Chishango changa ndi ndodo yachipulumutso changa, ndi linga langa.
3 Zazvat ću Jahvu, hvale predostojna, i od dušmana bit ću izbavljen.
Ndimayitana Yehova amene ndi woyenera matamando, ndipo ndapulumutsidwa kwa adani anga.
4 Valovi smrti okružiše mene, prestraviše me bujice pogubne.
Zingwe za imfa zinandizinga; mitsinje yothamanga yachiwonongeko inandiopsa kwambiri.
5 Užad Podzemlja sputiše me, smrtonosne zamke padoše na me: (Sheol )
Anandimanga ndi zingwe za ku manda; misampha ya imfa inalimbana nane. (Sheol )
6 u nevolji zazvah Jahvu i Bogu svome zavapih. Iz svog Hrama zov mi začu, i vapaj moj mu do ušiju doprije.
Mʼmasautso anga ndinapemphera kwa Yehova; ndinalirira kwa Mulungu wanga kuti andithandize. Ali mʼNyumba yake, anamva mawu anga; kulira kwanga kunafika pamaso pake ndi mʼmakutu mwake.
7 I zemlja se potrese i uzdrhta, uzdrmaše se temelji gora, pokrenuše se, jer On gnjevom planu.
Dziko lapansi linanjenjemera ndi kuchita chivomerezi, ndipo maziko a mapiri anagwedezeka; ananjenjemera chifukwa Iye anakwiya.
8 Iz nosnica mu dim se diže, iz usta mu oganj liznu, ugljevlje živo od njega plamsa.
Mʼmphuno mwake munatuluka utsi; moto wonyeketsa unatuluka mʼkamwa mwake, makala amoto anali lawilawi mʼkamwa mwake.
9 On nagnu nebesa i siđe, pod nogama oblaci mu mračni.
Iye anangʼamba thambo natsika pansi; pansi pa mapazi ake panali mitambo yakuda.
10 Na keruba stade i poletje; na krilima vjetra zaplovi.
Iye anakwera pa Kerubi ndi kuwuluka; nawuluka ndi mphepo mwaliwiro.
11 Ogrnu se mrakom kao koprenom, prekri se tamnim vodama i oblacima tmastim,
Iye anapanga mdima kukhala chofunda chake, chophimba chake chomuzungulira chinali mitambo yakuda ya mlengalenga.
12 od blijeska pred licem njegovim užga se ugljevlje plameno.
Mʼkuwala kumene kunali pamaso pake munkachokera matalala, makala amoto ndi ziphaliwali zongʼanima.
13 Jahve s neba zagrmje, Svevišnjega glas se ori.
Yehova anabangula kumwamba ngati bingu, mawu a Wammwambamwamba anamveka ponseponse.
14 Odape strijele i dušmane rasu, izbaci munje i na zemlju ih obori.
Iye anaponya mivi yake nabalalitsa adani ake, ndi zingʼaningʼani zake anawagonjetsa.
15 Morska se dna pokazaše, i temelji svijeta postaše goli od strašne prijetnje Jahvine, od olujna daha gnjeva njegova.
Zigwa za mʼnyanja zinaonekera poyera; maziko a dziko lapansi anakhala poyera, Yehova atabangula mwaukali, pamene mpweya wamphamvu unatuluka mʼmphuno mwanu.
16 On pruži s neba ruku i mene prihvati, iz silnih voda on me izbavi.
Ali kumwamba, Iye anatambalitsa dzanja lake ndipo anandigwira; anandivuwula mʼmadzi ozama.
17 Od protivnika moćnog mene oslobodi, od dušmana mojih jačih od mene.
Anandipulumutsa kwa mdani wanga wamphamvu, adani anga, amene anali amphamvu kuposa ine.
18 Navališe na me u dan zlosretni, ali me Jahve zaštiti,
Adaniwo analimbana nane pamene ndinali pa mavuto, koma Yehova anali thandizo langa.
19 na polje prostrano izvede me, spasi me jer sam mu mio.
Iye anandipititsa kumalo otakasuka; anandipulumutsa chifukwa amakondwera nane.
20 Po pravednosti mojoj Jahve mi uzvrati, po čistoći ruku mojih on me nagradi,
Yehova wandithandiza molingana ndi chilungamo changa; molingana ndi makhalidwe anga abwino, Iye wandipulumutsa.
21 jer čuvah putove Jahvine, od Boga se svoga ne udaljih.
Pakuti ine ndinatsata njira za Yehova; ndilibe mlandu wochoka pamaso Mulungu wanga.
22 Odredbe njegove sve su mi pred očima, zapovijedi njegove nisam odbacio,
Malamulo ake onse ali pamaso panga; sindinasiye malangizo ake.
23 do srži odan njemu sam bio, čuvam se grijeha svakoga.
Ndakhala moyo wosalakwa pamaso pake ndipo ndakhala ndi kupewa tchimo.
24 Jahve mi po pravdi mojoj vrati, čistoću ruku mojih vidje.
Yehova wandipatsa mphotho molingana ndi chilungamo changa, molingana ndi kuyera kwa manja anga pamaso pake.
25 S prijateljem ti si prijatelj, poštenu poštenjem uzvraćaš.
Kwa wokhulupirika, Inu mumaonetsa kukhulupirika kwanu; kwa anthu amakhalidwe abwino, Inu mumaonetsanso makhalidwe abwino,
26 S čovjekom čistim ti si čist, a lukavca izigravaš,
kwa woyera mtima, Inu mumaonetsa kuyera mtima kwanu, koma kwa achinyengo mumaonetsanso kunyansidwa nawo.
27 jer narodu poniženu spasenje donosiš, a ponižavaš oči ohole.
Inu mumapulumutsa anthu odzichepetsa, koma anthu amtima odzikuza mumawatsitsa.
28 Jahve, ti moju svjetiljku užižeš, Bože, tminu moju obasjavaš:
Inu Yehova, sungani nyale yanga kuti iziyakabe; Mulungu wanga wasandutsa mdima wanga kukhala kuwunika.
29 s tobom udaram na čete dušmanske, s Bogom svojim preskačem zidine.
Ndi thandizo lanu nditha kulimbana ndi gulu la ankhondo; ndi Mulungu wanga nditha kuchita zosatheka ndi munthu.
30 Savršeni su puti Gospodnji, i riječ je Božja ognjem kušana. On, samo on, štit je svima koji se k njemu utječu.
Kunena za Mulungu, zochita zake ndi zangwiro; mawu a Yehova alibe cholakwika. Iye ndi chishango kwa onse amene amathawira kwa Iye.
31 Jer tko je Bog osim Jahve? Tko li je hridina osim Boga našega?
Mulungu wina ndi uti wofanana nanu Yehova? Ndipo ndani amene ndi Thanthwe kupatula Mulungu wathu?
32 Taj Bog me snagom opasuje, stere mi put besprijekoran,
Ndi Mulungu amene anandipatsa mphamvu ndi kulungamitsa njira yanga.
33 noge mi dade brze k'o u košute i postavi me na visine čvrste,
Iye amasandutsa mapazi anga kukhala ngati ambawala yayikazi; Iye amandithandiza kuyimirira pamwamba pa mapiri.
34 ruke mi za borbu uvježba i mišice da luk mjedeni napinju.
Iye amaphunzitsa manja anga kuchita nkhondo; manja anga amatha kuthyola uta wachitsulo.
35 Daješ mi štit svoj koji spasava, tvoja me desnica drži, tvoja me brižljivost uzvisi.
Inu mumandipatsa chishango chachipambano, ndipo dzanja lanu lamanja limandichirikiza; mumawerama pansi kundikuza.
36 Pouzdanje daješ mom koraku, i noge mi više ne posrću.
Munakulitsa njira yoyendamo ine, kuti mapazi anga asaguluke.
37 Pognah svoje dušmane i dostigoh, i ne vratih se dok ih ne uništih.
Ndinathamangitsa adani anga ndi kuwapitirira; sindinabwerere mpaka atawonongedwa.
38 Obaram ih, ne mogu se dići, padaju, pod nogama mi leže.
Ndinakantha adaniwo kotero kuti sanathenso kudzuka; anagwera pa mapazi anga.
39 Ti me opasa snagom za borbu, a protivnike moje meni podloži.
Inu munandiveka ndi mphamvu yokachitira nkhondo, munachititsa kuti ndigonjetse adani anga.
40 Ti dušmane moje u bijeg natjera, i rasprših one koji su me mrzili.
Inu munachititsa adani anga kutembenuka, kuonetsa misana yawo pothawa, ndipo ine ndinawononga adani angawo.
41 Vapiju u pomoć - nikog da pomogne; vapiju Jahvi - ne odaziva se.
Iwo anafuwula kupempha thandizo, koma panalibe ndi mmodzi yemwe owapulumutsa. Analirira kwa Yehova koma sanawayankhe.
42 Smrvih ih kao prah na vjetru, zgazih ih k'o blato na putu.
Ine ndinawaperesa ngati fumbi lowuluka ndi mphepo. Ndinawapondaponda ngati matope a mʼmisewu.
43 Ti me izbavi od bune u mom narodu, postavi me glavarom pogana, puk koji ne poznavah služi mi.
Inu mwandipulumutsa mʼmanja mwa anthu; mwandisandutsa kukhala mtsogoleri wa anthu a mitundu ina. Anthu amene sindikuwadziwa ali pansi pa ulamuliro wanga.
44 Svaki moj šapat pokorno on sluša, sinovi tuđinci meni laskaju;
Alendo amadzipereka okha pamaso panga; akangomva za ine amandigonjera.
45 sinovi tuđinski gube srčanost, izlaze dršćuć' iz svojih utvrda.
Iwo onse anataya mtima; anatuluka mʼmalinga awo akunjenjemera.
46 Živio Jahve! Blagoslovljena hridina moja! Neka se uzvisi Bog, spasenje moje!
Yehova ndi wamoyo! Litamandidwe Thanthwe langa! Akuzike Mulungu Mpulumutsi wanga!
47 Bog koji mi daje osvetu i narode meni pokorava.
Iye ndi Mulungu amene amabwezera chilango, amene amagonjetsa anthu a mitundu yonse amene ali pansi pa ulamuliro wanga,
48 Od dušmana me mojih izbavljaš i nad protivnike me moje izdižeš, ti mene od čovjeka silnika spasavaš.
amene amandipulumutsa mʼmanja mwa adani anga. Inu munandikuza kuposa adani anga; munandilanditsa mʼmanja mwa anthu ankhanza.
49 Zato te slavim, Jahve, među pucima i psalam pjevam tvome Imenu:
Choncho ine ndidzakutamandani pakati pa anthu a mitundu ina, Inu Yehova; ndidzayimba nyimbo zotamanda dzina lanu.
50 umnožio si pobjede kralju svojemu, pomazaniku svome milost si iskazao, Davidu i potomstvu njegovu navijeke.
Iye amapereka chipambano chachikulu kwa mfumu yake; amaonetsa chikondi chosasinthika kwa wodzozedwa wake, kwa Davide ndi zidzukulu zake kwamuyaya.