< Psalmi 116 >
1 Ljubim Jahvu jer čuje vapaj molitve moje:
Ndimakonda Yehova pakuti Iyeyo amamva mawu anga; Iye amamva kulira kwanga kopempha chifundo.
2 uho svoje prignu k meni u dan u koji ga zazvah.
Pakuti ananditchera khutu, ndidzayitana Iye masiku onse a moyo wanga.
3 Užeta smrti sapeše me, stegoše me zamke Podzemlja, snašla me muka i tjeskoba. (Sheol )
Zingwe za imfa zinandizinga, zoopsa za ku dziko la anthu akufa zinandigwera; ndinapeza mavuto ndi chisoni. (Sheol )
4 Tada zazvah ime Jahvino: “O Jahve, spasi život moj!”
Pamenepo ndinayitana dzina la Yehova: “Inu Yehova, pulumutseni!”
5 Dobrostiv je Jahve i pravedan, pun sućuti je Bog naš.
Yehova ndi wokoma mtima ndi wolungama Mulungu wathu ndi wodzaza ndi chifundo.
6 Jahve čuva bezazlene: u nevolji bijah, on me izbavi.
Yehova amateteza munthu wodzichepetsa mtima; pamene ndinali ndi chosowa chachikulu, Iye anandipulumutsa.
7 Vrati se, dušo moja, u svoj pokoj, jer Jahve je dobrotvor tvoj.
Pumula iwe moyo wanga, pakuti Yehova wakuchitira zokoma.
8 On mi život od smrti izbavi, oči moje od suza, noge od pada.
Pakuti Inu Yehova mwapulumutsa moyo wanga ku imfa, maso anga ku misozi, mapazi anga kuti angapunthwe,
9 Hodit ću pred licem Jahvinim u zemlji živih.
kuti ine ndiyende pamaso pa Yehova mʼdziko la anthu amoyo.
10 Ja vjerujem i kada kažem: “Nesretan sam veoma.”
Ine ndinakhulupirira; choncho ndinati, “Ndasautsidwa kwambiri.”
11 U smetenosti svojoj rekoh: “Svaki je čovjek lažac!”
Ndipo ndili mʼnkhawa yanga ndinati, “Anthu onse ndi abodza.”
12 Što da uzvratim Jahvi za sve što mi je učinio?
Ndingamubwezere chiyani Yehova, chifukwa cha zokoma zake zonse zimene wandichitira?
13 Uzet ću čašu spasenja i zazvat ću ime Jahvino.
Ndidzakweza chikho cha chipulumutso ndipo ndidzayitana dzina la Yehova.
14 Izvršit ću Jahvi zavjete svoje pred svim pukom njegovim.
Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse.
15 Dragocjena je u očima Jahvinim smrt pobožnika njegovih.
Imfa ya anthu oyera mtima ndi yamtengowapatali pamaso pa Yehova.
16 Jahve, tvoj sam sluga, tvoj sluga, sin sluškinje tvoje: ti si razriješio okove moje.
Inu Yehova, zoonadi ndine mtumiki wanu: ndine mtumiki wanu, mwana wa mdzakazi wanu; Inu mwamasula maunyolo anga.
17 Tebi ću prinijeti žrtve zahvalne, zazvat ću ime Jahvino.
Ndidzapereka nsembe yachiyamiko kwa Inu ndipo ndidzayitanira pa dzina la Yehova.
18 Izvršit ću Jahvi zavjete svoje pred svim pukom njegovim,
Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse,
19 u predvorjima Doma Jahvina, posred tebe, Jeruzaleme!
mʼmabwalo a nyumba ya Yehova, mʼkati mwako iwe Yerusalemu. Tamandani Yehova.