< 2 Ljetopisa 32 >

1 Poslije tih događaja i dokaza vjernosti dođe asirski kralj Sanherib i, ušavši u Judeju, opkoli tvrde gradove misleći ih osvojiti.
Zitatha zonse zimene Hezekiya anachita mokhulupirika, Senakeribu mfumu ya ku Asiriya anabwera ndi kuthira nkhondo dziko la Yuda. Iye anazinga mizinda yotetezedwa ya Yuda, kuganiza kuti ayigonjetsa.
2 Ezekija, vidjevši gdje je došao Sanherib i kako snuje da zavojšti na Jeruzalem,
Pamene Hezekiya anaona kuti Senakeribu wabwera ndipo wakonzeka kuchita nkhondo ndi Yerusalemu,
3 posavjetova se s knezovima i s junacima da začepi vodene izvore koji bijahu izvan grada. Oni mu podupriješe osnovu.
iye anakambirana ndi akuluakulu ake pamodzi ndi atsogoleri a gulu lankhondo za kutseka akasupe ochoka ku kasupe amene anali kunja kwa mzinda, ndipo iwo anamuthandiza.
4 Sabralo se mnogo naroda te su začepili sva vrela i potok koji teče posred zemlje; govorahu: “Zašto da asirski kraljevi nađu toliko vode kad dođu!”
Gulu lalikulu la anthu linasonkhana, ndipo anatseka akasupe onse pamodzi ndi mtsinje umene umayenda mʼkati mwa nthakamo. Iwo ankanena kuti, “Nʼchifukwa chiyani mafumu a Asiriya akabwera kuno adzapeze madzi ambiri?”
5 Ezekija se osokolio, obnovio sav oboreni zid i podigao kule na njemu; izvana je sagradio drugi zid i utvrdio Milon u Davidovu gradu; napravio je mnogo kopalja i štitova,
Kenaka iye anagwira ntchito molimbika kukonza madera ogumuka a khoma ndi kumangapo msanja. Anamanganso mpanda wina kunja kwa mpanda winawo ndipo anamanga zolimbitsa Milo ku mzinda wa Davide.
6 zatim postavio vojvode nad narodom i, pozvavši ih k sebi na trg kraj gradskih vrata, ohrabri ih ovim riječima:
Iye anasankha atsogoleri a ankhondo olamulira anthu ndipo anawasonkhanitsa pamaso pake pa bwalo la chipata cha mzinda ndi kuwalimbikitsa ndi mawu awa:
7 “Budite hrabri i junaci; ne bojte se i ne plašite se asirskoga kralja, ni svega mnoštva što je s njim, jer je s nama moćniji nego s njim:
“Khalani amphamvu ndi olimba mtima. Musachite mantha kapena kutaya mtima chifukwa cha mfumu ya ku Asiriya ndi gulu lalikulu lankhondo limene ali nalo, pakuti ife tili ndi mphamvu yayikulu kuposa imene ili ndi iye.
8 s njim je tjelesna mišica, a s nama je Jahve, Bog naš, da nam pomaže i da bije naše bojeve.” Narod se uzda u riječi judejskoga kralja Ezekije.
Iye ali ndi mphamvu ya anthu basi, koma ife tili ndi Yehova Mulungu wathu kutithandiza ndi kuchita nkhondo zathu.” Ndipo anthu anapeza chilimbikitso kuchokera pa zimene Hezekiya mfumu ya Yuda ananena.
9 Poslije toga asirski je kralj Sanherib, dok bijaše kod Lakiša sa svom bojnom silom, poslao sluge u Jeruzalem k judejskome kralju Ezekiji i k svim Judejcima koji bijahu u Jeruzalemu i poručio im:
Nthawi ina, pamene Senakeribu mfumu ya ku Asiriya ndi gulu lake lonse lankhondo anali atazinga Lakisi, iye anatumiza atsogoleri ake ankhondo ku Yerusalemu ndi uthenga uwu kwa Hezekiya mfumu ya Yuda ndi anthu onse a ku Yuda amene anali kumeneko:
10 “Ovako veli asirski kralj Sanherib: 'U što se uzdate stojeći opsjednuti u Jeruzalemu?
“Senakeribu mfumu ya ku Asiriya akuti: Kodi inu mukukhulupirira chiyani, kuti mukukhalabe mu Yerusalemu mutazingidwa?
11 Ne zavodi li vas Ezekija da vas preda smrti od gladi i žeđi kad govori: Jahve, Bog naš, izbavit će nas iz ruke asirskoga kralja?
Pamene Hezekiya akunena kuti ‘Yehova Mulungu wathu adzatipulumutsa kuchoka mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya,’ iye akukusocheretsani, kuti mufe ndi njala ndi ludzu.
12 Nije li taj Ezekija uklonio njegove uzvišice i njegove žrtvenike; i zapovjedio Judejcima i Jeruzalemcima govoreći: Pred jednim se žrtvenikom klanjajte i na njemu kadite!
Kodi si Hezekiya amene anachotsa malo opembedzerapo Mulungu ameneyu ndi maguwa ansembe ndi kunena kwa anthu a ku Yuda ndi Yerusalemu kuti, ‘Muzipembedza pa guwa lansembe limodzi ndi kupserezapo nsembe?’
13 Zar ne znate što sam učinio ja i moji preci od svih zemaljskih naroda? Zar su bogovi zemaljskih naroda mogli izbaviti svoje zemlje iz moje ruke?
“Kodi inu simukudziwa zimene ine ndi makolo anga tachita kwa anthu a mitundu ina? Kodi milungu ya mitundu imeneyi inatha kupulumutsa dziko lawo kuchoka mʼdzanja langa?
14 Koji je među svim bogovima onih naroda što su ih sasvim uništili moji preci mogao izbaviti narod iz moje ruke, da bi mogao vaš Bog izbaviti vas iz moje ruke?'
Kodi ndi milungu iti mwa milungu ya mitundu ina ya anthuwo, imene makolo anga anayiwononga kotheratu, inatha kupulumutsa anthu ake mʼdzanja langa? Nanga tsono Mulungu wanuyo adzakupulumutsani mʼdzanja langa motani?
15 Zato nemojte da vas sada Ezekija vara i da vas tako zavodi i ne vjerujte mu! Jer nijedan bog nikojega naroda ili kraljevstva nije mogao izbaviti svoga naroda iz moje ruke, ni iz ruke mojih predaka, a kamoli će vaš Bog izbaviti vas iz moje ruke!”
Choncho inu musalole kuti Hezekiya akunamizeni ndi kukusocheretsani motere. Musamukhulupirire, pakuti palibe mulungu wa mtundu wina uliwonse kapena ufumu wina uliwonse umene unatha kupulumutsa anthu ake kuchoka mʼdzanja langa kapena mʼdzanja la makolo anga. Nanga bwanji Mulungu wanuyo, sadzatha kukupulumutsani kuchoka mʼdzanja langa!”
16 Još su više njegove sluge napadale Boga Jahvu i njegova slugu Ezekiju.
Atsogoleri a ankhondo a Senakeribu anapitiriza kuyankhula zotsutsana ndi Yehova Mulungu ndi mtumiki wake Hezekiya.
17 Napisao je i pismo ružeći Jahvu, Izraelova Boga: “Kao što bogovi zemaljskih naroda nisu izbavili svojih naroda iz moje ruke, tako neće ni Ezekijin Bog izbaviti svojega naroda iz moje ruke.”
Mfumunso inalemba makalata onyoza Yehova, Mulungu wa Israeli, ndipo inanena zotsutsana naye izi: “Monga momwe milungu ya anthu a mayiko ena sinathe kuwapulumutsa kuchoka mʼdzanja langa, chonchonso Mulungu wa Hezekiya sadzapulumutsa anthu ake kuchoka mʼdzanja langa.”
18 I vikahu iza glasa, na judejskom jeziku, jeruzalemskom narodu koji bijaše na zidu da ga uplaše i prepadnu kako bi osvojili grad.
Kenaka iwo anafuwula mu Chihebri kwa anthu a mu Yerusalemu amene anali pa khoma, kuwaopseza ndi kuwachititsa mantha ndi cholinga choti alande mzindawo.
19 Govorili su o jeruzalemskom Bogu kao o bogovima zemaljskih naroda, bogovima koji su djelo čovječjih ruku.
Iwo anayankhula za Mulungu wa Yerusalemu monga anayankhulira za milungu ya anthu ena a pa dziko lapansi, ntchito ya manja a anthu.
20 Stoga se pomoli kralj Ezekija i prorok Izaija, Amosov sin, i zazvaše nebo u pomoć.
Mfumu Hezekiya ndi mneneri Yesaya mwana wa Amozi anafuwulira kumwamba mʼpemphero chifukwa cha zimenezi.
21 Tada Jahve posla anđela koji uništi sve hrabre junake, zapovjednike i vojvode u vojsci asirskoga kralja, tako da se vratio posramljen u svoju zemlju. A kad je ušao u hram svoga boga, sasjekli su ga ondje mačem neki koji su se rodili iz njegova krila.
Ndipo Yehova anatumiza mngelo amene anadzapha anthu onse odziwa nkhondo ndi atsogoleri ndiponso oyangʼanira misasa ya mfumu ya ku Asiriya. Choncho Senakeribu anabwerera kwawo wamanyazi. Ndipo atalowa mʼnyumba ya mulungu wake, ena mwa ana ake anamupha ndi lupanga.
22 Tako je Jahve spasio Ezekiju i jeruzalemske stanovnike od ruke asirskoga kralja Sanheriba i iz ruku neprijatelja, te im dao mir odasvud uokolo.
Kotero Yehova anapulumutsa Hezekiya ndi anthu a ku Yerusalemu kuchoka mʼdzanja la Senakeribu mfumu ya ku Asiriya ndi mʼdzanja la anthu ena. Yehova anawateteza ku mbali zonse.
23 Mnogi su donosili darove Jahvi u Jeruzalem i dragocjenosti judejskome kralju Ezekiji. Poslije toga Ezekija se uzvisio u očima svih naroda.
Anthu ambiri anabweretsa zopereka kwa Yehova ku Yerusalemu ndi mphatso zamtengowapatali kwa Hezekiya mfumu ya Yuda. Kuyambira nthawi imeneyo Hezekiya ankalemekezedwa kwambiri ndi mitundu ina yonse.
24 U to se vrijeme Ezekija razbolio nasmrt, ali se pomolio Jahvi, koji mu je progovorio i učinio čudo.
Pa nthawi imeneyo Hezekiya anadwala ndipo anali pafupi kufa. Iye anapemphera kwa Yehova, amene anamuyankha ndi kumupatsa chizindikiro chodabwitsa.
25 Ali se Ezekija nije odužio dobročinstvu koje mu je iskazano, nego se uzoholio; stoga je došla srdžba na nj, na Judu i na Jeruzalem.
Koma Hezekiya anali ndi mtima wonyada ndipo sanachite molingana ndi kukoma mtima kumene Mulungu anamuonetsera. Choncho mkwiyo wa Yehova unali pa iye ndi pa Yuda ndi Yerusalemu.
26 Ezekija se ponizio zato što mu se bilo uzoholilo srce, i on i Jeruzalemci, pa tako nije došla na njih Jahvina srdžba za Ezekijina života.
Koma kenaka Hezekiya analapa za kunyada kwakeko, monga anachitanso anthu a mu Yerusalemu. Choncho mkwiyo wa Yehova sunafike pa iwo pa nthawi ya Hezekiya.
27 Ezekija je stekao vrlo veliko bogatstvo i slavu; napravio je riznice za srebro i zlato, za drago kamenje, za miomirise, za štitove i za svakojake dragocjene posude;
Hezekiya anali ndi chuma ndi ulemu wambiri ndipo anamanga nyumba zosungiramo chuma cha siliva wake ndi golide ndi za miyala yokongola, zokometsera zakudya, zishango ndi mtundu uliwonse wa zinthu zamtengowapatali.
28 skladište za prirod od žita, od novog vina i ulja, staje za svakojaku stoku, torove za stada.
Iye anamanganso nyumba zosungiramo tirigu, vinyo watsopano ndi mafuta a olivi, ndiponso anamanga nyumba zodyeramo ngʼombe zosiyanasiyana, ndi makola a nkhosa.
29 Podigao je i gradove, imao je mnogo blaga, sitne stoke i goveda, jer mu je Bog dao vrlo veliko imanje.
Iyeyo anamanga midzi ndipo anali ndi nkhosa ndi ngʼombe zambiri, pakuti Mulungu anamupatsa chuma chambiri.
30 Isti je Ezekija začepio gornji izvor Gihonske vode i svrnuo je pravo na zapadnu stranu Davidova grada. Ezekija je bio sretan u svakom poslu.
Ndi Hezekiya amene anatseka ku mtunda kwa kasupe wa Gihoni, ndi kumuwongolera kuti madzi ake apite mbali ya kumadzulo kwa Mzinda wa Davide. Iye ankachita bwino pa ntchito iliyonse imene ankagwira.
31 Samo kad su došli poslanici babilonskih knezova, poslani k njemu da se propitaju za čudo koje se dogodilo u zemlji, ostavio ga je Bog da bi ga iskušao i da bi se doznalo sve što mu je u srcu.
Koma pamene nthumwi zotumizidwa ndi atsogoleri a ku Babuloni zinabwera kudzamufunsa za chizindikiro chozizwitsa chimene chinachitika mʼdzikomo, Mulungu anamusiya yekha, kumuyesa kuti adziwe zonse zimene zinali mu mtima mwake.
32 Ostala Ezekijina djela, njegova pobožnost, zapisani su u proročkom viđenju proroka Izaije, Amosova sina, i u Knjizi o judejskim i izraelskim kraljevima.
Zina ndi zina zokhudza ulamuliro wa Hezekiya ndi ntchito za kudzipereka kwake zalembedwa mʼmasomphenya a Yesaya mwana wa Amozi, mʼbuku la mafumu a Yuda ndi Israeli.
33 Ezekija je počinuo kod svojih otaca. Sahranili su ga na usponu kako se ide ka grobovima Davidovih sinova. Po smrti su mu odali počast svi Judejci i Jeruzalemci. Na njegovo se mjesto zakraljio sin mu Manaše.
Hezekiya anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pa phiri pamene pali manda a zidzukulu za Davide. Ayuda onse ndi anthu a mu Yerusalemu anamulemekeza atamwalira. Ndipo Manase mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.

< 2 Ljetopisa 32 >