< 历代志上 24 >

1 亚伦子孙的班次记在下面:亚伦的儿子是拿答、亚比户、以利亚撒、以他玛。
Magulu a ana a Aaroni anali awa: Ana a Aaroni anali Nadabu, Abihu, Eliezara ndi Itamara.
2 拿答、亚比户死在他们父亲之先,没有留下儿子;故此,以利亚撒、以他玛供祭司的职分。
Koma Nadabu ndi Abihu anamwalira abambo awo asanamwalire, ndipo analibe ana aamuna. Kotero Eliezara ndi Itamara ankatumikira monga ansembe.
3 以利亚撒的子孙撒督和以他玛的子孙亚希米勒,同着大卫将他们的族弟兄分成班次。
Mothandizidwa ndi Zadoki chidzukulu cha Eliezara ndi Ahimeleki chidzukulu cha Itamara, Davide anawagawa mʼmagulu molingana ndi ntchito yawo yotumikira.
4 以利亚撒子孙中为首的比以他玛子孙中为首的更多,分班如下:以利亚撒的子孙中有十六个族长,以他玛的子孙中有八个族长;
Atsogoleri ambiri anapezeka pakati pa zidzukulu za Eliezara kusiyana ndi zidzukulu za Itamara ndipo anagawidwa moyenera: atsogoleri 16 a mabanja ochokera kwa Eliezara, ndipo atsogoleri asanu ndi atatu a mabanja ochokera kwa zidzukulu za Itamara.
5 都掣签分立,彼此一样。在圣所和 神面前作首领的有以利亚撒的子孙,也有以他玛的子孙。
Anawagawa mosakondera pochita maere, pakuti iwo anali akuluakulu a ku malo opatulika ndi akuluakulu a Mulungu pakati pa zidzukulu za Eliezara ndi Itamara.
6 作书记的利未人拿坦业的儿子示玛雅在王和首领,与祭司撒督、亚比亚他的儿子亚希米勒,并祭司利未人的族长面前记录他们的名字。在以利亚撒的子孙中取一族,在以他玛的子孙中取一族。
Mlembi Semaya mwana wa Netaneli, Mlevi, analemba mayina awo pamaso pa mfumu ndi akuluakulu ake: wansembe Zadoki, Ahimeleki mwana wa Abiatara ndi atsogoleri a mabanja a ansembe ndiponso Alevi, banja limodzi kuchokera kwa Eliezara kenaka limodzi kuchokera kwa Itamara.
7 掣签的时候,第一掣出来的是耶何雅立,第二是耶大雅,
Maere woyamba anagwera Yehoyaribu, achiwiri anagwera Yedaya,
8 第三是哈琳,第四是梭琳,
achitatu anagwera Harimu, achinayi anagwera Seorimu,
9 第五是玛基雅,第六是米雅民,
achisanu anagwera Malikiya, achisanu ndi chimodzi anagwera Miyamini,
10 第七是哈歌斯,第八是亚比雅,
achisanu ndi chiwiri anagwera Hakozi, achisanu ndi chitatu anagwera Abiya,
11 第九是耶书亚,第十是示迦尼,
achisanu ndi chinayi anagwera Yesuwa, a khumi anagwera Sekaniya,
12 第十一是以利亚实,第十二是雅金,
a 11 anagwera Eliyasibu, a 12 anagwera Yakimu,
13 第十三是胡巴,第十四是耶是比押,
a 13 anagwera Hupa, a 14 anagwera Yesebeabu,
14 第十五是璧迦,第十六是音麦,
a 15 anagwera Biliga, a 16 anagwera Imeri,
15 第十七是希悉,第十八是哈辟悉,
a 17 anagwera Heziri, a 18 anagwera Hapizezi,
16 第十九是毗他希雅,第二十是以西结,
a 19 anagwera Petahiya, a 20 anagwera Ezekieli,
17 第二十一是雅斤,第二十二是迦末,
a 21 anagwera Yakini, a 22 anagwera Gamuli,
18 第二十三是第来雅,第二十四是玛西亚。
a 23 anagwera Delaya, ndipo a 24 anagwera Maaziya.
19 这就是他们的班次,要照耶和华—以色列的 神借他们祖宗亚伦所吩咐的条例进入耶和华的殿办理事务。
Umu ndi mmene anasankhidwira kuti azigwira ntchito yotumikira pamene alowa mʼNyumba ya Yehova, motsatira dongosolo limene anapatsidwa ndi kholo lawo Aaroni, monga momwe Yehova Mulungu wa Israeli anamulamulira.
20 利未其余的子孙如下:暗兰的子孙里有书巴业;书巴业的子孙里有耶希底亚。
Za zidzukulu zina zonse za Levi: Kuchokera kwa ana a Amramu: Subaeli; kuchokera kwa ana a Subaeli: Yehideya.
21 利哈比雅的子孙里有长子伊示雅。
Kwa Rehabiya, kuchokera kwa ana ake: Mtsogoleri anali Isiya.
22 以斯哈的子孙里有示罗摩;示罗摩的子孙里有雅哈。
Kuchokera ku banja la Izihari: Selomoti; kuchokera kwa ana a Selomoti: Yahati.
23 希伯伦 的子孙里有长子耶利雅,次子亚玛利亚,三子雅哈悉,四子耶加面。
Ana a Hebroni: woyamba anali Yeriya, wachiwiri anali Amariya, wachitatu anali Yahazieli ndipo Yekameamu anali wachinayi.
24 乌薛的子孙里有米迦;米迦的子孙里有沙密。
Mwana wa Uzieli: Mika; kuchokera kwa ana a Mika: Samiri.
25 米迦的兄弟是伊示雅;伊示雅的子孙里有撒迦利雅。
Mʼbale wa Mika: Isiya; kuchokera kwa ana a Isiya: Zekariya.
26 米拉利的儿子是抹利、母示、雅西雅;雅西雅的儿子有比挪;
Ana a Merari: Mahili ndi Musi. Mwana wa Yaaziya: Beno.
27 米拉利的子孙里有雅西雅的儿子比挪、朔含、撒刻、伊比利。
Ana a Merari: Kuchokera kwa Yaaziya: Beno, Sohamu, Zakuri ndi Ibiri.
28 抹利的儿子是以利亚撒;以利亚撒没有儿子。
Kuchokera kwa Mahili: Eliezara, amene analibe ana aamuna.
29 基士的子孙里有耶拉篾。
Kuchokera kwa Kisi: Mwana wa Kisi: Yerahimeeli.
30 母示的儿子是末力、以得、耶利摩。按着宗族这都是利未的子孙。
Ndipo ana a Musi: Mahili, Ederi ndi Yerimoti. Awa anali Alevi potsata mabanja a makolo awo.
31 他们在大卫王和撒督,并亚希米勒与祭司利未人的族长面前掣签,正如他们弟兄亚伦的子孙一般。各族的长者与兄弟没有分别。
Iwonso anachita maere, monga anachitira abale awo, zidzukulu za Aaroni, pamaso pa mfumu Davide, ndi Zadoki ndi Ahimeleki, atsogoleri a mabanja a ansembe ndi Alevi. Mabanja a mwana wamkulu anachita nawo mofanana ndi a mwana wamngʼono.

< 历代志上 24 >