< Tingtoeng 77 >

1 Jeduthun te aka mawt ham Asaph kah Jeduthun tingtoenglung Pathen taengah ka ol ka huel tih ka pang. Pathen taengah ka ol ka huel tih kai taengla a hna han kaeng.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a Yedutuni. Salimo la Asafu. Ndinafuwulira Mulungu kupempha thandizo; ndinafuwula mokweza kwa Mulungu kuti anditcherere khutu.
2 Ka citcai tue vaengah ka Boeipa ka toem. Khoyin ah ka ban ka lam tih kha tlaih pawh. Ka hinglu hloep ham a aal.
Pamene ndinali pa masautso ndinafunafuna Ambuye; usiku ndinatambasula manja mosalekeza ndipo moyo wanga unakana kutonthozedwa.
3 Pathen ka ngaidam tih ka ko. Lolmang ka taeng vaengah ka mueihla rhae.
Ndinakumbukira Inu Mulungu, ndipo ndinabuwula; ndinasinkhasinkha ndipo mzimu wanga unalefuka. (Sela)
4 Ka mikhmuh ah miklung nan buem tih kai n'cahoeh he ka thui lek pawh. (Selah)
Munagwira zikope zanga kuti ndisagone ndipo ndinavutika kwambiri kuti ndiyankhule.
5 Khosuen hlamat kum kah khohnin te ka poek.
Ndinaganizira za masiku akale, zaka zamakedzana;
6 Khoyin ah ka rhotoeng ka ngaidam. Ka thinko ah lolmang ka taeng tih ka mueihla a sat.
Ndinakumbukira nyimbo zanga usiku. Mtima wanga unasinkhasinkha ndipo mzimu wanga unafunsa kuti,
7 Ka Boeipa loh kumhal duelam nim n'hlahpham vetih koekthoek kan doe bal eh ti voel pawt nim?
“Kodi Ambuye adzatikana mpaka muyaya? Kodi Iwo sadzaonetsanso kukoma mtima kwawo?
8 A sitlonah loh a yoeyah la a toeng vetih a olkhueh loh cadilcahma phoeikah cadilcahma ham bawtpat pawn a ya?
Kodi Chikondi chake chosatha chija chatheratu? Kodi malonjezo ake alephera nthawi yonse?
9 Pathen loh sitlohthamlam ham a hnilh tih a haidamnah te thintoek loh a uep bal nim? (Selah)
Kodi Mulungu wayiwala kukhala wokoma mtima? Kodi mu mkwiyo wake waleka chifundo chake?”
10 Ka nue coeng ka ti vaengah he Khohni kah bantang kut loh n'talh.
Ndipo ndinaganiza, “Pa izi ine ndidzapemphanso: zaka za dzanja lamanja la Wammwambamwamba.
11 BOEIPA kah khoboe tah ka ngaidam rhoe ka ngaidam pai tih hlamat lamkah na khobaerhambae khaw ka ngaidam.
Ine ndidzakumbukira ntchito za Yehova; Ine ndidzakumbukira zodabwitsa zanu za kalekale.
12 Te dongah na bisai boeih te ka thuep vetih na bibi boeih te lolmang ka taeng puei ni.
Ndidzakumbukira ntchito zanu ndi kulingalira zodabwitsa zanu.”
13 Pathen namah kah longpuei cim ah mebang pathen lae Pathen bangla aka tanglue bal?
Njira zanu Mulungu ndi zoyera. Kodi ndi mulungu uti ali wamkulu kuposa Mulungu wathu?
14 “Khobaerhambae aka saii Pathen namah loh pilnam rhoek taengah na sarhi khaw na tueng sak.
Inu ndinu Mulungu wochita zodabwitsa; Mumaonetsera mphamvu yanu pakati pa mitundu ya anthu.
15 Na pilnam Jakob neh Joseph koca te bantha neh na tlan. (Selah)
Ndi dzanja lanu lamphamvu munawombola anthu anu, zidzukulu za Yakobo ndi Yosefe. (Sela)
16 Tui rhoek loh Pathen namah m'hmuh uh. Tui rhoek loh namah m'hmuh uh vaengah kilkul uh tih a laedil pataeng tlai.
Madzi anakuonani Mulungu, madzi anakuonani ndipo anachita mantha; nyanja yozama inakomoka.
17 Khomai loh tui han hawk. Khomong khaw a ol hum. Na thaltang rhoek khaw thui.
Mitambo inakhuthula madzi ake pansi, mu mlengalenga munamveka mabingu; mivi yanu inawuluka uku ndi uku.
18 Humhae khui lamkah na khohum ol ah rhaek la phaa tih lunglai khaw tlai coeng, diklai khaw hinghuen coeng.
Bingu lanu linamveka mʼmphepo ya kamvuluvulu, mphenzi yanu inawalitsa dziko lonse; dziko lapansi linanjenjemera ndi kugwedezeka.
19 Tuitunli dongkah na longpuei neh tui puei dongah khaw na lamkat patoeng, lamkat patoeng om dae na kholaeh ming uh pawh.
Njira yanu inadutsa pa nyanja, njira yanu inadutsa pa madzi amphamvu, ngakhale zidindo za mapazi anu sizinaoneke.
20 Na pilnam te Moses kut, Aaron kut neh tuping bangla na mawt.
Inu munatsogolera anthu anu ngati gulu la nkhosa mwa dzanja la Mose ndi Aaroni.

< Tingtoeng 77 >