< Isaiah 28 >

1 Anunae, Ephraim yurhui rhoek kah rhimomnah rhuisam neh a boeimang kirhang kah tamlaep khaw tahah coeng. Te te laimen kolrhawk kah a lu ah misurtui neh a thoek uh dae ta.
Tsoka ufumu wonyada wa zidakwa za ku Efereimu. Tsoka kwa ulemerero wake wokongola umene ukufota ngati duwa limene lili pa mutu pa anthu oledzera a mʼchigwa chachonde.
2 Boeipa taengkah tlungluen neh rhapsat la aka om tah rhaelnu khohli, lucik hlithae, cingtui tui rhilh bangla a yo te khaw a kut neh diklai la a tloeng ni.
Taonani, ambuye ali naye wina wamphamvu ndi nyonga. Iye adzabwera ngati mkuntho wamatalala ndi namondwe wowononga, ngati madzi amphamvu osefukira a mvula yamkuntho; ndipo adzawagwetsa pansi mwankhanza.
3 Ephraim yurhui kah rhimomnah rhuisam te a kho hmuiah a taelh uh ni.
Ulamuliro wa atsogoleri oledzera a ku Efereimu adzawuthetsa.
4 Laimen kolrhawk lu kah a boeimang kirhang rhaipai bangla aka hoo te khohal hlan kah thaihloe bangla om ni. Te te aka hmuh la aka hmuh dongah a kut nen khaw pahoi a dolh.
Ndipo ulemerero wokongola wa mzinda umene uli ngati duwa lofota pamutu pa anthu oledzera a mʼchigwa chachonde uja, udzakhala ngati nkhuyu yoyambirira kupsa imene munthu akangoyiona amayithyola nthawi yokolola isanakwane.
5 Tekah khohnin ah tah caempuei BOEIPA te, a pilnam aka sueng ham kirhang rhuisam la, boeimang cangen la om ni.
Tsiku limenelo Yehova Wamphamvuzonse adzakhala ngati nkhata yaufumu, chipewa chokongola kwa anthu ake otsala.
6 Laitloeknah dongah aka ngol ham tiktamnah mueihla la, caemtloek kah vongka ah aka mael tak kah thayung thamal la om ni.
Iye adzapereka mtima wachilungamo kwa oweruza, adzakhala chilimbikitso kwa amene amabweza adani pa zipata za mzinda.
7 Te rhoek khaw misurtui loh a palang sak. Khosoih neh tonghma khaw yu dongah taengphael uh. Yu dongah palang uh tih misur dongah bol uh. Yu dongah kho a hmang uh. Khohmu lamloh palang uh tih laitloek dongah lol uh.
Nawonso awa ali dzandidzandi chifukwa cha vinyo ndipo akusochera chifukwa cha mowa: ansembe ndi aneneri akudzandira chifukwa cha mowa ndipo akusokonezeka chifukwa cha vinyo; akusochera chifukwa cha mowa, akudzandira pamene akuona masomphenya, kupunthwa pamene akupereka chigamulo.
8 Caboei tom te a lok kah a khawt baetawt la a hmuen tal.
Pa matebulo onse pali masanzi okhaokha ndipo palibenso malo wopanda zonyansa.
9 Lungming la a thuinuet te unim, olthang aka yakming sak te unim? Rhangsuk lamloh tampo suktui aka kan te.
Iwo akuti, “Kodi munthu ameneyu akufuna aphunzitse ndani? Uthengawu akufuna kufotokozera yani? Ndi kwa ana amene aleka kuyamwa, kwa makanda ongowachotsa kumene ku bere?
10 Olrhi soah olrhi te olrhi sokah olrhi neh, rhilam sokah rhilam te rhilam phoeikah rhilam neh hela vel, kela vel a ti.
Akuyesa kumatiphunzitsa pangʼonopangʼono lemba ndi lemba, mzere ndi mzere, phunziro ndi phunziro. Zonsezi akungoti apa pangʼono apa pangʼono.”
11 Te dongah hekah pilnam he tamdaengtamkha kah hmuilai neh, ol tloe neh a voek ni.
Mulungu adzayankhula kwa anthu ake kudzera mwa anthu aziyankhulo zachilendo, ziyankhulo zosamveka bwino. Mulungu adzayankhula kwa anthu awa, amene
12 Amah loh amih taengah, “Hekah duemnah dongah buhmueh rhahthih te duem saeh lamtah hilhoemnah he om saeh,” a ti nah. Tedae hnatun ham a ngaih uh moenih.
anakuwuzani kuti, “Malo opumulira ndi ano, otopa apumule, malo owusira ndi ano.” Koma inu simunamvere.
13 Te dongah BOEIPA ol loh amih taengah olrhi sokah olrhi patoeng loh, olrhi phoeikah olrhi a tloe loh, rhilam sokah rhilam loh, rhilam phoeikah rhilam pakhat loh hela vel, kela vel om ni. Te daengah ni cet uh vetih a hnuk la a palet uh eh. Te vaengah khaem uh vetih a hlaeh uh ni, a tuuk uh ni.
Choncho Yehova adzakuphunzitsani pangʼonopangʼono lemba ndi lemba, mzere ndi mzere, phunziro ndi phunziro. Kotero mudzayenda ndi kugwa chambuyo, adzapweteka ndi kukodwa mu msampha ndipo adzakutengani ku ukapolo.
14 Te dongah saipaat Jerusalem kah pilnam aka ngol thil hlang rhoek loh BOEIPA ol te ya uh lah.
Nʼchifukwa chake imvani mawu a Yehova, inu anthu achipongwe amene mumalamulira anthu awa mu Yerusalemu.
15 “Dueknah neh paipi ka saii uh tih saelkhui taengah khohmu khaw ka khueh uh coeng. Mueirhih loh lawngkaih rhuihet la a vikvuek tih pongpa khaw pongpa mai saeh, mamih taengla ha pawk mahpawh. Laithae he mamih kah hlipyingnah la n'khueh uh tih a honghi khuiah n'thuh uh coeng,” na ti uh. (Sheol h7585)
Inu mumayankhula monyada kuti, “Ife tinachita pangano ndi imfa, ife tachita mgwirizano ndi manda. Pamene mliri woopsa ukadzafika sudzatikhudza ife, chifukwa timadalira bodza ngati pothawirapo pathu ndi chinyengo ngati malo anthu obisalapo.” (Sheol h7585)
16 Te dongah ka Boeipa Yahovah loh he a thui. Zion kah lungto, nuemnainah lungto aka tloeng khaw kamah ni he. Bangkil te lung vang tungkho a suen tih aka tangnah rhoek te tamto uh mahpawh.
Tsono zimene Ambuye Yehova akunena ndi izi: “Taonani, ndikuyika mwala wovomerezeka ndi amisiri ngati maziko mu Ziyoni, mwala wapangodya, wamtengowapatali wopanga maziko amphamvu; munthu amene awukhulupirira sadzagwedezeka.
17 Tiktamnah he rhilam la, duengnah te mikrhael la ka khueh ni. Hlipyingnah laithae te rhaelnu loh a hnut vetih a huephael tui a yo pah ni.
Ntchito zolungama zidzakhala ngati chingwe choyezera maziko ake, ndipo chilungamo chidzakhala chowongolera mzere; matalala adzawononga malo anu othawirapo, amene ndi mabodza, ndipo madzi adzamiza malo anu obisalako.
18 Dueknah taengkah na paipi loh n'dawth vetih saelkhui taengkah na mangthui khaw thoo mahpawh. Mueirhih rhuihet loh vikvuek uh tih m'pah vaengah te kah a cawtkoi la na om ni. (Sheol h7585)
Pangano limene munachita ndi imfa lidzathetsedwa; mgwirizano wanu ndi manda udzachotsedwa. Pakuti mliri woopsa udzafika, ndipo udzakugonjetsani. (Sheol h7585)
19 Te te ha pawk carhil nen te nangmih ngawn tah mincang, mincang ah n'loh ni. Khothaih ah khaw khoyin ah khaw m'pah vetih olthang n'yakming te tonganah la om ni.
Ndipo ukadzangofika udzakutengani. Udzafika mmawa uliwonse, usiku ndi usana.” Anthu akadzamvetsetsa uthenga umenewu adzaopsedwa kwambiri.
20 Khawk sak hamla thingkong te a rhaem pah tih, a calui ham mueihloe te khaw a yaem pah.
Mudzakhala ngati munthu wogona pa bedi lalifupi kwambiri kuti sangathe kutambalitsapo miyendo; ndiponso mudzakhala ngati munthu amene wafunda bulangeti lochepa kwambiri kuti sangathe nʼkufunda komwe.
21 Perazim tlang kah bangla BOEIPA te thoo ni. Gibeon kol kah bangla a bibi saii ham tlai ni. A bibi he lang tih a thothuengnah tah kholong kah a thothuengnah bangla thothueng ham ni.
Yehova adzamenya nkhondo monga anachitira ku phiri la Perazimu adzakalipa monga anachitira ku chigwa cha Gibiyoni; adzagwira ntchito yake yooneka ngati yachilendo, ndipo zimene ati adzachite zidzakhala ngati zodabwitsa.
22 Hmuiyoi voel boeh, namah kah kuelrhui loh m'ven ve. Khohmuen tom a boeihnah neh pha vitvawt he ka Boeipa caempuei Yahovah taeng lamkah ka yaak coeng.
Tsopano lekani kunyoza, mukapanda kutero maunyolo anu adzakuthinani kwambiri; Ambuye, Yehova Wamphamvuzonse wandiwuza kuti, “Ndagamula kuti ndidzawononga dziko lapansi.”
23 Ka ol he hnakaeng lamtah ya uh lah, ka olthui he hnatung lamtah ya uh lah.
Tcherani khutu ndipo mumve mawu anga; mvetserani ndipo mumve zimene ndikunena.
24 Lotawn ham lo aka yoe loh hnin takuem a yoe a? A khohmuen te a yawt tih a thoe ta.
Kodi mlimi wofuna kudzala mbewu amangokhalira kutipula kokhakokha? Kodi amangokhalira kugawula ndi kugalawuza kokhakokha?
25 A hman te a hnil moenih a? Tlangsungsing a phul tih sungsing khaw a haeh. Cang te a kok dongah a phung tih a rhibawn ah cangtun neh cangkuem a duen ta.
Pamene iye wasalaza mundawo, kodi samafesa mawere ndi chitowe? Kodi suja samadzala tirigu ndi barele mʼmizere yake, nadzala mchewere mʼphepete mwa mundawo?
26 Anih te a toel vaengah a Pathen kah tiktamnah te a taengah a thuinuet pah.
Mulungu wake amamulangiza ndi kumuphunzitsa njira yabwino.
27 Tlangsungsing te thingphael neh a boh tih sungsing te leng kho neh a kuelh thil moenih. Tedae tlangsungsing te caitueng neh, sungsing te conghol neh a boh ta.
Mawere sapunthira chopunthira cha galeta lopanda mikombero, kapena chitowe sapuntha popondetsapo mikombero ya galeta; mawere amapuntha ndi ndodo ndipo chitowe amapuntha ndi kamtengo.
28 Buh khaw tip coeng dae a yoeyah la nook mahpawh. Te te a boh vaengah a leng kho neh a khawkkhek thil moenih. A marhang caem neh a tip sak moenih.
Tirigu ayenera kusinjidwa kuti apangire buledi, komabe munthu samangokhalira kupuntha tiriguyo osalekeza, kuopa kuti angatekedzeke. Ngakhale kuti amapuntha tiriguyo poyendetsapo mikombero ya galeta, koma akavalo ake satekedza tiriguyo.
29 He khaw caempuei BOEIPA taeng lamkah ni. Amah kah cilsuep tah khobaerhambae la ha pawk tih a lungming cueihnah a pantai sak.
Izinso zimachokera kwa Yehova Wamphamvuzonse, wa uphungu wodabwitsa ndi wa nzeru zopambana.

< Isaiah 28 >