< Zekariya 6 >

1 Ndinayangʼananso ndipo taonani ndinaona magaleta anayi akutuluka pakati pa mapiri awiri, mapiri amkuwa.
Againe, I turned and lift vp mine eyes, and looked: and beholde, there came foure charets out from betweene two mountaines, and the mountaines were mountaines of brasse.
2 Galeta loyamba limakokedwa ndi akavalo ofiira, lachiwiri ndi akavalo akuda,
In the first charet were red horses, and in the second charet blacke horses,
3 lachitatu ndi akavalo oyera, ndipo lachinayi ndi akavalo otuwa a mawanga ofiirira, onsewa anali akavalo amphamvu kwambiri.
And in the thirde charet white horses, and in the fourth charet, horses of diuers colours, and reddish.
4 Ndinafunsa mngelo amene amayankhula nane uja kuti, “Kodi mbuye wanga chimenechi nʼchiyani?”
Then I answered, and saide vnto the Angell that talked with mee, What are these, my Lord?
5 Mngeloyo anandiyankha kuti, “Imeneyi ndi mizimu inayi yakumwamba, imene ikuchokera pamaso pa Ambuye wa dziko lonse.
And the Angell answered, and sayde vnto mee, These are the foure spirites of the heauen, which goe foorth from standing with the Lord of all the earth.
6 Galeta la akavalo akuda likupita ku dziko la kumpoto, galeta la akavalo oyera likutsatira, ndipo galeta la akavalo amawanga ofiirira likupita ku dziko la kummwera.”
That with the blacke horse went forth into the land of the North, and the white went out after them, and they of diuers colours went forth toward the South countrey.
7 Pamene akavalo amphamvuwa ankapita, anali ndi changu chofuna kuyendera dziko lapansi. Ndipo iye anati, “Pitani, kayendereni dziko lapansi!”
And the reddish went out, and required to go, and passe through the world, and he sayde, Goe passe through the worlde. So they went thorowout the world.
8 Pamenepo anandiyitana, “Taona, akavalo amene apita ku dziko la kumpoto apumulitsa Mzimu wanga kumeneko.”
Then cryed hee vpon me, and spake vnto me, saying, Beholde, these that goe towarde the North countrey, haue pacified my spirit in the North countrey.
9 Yehova anayankhula nane kuti,
And the worde of the Lord came vnto me, saying,
10 “Landira mphatso kuchokera kwa anthu amene abwera ku ukapolo, Helidai, Tobiya ndi Yedaya, amene achokera ku Babuloni. Tsiku lomwelo pita ku nyumba ya Yosiya mwana wa Zefaniya.
Take of them of ye captiuitie, euen of Heldai, and of Tobijah, and Iedaiah, which are come from Babel, and come thou the same day, and goe vnto the house of Ioshiah, the sonne of Zephaniah.
11 Tenga siliva ndi golide upange chipewa chaufumu, ndipo uchiyike pamutu pa mkulu wa ansembe, Yoswa mwana wa Yehozadaki.
Take euen siluer, and golde, and make crownes, and set them vpon the head of Iehoshua, the sonne of Iehozadak the hie Priest,
12 Muwuze kuti zimene akunena Yehova Wamphamvuzonse ndi izi: ‘Taonani, munthu wotchedwa Nthambi ndi ameneyu, ndipo adzaphuka pomwe alipo ndi kumanga Nyumba ya Yehova.
And speake vnto him, saying, Thus speaketh the Lord of hostes, and sayth, Behold the man whose name is the Branch, and he shall growe vp out of his place, and he shall build the Temple of the Lord.
13 Ndiye amene adzamange Nyumba ya Yehova, adzalandira ulemerero waufumu ndipo adzalamulira pa mpando wake waufumu. Adzakhalanso wansembe pa mpando wake waufumu. Ndipo padzakhala mtendere.’
Euen hee shall build the Temple of the Lord, and he shall beare the glory, and shall sit and rule vpon his throne, and he shalbe a Priest vpon his throne, and the counsell of peace shall be betweene them both.
14 Chipewa cha ufumucho adzachipereka kwa Helemu, Tobiya, Yedaya, ndi kwa Heni mwana wa Zefaniya, kuti chikhale chikumbutso mʼNyumba ya Yehova.
And the crownes shall be to Helem, and to Tobijah, and to Iedaiah, and to Hen the sonne of Zephaniah, for a memoriall in the Temple of the Lord.
15 Anthu okhala kutali adzabwera kudzathandiza kumanga Nyumba ya Yehova, ndipo iwe udzadziwa kuti Yehova Wamphamvuzonse wandituma kwa iwe. Zimenezi zidzachitika ngati mudzamvera mwachangu Yehova Mulungu wanu.”
And they that are farre off, shall come and build in the Temple of the Lord, and ye shall know, that the Lord of hostes hath sent me vnto you. And this shall come to passe, if ye will obey the voyce of the Lord your God.

< Zekariya 6 >