< Aroma 6 >
1 Nanga tinene chiyani? Kodi tipitirire kuchimwa kuti chisomo chichulukebe?
Su hatutakuli shishi? Hashi twendereyi kulikala muvidoda, su manemu ga Mlungu gongereki?
2 Ayi. Mʼnjira iliyonse! Popeza tinafa ku tchimo, nanga tidzapitirira bwanji kukhalabe mʼmenemo?
Ndala! Twenga tulikala gweka na vidoda, su hatwendereyi hashi kulikala kayi muvidoda?
3 Kodi simukudziwa kuti tonse amene tinabatizidwa mwa Khristu Yesu tinabatizidwa mu imfa yake?
Nakaka muvimana kuwera twenga patubatizitwi tuwera pamuhera na Kristu Yesu, watubatiziti na tuwera pamuhera na mukuhowa kwakuwi.
4 Chifukwa chake ife tinayikidwa mʼmanda pamodzi ndi Iye mwa ubatizo. Tinalowa mu imfa ndi cholinga choti monga momwe Khristu anaukitsidwa kwa akufa ndi ulemerero wa Atate, ifenso tikakhale mʼmoyo watsopano.
Su, patubatizitwi mumashi iweriti handa tusilwa pamuhera na Yesu, su Kristu ntambu yakazyukiti kwa makakala ga ukwisa wa Tati, kayi twenga tuwezi kulikala makaliru gasyayi.
5 Pakuti ngati ife tinakhala amodzi ndi Iye mu imfa yake, tidzakhalanso ndithu amodzi ndi Iye mu kuuka kwake.
Toziya handa twenga tuwera pamuhera nayomberi mukuhowa, viraa vilii twenga hatuweri yumu pamuhera na yomberi mukuzyukisiya.
6 Ife tikudziwa kuti umunthu wathu wakale unapachikidwa pamodzi ndi Iye kuti thupi la uchimo likhale lopanda mphamvu ndi kuti tisakakhalenso akapolo a tchimo
Twenga tuvimana kuwera makaliru getu ga makashu gapinjikitwi pamuhera na Kristu palupinjika lwakuwi, su makakala ga vidoda gaagamiziwi, natuwera kayi wamanda wa vidoda.
7 chifukwa aliyense amene anafa anamasuka ku tchimo.
Shipindi wantu tuhowiti pamuhera na Kristu, tulekiziwa kulawa mumakakala ga vidoda.
8 Koma ngati tinafa pamodzi ndi Khristu, tikhulupirira kuti tidzakhalanso ndi moyo pamodzi ndi Iye.
Kwanjira patuhowiti pamuhera na Kristu, twenga tujimira kuwera hatulikali kayi pamuhera na yomberi.
9 Pakuti tikudziwa kuti popeza Khristu anaukitsidwa kwa akufa, Iye sangafenso. Imfa ilibenso mphamvu pa Iye.
Twenga tuvimana handa Kristu kazyukisiwitwi kala na hapeni kahowi kayi. Kuhowa hapeni kumkoli kayi.
10 Imfa imene Iye anafa, anafa ku tchimo kamodzi kokha, koma moyo umene akhala ndi wa kwa Mulungu.
Su toziya kahowiti, vidoda vyahera makakala kwa yomberi, na vinu kalikala makaliru gakuwi mukulikolerana pamuhera na Mlungu.
11 Kotero inunso, mudzione nokha ngati akufa ku tchimo koma a moyo kwa Mulungu mwa Khristu Yesu.
Ntambu iraa ilii mwenga muliholi maweni kuwera mwagweka na vidoda, kumbiti mulikala mukulikolerana pamuhera na Mlungu kupitira Yesu Kristu.
12 Nʼchifukwa chake, musalole tchimo lilamulire matupi anu amene anafa kuti mumvere zilakolako zonyansa.
Vidoda naviwalonguziya kayi nshimba zyenu zyaziwola na mwenga kulijimira lumatamata lwakuwi.
13 Musapereke ziwalo zathupi lanu ku tchimo, ngati zipangizo zamakhalidwe oyipa. Mʼmalo mwake, mudzipereke kwa Mulungu, ngati amene achoka ku imfa kupita ku moyo. Ndipo mupereke ziwalo zathupi lanu ngati zipangizo zachilungamo.
Namlaviya ata pahala pamu pa nshimba zyenu ziweri shintu sha kutendera madoda na vidoda, kumbiti mulilaviyi maweni kwa Mlungu gambira wantu woseri yawazyukusiwitwi na mulaviyi umuntu wenu kwa Mlungu kwa kutenda matendu gagamfiriziya Mlungu.
14 Tchimo silidzakhalanso ndi mphamvu pa inu, chifukwa Malamulo sakulamulira moyo wanu koma chisomo.
Vidoda hapeni vikulongoziyi, toziya mwapasi ndiri pa malagaliru, kumbiti mwapasi pa manemu ga Mlungu.
15 Nʼchiyani tsono? Kodi tidzichimwa chifukwa sitikulamulidwa ndi Malamulo koma chisomo? Ayi. Mʼnjira iliyonse ayi!
Su tutakuli shishi? Hashi, tutendi vidoda toziya twapasi ndiri pa Malagaliru, kumbiti twapasi pa manemu ga Mlungu? Ndala!
16 Kodi inu simudziwa kuti pamene mudzipereka kwa wina wake, kumumvera ngati akapolo, ndinu akapolo a amene mumumvera? Ngati ndinu akapolo a tchimo mudzafa. Koma ngati ndinu akapolo akumvera, mudzakhala olungama pamaso pake.
Nakaka muvimana kuwera mwenga mwagambira wamanda. Handa mwenga pamujimira vidoda, malawiranu gakuwi hagaweri kuhowa. Handa pamumjimira Mlungu, malawiranu gakuwi ndo kuwera na matendu gagamfiriziya Mlungu.
17 Koma ayamikidwe Mulungu pakuti ngakhale munali akapolo a tchimo, munamvera ndi mtima wonse chiphunzitso chimene munalandira.
Kumbiti gulongi mayagashii Mlungu! Tembera muweriti wamanda wa vidoda pamakashu, mjimiriti kwa moyu gwoseri gwa nakaka galii mumafundu gamupatiti.
18 Inu munamasulidwa ku tchimo ndipo tsopano mwasanduka akapolo achilungamo.
Mwenga mlekeziwa kulawa muvidoda na muwera wamanda wa kutenda vyavimfiriziya Mlungu.
19 Ine ndikufanizira zinthu za tsiku ndi tsiku chifukwa chikhalidwe chanu nʼchofowoka. Monga momwe munkapereka ziwalo za matupi kukhala akapolo a zonyansa ndi makhalidwe oyipa, zimene zimanka zichulukirabe, choncho tsopano dziperekeni ziwalozo kuti zikhale akapolo achilungamo ndi a kuyera mtima.
Neni ntendera visoweru vya mashaka goseri toziya ya goyigoyi ya mwenga. Mushipindi shimu mwenga mulilaviyi maweni kuwera wamanda wa vidoda na kuwera wadoda kwa ukondola. Ntambu iraayi mwenga vinu kulilaviya maweni kutendera gambira wamanda kwa uheri kuwalonguziya mwenga muunanagala.
20 Pomwe munali akapolo atchimo, simunkalabadira za chilungamo.
Pamuweriti wamanda wa vidoda, muweriti kutali na kutenda uheri.
21 Kodi munapeza phindu lanji pochita zinthu zimenezi, zomwe tsopano mukuchita nazo manyazi? Zinthu zimenezo zotsatira zake ndi imfa!
Hashi, mpatiti mota gaa mashaka galii kulawirana na vitwatira ndovyeni vinu vyamuviwonera soni? Malawiranu ga vitwatira vyoseri ndo kuhowa!
22 Koma tsopano pakuti inu mwamasulidwa ku tchimo ndipo mwasanduka akapolo a Mulungu, phindu lomwe mulipeza ndi kuyera mtima ndipo chotsatira chake ndi moyo wosatha. (aiōnios )
Kumbiti vinu mwenga mlopoziwa kala kulawa muvidoda na kuwera wamanda wa Mlungu. Mota yamuwera nayu vinu ndo unanagala na malawiranu gakuwi ndo ukomu wa mashaka goseri. (aiōnios )
23 Pakuti malipiro a tchimo ndi imfa, koma mphatso yaulere imene Mulungu amapereka ndi moyo wosatha mwa Khristu Yesu Ambuye athu. (aiōnios )
Toziya shibenamgongu sha vidoda ndo kuhowa, kumbiti lifupu lya Mlungu ndo ukomu gwa mashaka goseri kulikolerana pamuhera na Kristu Yesu Mtuwa gwetu. (aiōnios )