< Masalimo 97 >

1 Yehova akulamulira, dziko lapansi lisangalale; magombe akutali akondwere.
The Lord reigneth: let the earth reioyce: let the multitude of the yles be glad.
2 Mitambo ndi mdima waukulu zamuzungulira; chilungamo ndi kuweruza molungama ndiwo maziko a mpando wake waufumu.
Cloudes and darkenes are round about him: righteousnesse and iudgement are the foundation of his throne.
3 Moto umapita patsogolo pake ndi kunyeketsa amaliwongo kumbali zonse.
There shall goe a fire before him, and burne vp his enemies round about.
4 Zingʼaningʼani zake zimawalitsa dziko lonse; dziko lapansi limaona ndipo limanjenjemera.
His lightnings gaue light vnto the worlde: the earth sawe it and was afraide.
5 Mapiri amasungunuka ngati phula pamaso pa Yehova, pamaso pa Ambuye a dziko lonse lapansi.
The mountaines melted like waxe at the presence of the Lord, at the presence of the Lord of the whole earth.
6 Mayiko akumwamba amalengeza za chilungamo chake, ndipo mitundu yonse ya anthu imaona ulemerero wake.
The heauens declare his righteousnes, and all the people see his glory.
7 Onse amene amalambira mafano osema amachititsidwa manyazi, iwo amene amanyadira mafano; mulambireni, inu milungu yonse!
Confounded be all they that serue grauen images, and that glory in idoles: worship him all ye gods.
8 Ziyoni akumva ndipo akukondwera, midzi ya Yuda ikusangalala chifukwa cha maweruzo anu Yehova.
Zion heard of it, and was glad: and the daughters of Iudah reioyced, because of thy iudgements, O Lord.
9 Pakuti Inu Yehova ndi Wammwambamwamba pa dziko lonse lapansi; ndinu wokwezeka kupambana milungu yonse.
For thou, Lord, art most High aboue all the earth: thou art much exalted aboue all gods.
10 Iwo amene amakonda Yehova adane ndi zoyipa pakuti Iye amayangʼanira miyoyo ya amene amamukhulupirira ndipo amawapulumutsa mʼdzanja la anthu oyipa
Ye that loue the Lord, hate euill: he preserueth the soules of his Saints: hee will deliuer them from the hand of the wicked.
11 Kuwala kumafika pa anthu olungama, ndi chimwemwe kwa olungama mtima.
Light is sowen for the righteous, and ioy for the vpright in heart.
12 Kondwerani mwa Yehova Inu olungama ndipo tamandani dzina lake loyera.
Reioyce ye righteous in the Lord, and giue thankes for his holy remembrance.

< Masalimo 97 >