< Masalimo 81 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a gititi. Salimo la Asafu. Imbani mwachimwemwe kwa Mulungu mphamvu yathu; Fuwulani mokweza kwa Mulungu wa Yakobo!
Kantaanyo iti napigsa ti Dios a pigsatayo; idir-iyo ti ragsakyo a maipaay iti Dios ni Jacob.
2 Yambani nyimbo, imbani tambolini imbani pangwe wolira bwino ndi zeze.
Agkantakayo ken tukarenyo ti pandereta, ti makaay-ayo ti unina a lira a mabuyogan iti arpa.
3 Imbani lipenga la nyanga ya nkhosa yayimuna pa mwezi watsopano, ndi pamene mwezi waoneka wonse, pa tsiku la phwando;
Puyotanyo ti tangguyob iti aldaw iti baro a bulan, iti aldaw ti kabus, inton mangrugi ti piestatayo.
4 ili ndi lamulo kwa Israeli, langizo la Mulungu wa Yakobo.
Ta daytoy ket linteg para iti Israel, maysa a bilin nga inted ti Dios ni Jacob.
5 Iye anapereka lamulolo kwa zidzukulu za Yosefe pamene anatuluka kulimbana ndi Igupto, kumene tinamva chiyankhulo chimene sitinachidziwe.
Impaulogna daytoy a kas pagalagadan kenni Jose idi binusorna ti daga ti Egipto, a nakangngegak iti pagsasao a saanko nga ammo.
6 Iye akunena kuti, “Ine ndinachotsa zolemetsa pa mapewa awo; Manja awo anamasulidwa mʼdengu.
“Inikkatko ti dadagsen iti abagana; nawaya-wayaan dagiti imana manipud iti panangig-iggemna iti basket.
7 Pa mavuto anu munayitana ndipo ndinakulanditsani, ndinakuyankhani kuchokera mʼmitambo ya mabingu; ndinakuyesani pa madzi a ku Meriba. (Sela)
Iti panagtutuokyo, immawagkayo, ket tinulongankayo; sinungbatankayo manipud iti nasipnget nga ulep ti gurruod. Sinuotkayo kadagiti danum idiay Meriba. (Selah)
8 “Imvani anthu anga, ndipo ndidzakuchenjezani ngati mungathe kumvetsera, Inu Israeli!
Dumngegkayo dakayo a tattaok, ta ballaagankayo, O Israel, no laeng koma ta dumngegkayo kaniak!
9 Musadzakhale ndi mulungu wachilendo pakati panu; musadzagwadire mulungu wina.
Masapul nga awan ti ganganaet a dios kadakayo; masapul a saanyo a dayawen ti aniaman a ganganaet a dios.
10 Ine ndine Yehova Mulungu wanu, amene ndinakutulutsani mʼdziko la Igupto. Yasamani kukamwa kwanu ndipo ndidzakudyetsani.
Siak ni Yahweh a Diosyo, a nangiruar kadakayo manipud iti daga ti Egipto. Ingangam ta ngiwatmo, ket punnoek dayta.
11 “Koma anthu anga sanandimvere; Israeli sanandigonjere.
Ngem saan a dimngeg dagiti tattaok kadagiti sasaok; saannak nga impangag ti Israel.
12 Kotero ndinawasiya ndi mitima yawo yosamverayo kuti atsate zimene ankafuna.
Isu nga inyawatko ida iti kinasukirda tapno maaramidda ti ipagarupda nga umno.
13 “Anthu anga akanangondimvera, Israeli akanatsatira njira zanga,
No koma ta dumngeg kaniak dagiti tattaok; no koma ta magna dagiti tattaok kadagiti dalanko.
14 nʼkanafulumira motani kuti ndigonjetse adani awo ndi kutembenuza mkono wanga kulimbana ndi amaliwongo!
Ket dagus a parmekek dagiti kabusorda ken ibaw-ingko ti imak maibusor kadagiti mangidaddadanes kadakuada.
15 Iwo amene amadana ndi Yehova akanakhwinyata pamaso pake, ndipo chilango chawo chinakakhala mpaka kalekale.
Agtigerger koma iti butengda dagiti manggurgura kenni Yahweh iti sangoananna! Maibabainda koma iti agnanayon.
16 Koma inu mukanadyetsedwa tirigu wabwino kwambiri; ndikanakukhutitsani ndi uchi wochokera pa thanthwe.”
Taraonakto ti Israel iti kasasayaatan a trigo; pennekenkayonto iti diro a naggapu kadagiti dadakkel a bato.”