< Masalimo 71 >
1 Mwa Inu Yehova ine ndathawiramo; musalole kuti ndichititsidwe manyazi.
In thee, O LORD, do I put my trust: let me never be ashamed.
2 Mundilanditse ndi kundipulumutsa mwa chilungamo chanu, mutchere khutu lanu ndi kundipulumutsa.
Deliver me in thy righteousness, and rescue me: bow down thine ear unto me, and save me.
3 Mukhale thanthwe langa lothawirapo, kumene ine nditha kupita nthawi zonse; lamulani kuti ndipulumuke, pakuti Inu ndinu thanthwe langa ndi linga langa.
Be thou to me a rock of habitation, whereunto I may continually resort: thou hast given commandment to save me; for thou art my rock and my fortress.
4 Landitseni Inu Mulungu wanga, kuchoka mʼdzanja la oyipa, kuchoka mʼdzanja la oyipa ndi anthu ankhanza.
Rescue me, O my God, out of the hand of the wicked, out of the hand of the unrighteous and cruel man.
5 Pakuti Inu mwakhala chiyembekezo changa, Inu Ambuye Wamphamvuzonse, chilimbikitso changa kuyambira ndili mwana.
For thou art my hope, O Lord GOD: [thou art] my trust from my youth.
6 Kuyambira pamene ndinabadwa, ndakhala ndikudalira Inu; Inu munanditulutsa mʼmimba mwa amayi anga, ndipo ndidzakupembedzani nthawi zonse.
By thee have I been holden up from the womb: thou art he that took me out of my mother’s bowels: my praise shall be continually of thee.
7 Ine ndakhala chinthu chodabwitsa kwa anthu ambiri koma Inu ndinu wonditchinjiriza wamphamvu.
I am as a wonder unto many; but thou art my strong refuge.
8 Pakamwa panga padzaza ndi matamando anu, kulengeza ulemerero wanu tsiku lonse.
My mouth shall be filled with thy praise, and with thy honour all the day.
9 Musanditaye pamene ndakalamba; musandisiye pamene mphamvu zanga zatha.
Cast me not off in the time of old age; forsake me not when my strength faileth.
10 Pakuti adani anga ayankhula motsutsana nane; iwo amene amadikira kuti andiphe amapangana pamodzi.
For mine enemies speak concerning me; and they that watch for my soul take counsel together,
11 Iwo amati, “Mulungu wamusiya; mutsatireni ndi kumugwira, pakuti palibe amene adzamupulumutse.”
Saying, God hath forsaken him: pursue and take him; for there is none to deliver.
12 Musakhale kutali ndi ine Inu Mulungu, bwerani msanga, Inu Mulungu wanga; thandizeni.
O God, be not far from me: O my God, make haste to help me.
13 Ondineneza anga awonongeke mwa manyazi, iwo amene akufuna kundipweteka avale chitonzo ndi manyazi.
Let them be ashamed [and] consumed that are adversaries to my soul; let them be covered with reproach and dishonour that seek my hurt.
14 Koma ine ndidzakhala ndi chiyembekezo mwa Inu nthawi zonse, ndidzakutamandani mowirikizawirikiza.
But I will hope continually, and will praise thee yet more and more.
15 Pakamwa panga padzafotokoza za chilungamo chanu, za chipulumutso chanu tsiku lonse, ngakhale sindikudziwa muyeso wake.
My mouth shall tell of thy righteousness, [and] of thy salvation all the day; for I know not the numbers [thereof].
16 Ndidzabwera ndi kulengeza za machitidwe amphamvu zanu Inu Ambuye Wamphamvuzonse. Ndidzalengeza chilungamo chanu, chanu chokha.
I will come with the mighty acts of the Lord GOD: I will make mention of thy righteousness, even of thine only.
17 Kuyambira ubwana wanga, Inu Mulungu mwakhala mukundiphunzitsa, ndipo mpaka lero ine ndikulengeza za ntchito zanu zodabwitsa
O God, thou hast taught me from my youth; and hitherto have I declared thy wondrous works.
18 Ngakhale pamene ndakalamba ndipo imvi zili mbuu musanditaye Inu Mulungu, mpaka nditalengeza mphamvu zanu kwa mibado yonse yakutsogolo.
Yea, even when I am old and grayheaded, O God, forsake me not; until I have declared thy strength unto [the next] generation, thy might to every one that is to come.
19 Mphamvu zanu ndi kulungama kwanu zimafika mpaka kumwambamwamba. Ndani wofanana nanu Inu Mulungu, amene mwachita zazikulu?
Thy righteousness also, O God, is very high; thou who hast done great things, O God, who is like unto thee?
20 Ngakhale mwandionetsa mavuto ambiri owawa, mudzabwezeretsanso moyo wanga; kuchokera kunsi kwa dziko lapansi, mudzandiukitsanso.
Thou, which hast shewed us many and sore troubles, shalt quicken us again, and shalt bring us up again from the depths of the earth.
21 Inu mudzachulukitsa ulemu wanga ndi kunditonthozanso.
Increase thou my greatness, and turn again and comfort me.
22 Ndidzakutamandani ndi zeze chifukwa cha kukhulupirika kwanu Mulungu, ndidzayimba matamando kwa Inu ndi pangwe, Inu Woyera wa Israeli.
I will also praise thee with the psaltery, [even] thy truth, O my God: unto thee will I sing praises with the harp, O thou Holy One of Israel.
23 Milomo yanga idzafuwula ndi chimwemwe pamene ndidzayimba matamando kwa Inu amene mwandiwombola.
My lips shall greatly rejoice when I sing praises unto thee; and my soul, which thou hast redeemed.
24 Lilime langa lidzafotokoza za ntchito zanu zachilungamo tsiku lonse, pakuti iwo amene amafuna kundipweteka achititsidwa manyazi ndi kusokonezedwa.
My tongue also shall talk of thy righteousness all the day long: for they are ashamed, for they are confounded, that seek my hurt.