< Masalimo 67 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Salimo. Yehova atikomere mtima ndi kutidalitsa, achititse kuti nkhope yake itiwalire.
To him that excelleth on Neginoth. A Psalme or song. God be mercifull vnto vs, and blesse vs, and cause his face to shine among vs. (Selah)
2 Kuti njira zanu zidziwike pa dziko lapansi, chipulumutso chanu pakati pa mitundu yonse.
That they may know thy way vpon earth, and thy sauing health among all nations.
3 Mitundu ya anthu ikutamandeni Inu Mulungu; mitundu yonse ya anthu ikutamandeni.
Let the people prayse thee, O God: let all the people prayse thee.
4 Mitundu yonse ya anthu isangalale ndi kuyimba mwachimwemwe, pakuti inu mumaweruza mitundu ya anthu mwachilungamo ndi kutsogolera mitundu ya anthu a dziko lapansi.
Let the people be glad and reioyce: for thou shalt iudge the people righteously, and gouerne the nations vpon the earth. (Selah)
5 Mitundu ya anthu ikutamandeni Inu Mulungu; mitundu yonse ya anthu ikutamandeni.
Let the people prayse thee, O God: let all the people prayse thee.
6 Nthaka yabereka zokolola zake; tidalitseni Mulungu wathu.
Then shall the earth bring foorth her increase, and God, euen our God shall blesse vs.
7 Mulungu atidalitse kuti pamenepo malekezero onse a dziko lapansi apembedze Iyeyo.
God shall blesse vs, and all the endes of the earth shall feare him.

< Masalimo 67 >