< Masalimo 62 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Kutsata mayimbidwe a Yedutuni. Salimo la Davide. Moyo wanga umapeza mpumulo mwa Mulungu yekha; chipulumutso changa chimachokera kwa Iye.
Для дириґента хору. Для Єдуту́на. Псалом Давидів. Тільки від Бога чекай у мовча́нні, о душе́ моя, від Нього спасі́ння моє!
2 Iye yekhayo ndiye thanthwe langa ndi chipulumutso changa; Iye ndi linga langa, choncho sindidzagwedezeka.
Тільки Він моя ске́ля й спасі́ння моє, Він тверди́ня моя, — тому́ не захита́юся дуже!
3 Kodi nonsenu mudzalimbana naye munthu mpaka liti? Kodi mudzamugwetsa pansi ngati khoma losalimba, ngati mpanda wogwedezeka?
Доки бу́дете ви напада́ти на люди́ну? Усі хочете ви розтрощи́ти її, немов мур той похи́лений, мов би парка́н той валю́щий!
4 Iwo akufunitsitsa kumugwetsa kuti achoke pa malo ake apamwamba. Iwo amakondweretsedwa ndi mabodza. Ndi pakamwa pawo amadalitsa koma mʼmitima yawo amatemberera.
Вони́ тільки й ду́мають, я́к би зіпхнути її з висоти, вони полюбили непра́вду: благословляють своїми уста́ми, в своєму ж нутрі́ проклинають! (Се́ла)
5 Peza mpumulo mwa Mulungu yekhayo iwe moyo wanga; chiyembekezo changa chichokera mwa Iye.
Тільки від Бога чекай у мовча́нні, о душе́ моя, бо від Нього надія моя!
6 Iye yekhayo ndiye thanthwe langa ndi chipulumutso changa; Iyeyo ndi linga langa; sindidzagwedezeka.
Тільки Він моя скеля й спасі́ння моє, Він тверди́ня моя, — тому́ не захитаюсь!
7 Chipulumutso changa ndi ulemu wanga zimachokera kwa Mulungu: Iye ndiye thanthwe langa lamphamvu; Mulungu ndiye pothawira panga.
У Бозі спасі́ння моє й моя слава, скеля сили моєї, моє пристано́вище в Бозі!
8 Dalirani Iye nthawi zonse, inu anthu; khuthulani mitima yanu kwa Iye, pakuti Mulungu ndiye pothawirapo pathu. (Sela)
Мій наро́де, — кожного ча́су наді́йтесь на Нього, серце своє перед Ним вилива́йте, Бог для нас — пристано́вище! (Се́ла)
9 Anthu wamba ndi mpweya chabe; anthu apamwamba ndi bodza chabe; ngati atayezedwa pa sikelo iwo ndi chabe; iwowo pamodzi ndi mpweya ndi chabe
Справді, лю́дські сини́ — як та па́ра, сини́ й вищих му́жів — обма́на: як узяти на вагу́ — вони легші від пари всі ра́зом!
10 Musadalire kulanda mwachinyengo kapena katundu wobedwa; ngakhale chuma chanu chichuluke, musayike mtima wanu pa icho.
Не наді́йтесь на у́тиск, і не пишайтесь грабу́нком; як багатство росте, — не приклада́йте свого серця до нього!
11 Mulungu wayankhula kamodzi, ine ndamvapo zinthu ziwiri; choyamba nʼchakuti Inu Mulungu ndinu wamphamvu,
Один раз Бог сказав, а двічі я чув, — що сила — у Бога!
12 komanso Inu Ambuye, chikondi chanu nʼchosasinthika. Chachiwiri nʼchakuti mumamuchitira munthu molingana ndi ntchito zake.
І в Тебе, о Господи, милість, бо відпла́чуєш кожному згідно з діла́ми його!