< Masalimo 51 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Pamene Mneneri Natani anabwera kwa iye atachita chigololo ndi Batiseba. Mundichitire chifundo, Inu Mulungu, molingana ndi chikondi chanu chosasinthika; molingana ndi chifundo chanu chachikulu mufafanize mphulupulu zanga.
Davidin Psalmi, edelläveisaajalle, Kuin propheta Natan tuli hänen tykönsä, sittekuin hän Batseban tykönä käynyt oli. Jumala, ole minulle armollinen sinun hyvyytes tähden: pyyhi pois minun syntini suuren laupiutes tähden.
2 Munditsuke zolakwa zanga zonse ndipo mundiyeretse kuchotsa tchimo langa.
Pese minua hyvin vääryydestäni, ja puhdista minua synnistäni.
3 Pakuti ndikudziwa mphulupulu zanga, ndipo tchimo langa lili pamaso panga nthawi zonse.
Sillä minä tunnen pahat tekoni, ja minun syntini on aina edessäni.
4 Motsutsana ndi Inu, Inu nokha, ndachimwa ndipo ndachita zoyipa pamaso panu, Kotero kuti inu mwapezeka kuti ndinu wolungama pamene muyankhula ndi pamene muweruza.
Sinua, sinua ainoaa vastaan minä syntiä tein, ja pahasti tein sinun edessäs, ettäs olisit oikia sanoissas ja puhdas tuomitessas.
5 Zoonadi ine ndinali wochimwa pomwe ndimabadwa, wochimwa kuyambira pa nthawi imene amayi anga anakhala woyembekezera ine.
Katso, minä olen synnissä syntynyt, ja minun äitini on synnissä minun siittänyt.
6 Zoonadi inu mumafuna choonadi mu ziwalo zamʼkati mwanga; mumandiphunzitsa nzeru mʼkati mwanga mwenimweni.
Katso, sinä halajat totuutta, joka salaudessa on, ja ilmoitat salatun viisauden minulle.
7 Mundiyeretse ndi hisope ndipo ndidzayera, munditsuke ndipo ndidzayera kuposa matalala
Puhdista minua isopilla, että minä puhdistuisin: pese minua, että minä lumivalkiaksi tulisin.
8 Mundilole ndimve chimwemwe ndi chisangalalo, mulole kuti mafupa amene mwawamphwanya akondwere.
Anna minun kuulla iloa ja riemua, että ne luut ihastuisivat, jotka särkenyt olet.
9 Mufulatire machimo anga ndi kufafaniza zolakwa zanga zonse.
Peitä kasvos minun synneistäni, ja pyyhi pois kaikki pahat tekoni.
10 Mulenge mʼkati mwanga mtima woyera Inu Mulungu ndi kukonzanso mzimu wokhazikika mwa ine.
Jumala, luo minuun puhdas sydän, ja anna minulle uusi vahva henki.
11 Musandichotse pamaso panu kapena kuchotsa Mzimu wanu Woyera mwa ine.
Älä heitä minua pois kasvois edestä, ja älä minulta ota pois sinun Pyhää Henkeäs.
12 Bwezeretsani mwa ine chimwemwe cha chipulumutso chanu ndipo mundipatse mzimu wofuna kumvera kuti undilimbitse.
Anna minulle taas sinun autuutes ilo, ja sillä hyvällä hengelläs tue minua.
13 Pamenepo ndidzaphunzitsa anthu amphulupulu njira zanu kuti ochimwa adzabwerere kwa inu.
Minä tahdon väärille opettaa sinun ties, että syntiset tykös palajaisivat.
14 Mundipulumutse ku tchimo lokhetsa magazi, Inu Mulungu, Mulungu wa chipulumutso changa, ndipo lilime langa lidzayimba zachilungamo chanu.
Päästä minua veren vioista, Jumala, minun autuuteni Jumala, että minun kieleni ylistäis sinun vanhurskauttas.
15 Inu Ambuye tsekulani milomo yanga, ndipo pakamwa panga padzalengeza matamando anu.
Avaa, Herra, minun huuleni, että minun suuni ilmoittais sinun kiitokses.
16 Inu simusangalatsidwa ndi nsembe wamba. Ndikanapereka nsembe yopsereza, Inu simukondwera nayo.
Sillä ei sinulle kelpaa uhri, että minä sen antaisin; ja ei polttouhri sinulle ensinkään kelpaa.
17 Nsembe za Mulungu ndi mzimu wosweka; mtima wosweka ndi wachisoni Inu Mulungu simudzawunyoza.
Ne uhrit, jotka Jumalalle kelpaavat, ovat murheellinen henki: ahdistettua ja särjettyä sydäntä et sinä, Jumala, hylkää.
18 Mwa kukoma mtima kwanu mupange Ziyoni kuti alemere; mumange makoma a Yerusalemu.
Tee Zionille hyvästi sinun armos jälkeen; rakenna Jerusalemin muurit.
19 Kotero kudzakhala nsembe zachilungamo, nsembe yonse yopsereza yokondweretsa Inu; ndipo ngʼombe zazimuna zidzaperekedwa pa guwa lanu la nsembe.
Silloin sinulle kelpaavat vanhurskauden uhrit, polttouhrit ja muut uhrit: silloin sinun alttarillas härkiä uhrataan.

< Masalimo 51 >