< Masalimo 51 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Pamene Mneneri Natani anabwera kwa iye atachita chigololo ndi Batiseba. Mundichitire chifundo, Inu Mulungu, molingana ndi chikondi chanu chosasinthika; molingana ndi chifundo chanu chachikulu mufafanize mphulupulu zanga.
For the music director. A psalm of David. When Nathan the prophet came to him after he had committed adultery with Bathsheba. God, please be gracious to me, because of your trustworthy love, because of your infinite kindness please wipe away my sins.
2 Munditsuke zolakwa zanga zonse ndipo mundiyeretse kuchotsa tchimo langa.
Wash away all my guilt; cleanse me from my sin.
3 Pakuti ndikudziwa mphulupulu zanga, ndipo tchimo langa lili pamaso panga nthawi zonse.
I admit my rebellion; my sin always stares me in my face.
4 Motsutsana ndi Inu, Inu nokha, ndachimwa ndipo ndachita zoyipa pamaso panu, Kotero kuti inu mwapezeka kuti ndinu wolungama pamene muyankhula ndi pamene muweruza.
I have sinned against you, you alone. I have done evil in your sight. So you are right in what you say, and fair when you judge.
5 Zoonadi ine ndinali wochimwa pomwe ndimabadwa, wochimwa kuyambira pa nthawi imene amayi anga anakhala woyembekezera ine.
It's true that I was born guilty—sinful from the time my mother conceived me.
6 Zoonadi inu mumafuna choonadi mu ziwalo zamʼkati mwanga; mumandiphunzitsa nzeru mʼkati mwanga mwenimweni.
But you want truth on the inside; you teach me wisdom deep within.
7 Mundiyeretse ndi hisope ndipo ndidzayera, munditsuke ndipo ndidzayera kuposa matalala
Purify me with hyssop so I can be clean; wash me so I can be whiter than snow.
8 Mundilole ndimve chimwemwe ndi chisangalalo, mulole kuti mafupa amene mwawamphwanya akondwere.
Please let me hear joy and happiness again; let the bones you have crushed be glad once more.
9 Mufulatire machimo anga ndi kufafaniza zolakwa zanga zonse.
Turn your face away from looking at my sins; please wipe away my guilt.
10 Mulenge mʼkati mwanga mtima woyera Inu Mulungu ndi kukonzanso mzimu wokhazikika mwa ine.
Create a pure mind in me, God, and make me trustworthy again.
11 Musandichotse pamaso panu kapena kuchotsa Mzimu wanu Woyera mwa ine.
Don't expel me from your presence; don't take away your Holy Spirit from me.
12 Bwezeretsani mwa ine chimwemwe cha chipulumutso chanu ndipo mundipatse mzimu wofuna kumvera kuti undilimbitse.
Give me back the happiness of your salvation; help me to have a willing nature.
13 Pamenepo ndidzaphunzitsa anthu amphulupulu njira zanu kuti ochimwa adzabwerere kwa inu.
Then I will teach your ways to rebellious people, and these sinners will come back to you.
14 Mundipulumutse ku tchimo lokhetsa magazi, Inu Mulungu, Mulungu wa chipulumutso changa, ndipo lilime langa lidzayimba zachilungamo chanu.
God, please forgive me for the blood I have shed, God of my salvation, and I will sing for joy of your goodness.
15 Inu Ambuye tsekulani milomo yanga, ndipo pakamwa panga padzalengeza matamando anu.
Open my lips so I can speak your praise!
16 Inu simusangalatsidwa ndi nsembe wamba. Ndikanapereka nsembe yopsereza, Inu simukondwera nayo.
For sacrifices don't make you happy, or I would bring one; burnt offerings aren't what pleases you.
17 Nsembe za Mulungu ndi mzimu wosweka; mtima wosweka ndi wachisoni Inu Mulungu simudzawunyoza.
The “sacrifices” that God wants are on the inside—the brokenness of repentance. God won't reject a broken and sorrowful heart.
18 Mwa kukoma mtima kwanu mupange Ziyoni kuti alemere; mumange makoma a Yerusalemu.
Be kind to Zion, help the city; rebuild the walls of Jerusalem.
19 Kotero kudzakhala nsembe zachilungamo, nsembe yonse yopsereza yokondweretsa Inu; ndipo ngʼombe zazimuna zidzaperekedwa pa guwa lanu la nsembe.
Then you will be pleased with sacrifices given in the right spirit, for all kinds of burnt offerings, and bulls sacrificed on your altar once more.

< Masalimo 51 >