< Masalimo 44 >
1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya ana a Kora. Ife tamva ndi makutu athu, Inu Mulungu; makolo athu atiwuza zimene munachita mʼmasiku awo, masiku akalekalewo.
To the chief music-maker. Of the sons of Korah Maschil. It has come to our ears, O God, our fathers have given us the story, of the works which you did in their days, in the old times,
2 Ndi dzanja lanu munathamangitsa mitundu ya anthu ena ndi kudzala makolo athu; Inu munakantha mitundu ya anthu, koma makolo athuwo Inu munawapatsa ufulu.
Uprooting the nations with your hand, and planting our fathers in their place; cutting down the nations, but increasing the growth of your people.
3 Sanalande dziko ndi lupanga lawo, si mkono wawo umene unawabweretsera chigonjetso, koma ndi dzanja lanu lamanja, mkono wanu ndi kuwala kwa nkhope yanu, pakuti munawakonda.
For they did not make the land theirs by their swords, and it was not their arms which kept them safe; but your right hand, and your arm, and the light of your face, because you had pleasure in them.
4 Inu ndinu Mfumu yanga ndi Mulungu wanga amene mumalamulira chigonjetso cha Yakobo.
You are my King and my God; ordering salvation for Jacob.
5 Kudzera kwa inu ife timabweza adani athu; kudzera mʼdzina lanu timapondereza otiwukirawo.
Through you will we overcome our haters; by your name will they be crushed under our feet who are violent against us.
6 Sindidalira uta wanga, lupanga langa silindibweretsera chigonjetso;
I will not put faith in my bow, my sword will not be my salvation.
7 koma Inu mumatigonjetsera adani athu, mumachititsa manyazi amene amadana nafe.
But it is you who have been our saviour from those who were against us, and have put to shame those who had hate for us.
8 Timanyadira mwa Mulungu wathu tsiku lonse, ndipo tidzatamanda dzina lanu kwamuyaya.
Our pride is in God at all times, to his name we give praise for ever. (Selah)
9 Koma tsopano mwatikana ndi kutichepetsa; Inu simupitanso ndi ankhondo athu.
But now you have sent us away from you, and put us to shame; you do not go out with our armies.
10 Munachititsa ife kubwerera mʼmbuyo pamaso pa mdani ndipo amene amadana nafe atilanda katundu.
Because of this we are turned back by the attacker: those who have hate for us take our goods for themselves.
11 Inu munatipereka kuti tiwonongedwe monga nkhosa ndipo mwatibalalitsa pakati pa anthu a mitundu ina.
You have made us like sheep which are taken for meat; we are put to flight among the nations.
12 Inu munagulitsa anthu anu pa mtengo wotsika, osapindulapo kanthu pa malondawo.
You let your people go for nothing; your wealth is not increased by their price.
13 Mwachititsa kuti tikhale chochititsa manyazi kwa anthu a mitundu ina, chonyozeka ndi chothetsa nzeru kwa iwo amene atizungulira.
You have made us to be looked down on by our neighbours, we are laughed at and shamed by those who are round about us.
14 Mwachititsa kuti tikhale onyozeka pakati pa anthu a mitundu ina; anthu amapukusa mitu yawo akationa.
Our name is a word of shame among the nations, a sign for the shaking of heads among the peoples.
15 Manyazi anga ali pamaso panga tsiku lonse ndipo nkhope yanga yaphimbidwa ndi manyazi
My downfall is ever before me, and I am covered with the shame of my face;
16 chifukwa cha mawu otonza a iwo amene amandinyoza ndi kundichita chipongwe, chifukwa cha mdani amene watsimikiza kubwezera.
Because of the voice of him who says sharp and bitter words; because of the hater and him who is the instrument of punishment.
17 Zonsezi zinatichitikira ngakhale kuti ifeyo sitinayiwale Inu kapena kuonetsa kusakhulupirika pa pangano lanu.
All this has come on us, but still we have kept you in our memory; and we have not been false to your word.
18 Mitima yathu sinabwerere mʼmbuyo; mapazi athu sanatayike pa njira yanu.
Our hearts have not gone back, and our steps have not been turned out of your way;
19 Koma Inu mwatiphwanya ndi kuchititsa kuti tikhale ozunzidwa ndi ankhandwe ndipo mwatiphimba ndi mdima waukulu.
Though you have let us be crushed in the place of jackals, though we are covered with darkest shade.
20 Tikanayiwala dzina la Mulungu wathu kapena kutambasulira manja athu kwa mulungu wachilendo,
If the name of our God has gone out of our minds, or if our hands have been stretched out to a strange god,
21 kodi Mulungu wathu sakanazidziwa zimenezi, pakuti Iye amadziwa zinsinsi zamumtima?
Will not God make search for it? for he sees the secrets of the heart.
22 Komabe chifukwa cha Inu timakumana ndi imfa tsiku lonse, tili ngati nkhosa zoyenera kuti ziphedwe.
Truly, because of you we are put to death every day; we are numbered like sheep for destruction.
23 Dzukani Ambuye! Nʼchifukwa chiyani mukugona! Dziwutseni nokha! Musatikane kwamuyaya.
Why are you sleeping, O Lord? awake! and come to our help, do not give us up for ever.
24 Nʼchifukwa chiyani mukubisa nkhope yanu, ndi kuyiwala mavuto athu ndi kuponderezedwa kwathu?
Why is your face covered, and why do you give no thought to our trouble and our cruel fate?
25 Tatsitsidwa pansi mpaka pa fumbi; matupi athu amatirira pa dothi.
For our souls are crushed down to the dust: our bodies are stretched out on the earth.
26 Imirirani ndi kutithandiza, tiwomboleni chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika.
Up! and come to our help, and give us salvation because of your mercy.