< Masalimo 4 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe wa zida za zingwe. Salimo la Davide. Ndiyankheni pamene ndiyitana Inu, Inu Mulungu wa chilungamo changa. Pumulitseni ku zowawa zanga; chitireni chifundo ndi kumva pemphero langa.
Для дириґе́нта хору. На струнних знаря́ддях. Псало́м Давидів. Коли кли́чу, — озвися до мене, Боже правди моєї, Ти про́стір для мене робив у тісноті́ … Помилуй мене, і почу́й молитву мою!
2 Anthu inu, mpaka liti mudzakhala mukusandutsa ulemerero wanga kukhala manyazi? Mpaka liti mudzakonda zachabe ndi kufuna milungu yabodza? (Sela)
Лю́дські сини, — доки слава моя буде га́ньбитись? Доки будете марне любити, шукати неправди? (Се́ла)
3 Dziwani kuti Yehova wadziyikira padera anthu okhulupirika; Yehova adzamva pamene ndidzamuyitana.
І знайте, що святого для Себе Господь відділив, почує Господь, як я кликати буду до Нього!
4 Kwiyani koma musachimwe; pamene muli pa mabedi anu, santhulani mitima yanu ndi kukhala chete. (Sela)
Гнівайтеся, та не грішіть; на ложах своїх розмишляйте у ваших серця́х, та й мовчіть! (Села)
5 Perekani nsembe zolungama ndipo dalirani Yehova.
Жертви правди прино́сьте, і наді́йтесь на Господа.
6 Ambiri akufunsa kuti, “Ndani angationetse chabwino chilichonse?” Kuwunika kwa nkhope yanu kutiwalire, Inu Yehova.
Багато-хто кажуть: „Хто нам покаже добро́?“Підійми ж на нас, Господи, світло Свого лиця!
7 Inu mwadzaza mtima wanga ndi chimwemwe chachikulu kuposa kuchuluka kwa tirigu wawo ndi vinyo watsopano.
Ти даєш більшу радість у серці моїм, ніж у них, як помно́жилося їхнє збіжжя та їхнє вино молоде.
8 Ine ndidzagona ndi kupeza tulo mwamtendere, pakuti Inu nokha, Inu Yehova, mumandisamalira bwino.
У споко́ї я ляжу, і засну́, бо Ти, Господи, єдиний даєш мені жити безпе́чно!

< Masalimo 4 >