< Masalimo 33 >

1 Imbirani Yehova mokondwera Inu olungama, nʼkoyenera kuti owongoka mtima azitamanda Iyeyo.
Agrag-okayo kenni Yahweh, dakayo a nalinteg; umno ti pammadayaw kadagiti nalinteg.
2 Mutamandeni Yehova ndi pangwe; muyimbireni Iye nyimbo pa zeze wa zingwe khumi.
Pagyamananyo ni Yahweh babaen iti arpa; agkantakayo kadagiti panagdaydayaw kenkuana babaen iti arpa a sangapulo ti kuerdasna.
3 Muyimbireni nyimbo yatsopano; imbani mwaluso, ndipo fuwulani mwachimwemwe.
Agkantakayo kenkuana iti baro a kanta; lalaingenyo ti agtukar ken agkantakayo nga addaan rag-o.
4 Pakuti mawu a Yehova ndi olungama ndi owona; Iye ndi wokhulupirika pa zonse zimene amachita.
Ta nalinteg ti sao ni Yahweh, ken maiparbeng dagiti amin nga ar-aramidenna.
5 Yehova amakonda chilungamo ndipo amaweruza molungama; dziko lapansi ladzaza ndi chikondi chake chosatha.
Pagay-ayatna ti kinalinteg ken hustisia. Napno ti daga iti kinapudno ti tulag ni Yahweh.
6 Ndi mawu a Yehova mayiko akumwamba anapangidwa, zolengedwa zake ndi mpweya wa mʼkamwa mwake.
Babaen iti sao ni Yahweh naaramid dagiti langlangit, ken naaramid dagiti bituen babaen iti sang-aw ti ngiwatna.
7 Iye amasonkhanitsa pamodzi madzi a mʼnyanja mʼmitsuko; amayika zozama mʼnyumba zosungiramo.
Sangsangkamaysaenna nga urnongen dagiti danum ti baybay a kasla maysa a gabsuon; ikabkabilna dagiti taaw kadagiti pagidulinan.
8 Dziko lonse lapansi liope Yehova; anthu onse amulemekeze Iye.
Agbuteng koma ti entero a daga kenni Yahweh; agtakder koma nga addaan panagbuteng kenkuana dagiti amin nga agnanaed iti lubong.
9 Pakuti Iye anayankhula ndipo zinakhalapo; Iye analamulira ndipo zinakhazikika.
Ta nagsao isuna, ket naaramid daytoy; imbilinna, ket timmakder daytoy iti lugarna.
10 Yehova amalepheretsa chikonzero cha anthu a mitundu ina; Iye amaphwanya zolinga za anthu ambiri.
Papaayen ni Yahweh dagiti panagkakadua dagiti nasion; artapanna dagiti panggep dagiti tattao.
11 Koma chikonzero cha Yehova chimakhala mpaka muyaya, zolinga za mu mtima mwake pa mibado yonse.
Agtakder iti agnanayon dagiti panggep ni Yahweh, dagiti panggep ti pusona para kadagiti amin a kaputotan.
12 Wodala mtundu wa anthu umene Mulungu wake ndi Yehova, anthu amene Iye anawasankha kukhala cholowa chake.
Nagasat ti nasion a ti Diosna ket ni Yahweh, dagiti tattao a pinilina a kas bukodna a tawid.
13 Kuchokera kumwamba Yehova amayangʼana pansi ndi kuona anthu onse;
Kumitkita ni Yahweh manipud langit; makitkitana dagiti amin a tattao.
14 kuchokera ku malo ake okhalako Iye amayangʼanira onse amene amakhala pa dziko lapansi.
Manipud iti lugar a pagnanaedanna, tantannawaganna dagiti amin nga agnanaed iti daga.
15 Iye amene amapanga mitima ya onse, amaona zonse zimene akuchita.
Isuna a mangbukbukel kadagiti puspusoda amin, palpaliiwenna dagiti amin nga aramidda.
16 Palibe mfumu imene imapulumutsidwa chifukwa cha kukula kwa gulu lake lankhondo; palibe msilikali amene amathawa ndi mphamvu zake zazikulu.
Awan ti ari a naisalakan ti nakaad-adu unay a suldado; saan a maisalakan ti maysa a mannakigubat babaen iti nabileg a pigsana.
17 Kavalo ndi chiyembekezo cha chabechabe cha chipulumutso, ngakhale ali ndi mphamvu yayikulu sangathe kupulumutsa.
Saan a pakanamnamaan iti balligi ti maysa kabalio; uray pay no nabileg ti pigsana, saan daytoy a makaispal.
18 Koma maso a Yehova ali pa iwo amene amaopa Iye; amene chiyembekezo chawo chili mʼchikondi chake chosatha,
Makitayo, ti mata ni Yahweh ket adda kadagiti agbuteng kenkuana, kadagiti agtaltalek iti kinapudno ti tulagna
19 kuwawombola iwo ku imfa ndi kuwasunga ndi moyo nthawi ya njala.
a mangilapsut kadagiti biagda manipud patay ken mangpatalinaed kadakuada a sibibiag iti tiempo ti panagbisin.
20 Ife timadikira kwa Yehova mwachiyembekezo; Iye ndiye thandizo lathu ndi chishango chathu.
Aguraytayo kenni Yahweh; isuna ti tulong ken kalasagtayo.
21 Mwa Iye mitima yathu imakondwera, pakuti ife timadalira dzina lake loyera.
Agrag-o dagiti pusotayo kenkuana, ta agtalektayo iti nasantoan a naganna.
22 Chikondi chanu chosatha chikhale pa ife Inu Yehova, pamene tikuyembekeza kwa Inu.
Ti kinapudno ti tulagmo O Yahweh, makikadua koma kadakami kas mangnamnamakami kenka.

< Masalimo 33 >