< Masalimo 27 >

1 Salimo la Davide. Yehova ndiye kuwunika kwanga ndi chipulumutso changa; ndidzaopa yani? Yehova ndi linga la moyo wanga; ndidzachita mantha ndi yani?
Давидів.
2 Pamene anthu oyipa abwera kudzalimbana nane kudzadya mnofu wanga, pamene adani anga ndi achiwembu andithira nkhondo, iwo adzapunthwa ndi kugwa.
Коли будуть зближа́тись до ме́не злочи́нці, щоб жерти їм тіло моє, мої напасники́ та мої вороги, — вони спотикну́ться й попа́дають!
3 Ngakhale gulu lankhondo lindizinge, mtima wanga sudzaopa. Ngakhale nkhondo itayambika kulimbana nane, ngakhale nthawi imeneyo, ine ndidzalimbika mtima.
коли проти мене розло́житься та́бір, то серце моє не злякається, коли проти мене повста́не війна, — я наді́ятись буду на те́, — на по́міч Його́!
4 Chinthu chimodzi chokha chimene ndipempha kwa Yehova, ichi ndi chimene ndidzachifunafuna: kuti ndikhale mʼNyumba ya Yehova masiku onse a moyo wanga, ndi kuyangʼana kukongola kwa Yehova, ndi kumufunafuna Iye mʼNyumba yake.
Одно́го прошу́ я від Господа, буду жадати того́, — щоб я міг пробува́ти в Господньому домі по всі дні свого життя, щоб я міг оглядати Господню приємність і в храмі Його пробува́ти!
5 Pakuti pa tsiku la msautso Iye adzanditeteza mʼmalo ake okhalamo; adzandibisa mʼkati mwa Nyumba yake ndi kukhazika ine pamwamba pa thanthwe.
бо Він заховає мене дня нещастя в Своїй ски́нії, сховає мене потає́мно в Своєму наме́ті, на скелю мене проведе́!
6 Kotero mutu wanga udzakwezedwa kuposa adani anga amene andizungulira; pa Nyumba yake ndidzapereka nsembe ndi mfuwu wachimwemwe; ndidzayimba nyimbo kwa Yehova.
А тепер піднесе́ться моя голова понад ворогами моїми навко́ло мене, і я в Його ски́нії буду прино́сити жертви при ві́дзвуках сурм, і я буду співати та грати Господе́ві!
7 Imvani mawu anga pamene ndiyitana Inu Yehova mundichitire chifundo ndipo mundiyankhe.
Почуй, Господи, голос мій, коли кли́чу, і помилуй мене, і озви́ся до мене!
8 Mtima wanga ukuti kwa Inu, “Funafuna nkhope yake!” Nkhope yanu Yehova ndidzayifunafuna.
За Тебе промовило серце моє: „Шукайте Мого лиця!“тому, Господи, буду шукати обличчя Твого́:
9 Musandibisire nkhope yanu, musamubweze mtumiki wanu mwamkwiyo; mwakhala muli thandizo langa. Musandikane kapena kunditaya, Inu Mulungu Mpulumutsi wanga.
не ховай же від мене обличчя Свого́, у гніві Свого раба не відкинь! Ти був мені по́міч, — не кидай мене, і не лишай мене, Боже спасі́ння мого,
10 Ngakhale abambo ndi amayi anga anditaya Yehova adzandisamala.
бо мій батько та мати моя мене кинули, — та Господь прийме́ мене!
11 Phunzitseni njira yanu Inu Yehova, munditsogolere mʼnjira yowongoka chifukwa cha ondizunza.
Дорогу Свою покажи мені, Господи, і провадь мене сте́жкою рівною, ради моїх ворогів!
12 Musandipereke ku zokhumba za adani anga, pakuti mboni zambiri zauka kutsutsana nane ndipo zikundiopseza.
Не видай мене на сваво́лю моїх ворогів, бо повстали на мене ті свідки облу́дні та неправдомо́вці,
13 Ine ndikutsimikiza mtima za zimenezi; ndidzaona ubwino wa Yehova mʼdziko la anthu amoyo.
немов би не вірував я, що в країні життя я побачу Господнє добро́!
14 Dikirani pa Yehova; khalani anyonga ndipo limbani mtima nimudikire Yehova.
Наді́йся на Господа, будь си́льний, і хай буде міцне́ твоє серце, і надійся на Господа!

< Masalimo 27 >