< Masalimo 24 >
1 Salimo la Davide. Dziko lapansi ndi la Yehova ndi zonse zimene zili mʼmenemo, dziko ndi onse amene amakhala mʼmenemo;
Псалом Давидів.
2 pakuti Iye ndiye anayika maziko ake pa nyanja ndi kulikhazika pamwamba pa madzi.
бо заклав Він її на моря́х, і на річках її встанови́в.
3 Ndani angakwere phiri la Yehova? Ndani angathe kuyima pa malo ake opatulika?
Хто зі́йде на го́ру Господню, і хто бу́де стояти на місці святому Його? —
4 Iye amene ali ndi mʼmanja moyera ndi mtima woyera, amene sapereka moyo wake kwa fano kapena kulumbira mwachinyengo.
У кого́ чисті руки та щиреє серце, і хто не нахиля́в на марно́ту своєї душі, і хто не присягав на обма́ну,
5 Iyeyo adzalandira madalitso kwa Yehova ndipo Mulungu mpulumutsi wake adzagamula kuti alibe mlandu.
нехай но́сить він благослове́ння від Господа, а праведність — від Бога спасі́ння свого!
6 Umenewo ndiwo mʼbado wa amene amafunafuna Yehova; amene amafunafuna nkhope yanu, Inu Mulungu wa Yakobo. (Sela)
Таке поколі́ння усіх, хто шукає Його́, хто пра́гне обличчя Твого́, Боже Яковів! (Се́ла)
7 Tukulani mitu yanu inu zipata; tsekukani, inu zitseko zakalekalenu, kuti Mfumu yaulemerero ilowe.
Піднесі́те верхи́ свої, брами, і будьте відчи́нені, вхо́ди відві́чні, — і вві́йде Цар слави!
8 Kodi Mfumu yaulemereroyo ndani? Yehova Wamphamvuzonse, Yehova ndiye wamphamvu pa nkhondo.
Хто ж то Цар слави? — Господь си́льний й могу́тній, Господь, що поту́жний в бою́!
9 Tukulani mitu yanu, inu zipata; tsekukani, inu zitseko zakalekalenu, kuti Mfumu yaulemerero ilowe.
Піднесіте верхи́ свої, брами, і піднесіте, вхо́ди відві́чні, — і вві́йде Цар слави!
10 Kodi Mfumu yaulemereroyo ndani? Yehova Wamphamvuzonse, Iye ndiye Mfumu yaulemerero. (Sela)
Хто ж то Він, той Цар слави? Господь Савао́т — Він Цар слави! (Се́ла)