< Masalimo 143 >
1 Salimo la Davide. Yehova imvani pemphero langa, mvetserani kulira kwanga kopempha chifundo; mwa kukhulupirika kwanu ndi chilungamo chanu bwerani kudzandithandiza.
A Psalme of David. Heare my prayer, O Lord, and hearken vnto my supplication: answer me in thy trueth and in thy righteousnes.
2 Musazenge mlandu mtumiki wanu, pakuti palibe munthu wamoyo amene ndi wolungama pamaso panu.
(And enter not into iudgement with thy seruant: for in thy sight shall none that liueth, be iustified)
3 Mdani akundithamangitsa, iye wandipondereza pansi; wachititsa kuti ndikhale mu mdima ngati munthu amene anafa kale.
For the enemie hath persecuted my soule: he hath smitten my life downe to the earth: he hath layde me in the darkenes, as they that haue bene dead long agoe:
4 Choncho mzimu wanga ukufowoka mʼkati mwanga; mʼkati mwanga, mtima wanga uli ndi nkhawa.
And my spirit was in perplexitie in me, and mine heart within me was amased.
5 Ndimakumbukira masiku amakedzana; ndimalingalira za ntchito yanu yonse, ndimaganizira zimene manja anu anachita.
Yet do I remember the time past: I meditate in all thy workes, yea, I doe meditate in the workes of thine hands.
6 Ndatambalitsa manja anga kwa Inu; moyo wanga uli ndi ludzu lofuna Inu monga nthaka yowuma. (Sela)
I stretche forth mine hands vnto thee: my soule desireth after thee, as the thirstie land. (Selah)
7 Yehova ndiyankheni msanga; mzimu wanga ukufowoka. Musandibisire nkhope yanu, mwina ndidzakhala ngati iwo amene atsikira ku dzenje.
Heare me spedely, O Lord, for my spirit faeleth: hide not thy face from me, els I shall be like vnto them that go downe into the pit.
8 Lolani kuti mmawa ubweretse mawu achikondi chanu chosasinthika, pakuti ine ndimadalira Inu. Mundisonyeze njira yoti ndiyendemo, pakuti kwa Inu nditukulira moyo wanga.
Let me heare thy louing kindenes in the morning, for in thee is my trust: shewe mee the waie, that I should walke in, for I lift vp my soule vnto thee.
9 Pulumutseni kwa adani anga, Inu Yehova, pakuti ndimabisala mwa Inu.
Deliuer me, O Lord, from mine enemies: for I hid me with thee.
10 Phunzitseni kuchita chifuniro chanu, popeza ndinu Mulungu wanga; Mzimu wanu wabwino unditsogolere pa njira yanu yosalala.
Teach me to do thy will, for thou art my God: let thy good Spirit leade me vnto the land of righteousnes.
11 Sungani moyo wanga Inu Yehova chifukwa cha dzina lanu; mwa chilungamo chanu tulutseni mʼmasautso anga.
Quicken me, O Lord, for thy Names sake, and for thy righteousnes bring my soule out of trouble.
12 Mwa chikondi chanu chosasinthika khalitsani chete adani anga; wonongani adani anga, pakuti ndine mtumiki wanu.
And for thy mercy slay mine enemies, and destrie all them that oppresse my soule: for I am thy seruant.