< Masalimo 121 >
1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Ndikweza maso anga ku mapiri; kodi thandizo langa limachokera kuti?
Ein Lied für Wallfahrten. Ich hebe meine Augen auf zu den Bergen:
2 Thandizo langa limachokera kwa Yehova, wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.
Meine Hilfe kommt vom HERRN, der Himmel und Erde geschaffen.
3 Sadzalola kuti phazi lako literereke; Iye amene amakusunga sadzawodzera.
Er wird deinen Fuß nicht wanken lassen; nicht schlummert dein Hüter.
4 Taonani, Iye amene amasunga Israeli sadzawodzera kapena kugona.
Nein, nicht schlummert und nicht schläft der Hüter Israels.
5 Yehova ndiye amene amakusunga; Yehova ndiye mthunzi wako ku dzanja lako lamanja.
Der HERR ist dein Hüter, der HERR dein Schatten über deiner rechten Hand,
6 Dzuwa silidzakupweteka nthawi ya masana, kapena mwezi nthawi ya usiku.
daß dich bei Tage die Sonne nicht sticht, noch der Mond in der Nacht.
7 Yehova adzakuteteza ku zoyipa zonse; adzasunga moyo wako.
Der HERR behütet dich vor allem Übel, er behütet deine Seele;
8 Yehova adzayangʼanira kutuluka kwako ndi kulowa kwako; kuyambira tsopano mpaka muyaya.
der HERR behütet deinen Ausgang und Eingang von nun an bis in Ewigkeit.