< Masalimo 121 >
1 Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Ndikweza maso anga ku mapiri; kodi thandizo langa limachokera kuti?
A Song of Ascents. I will lift up mine eyes unto the mountains: from whence shall my help come?
2 Thandizo langa limachokera kwa Yehova, wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.
My help [cometh] from the LORD, which made heaven and earth.
3 Sadzalola kuti phazi lako literereke; Iye amene amakusunga sadzawodzera.
He will not suffer thy foot to be moved: he that keepeth thee will not slumber.
4 Taonani, Iye amene amasunga Israeli sadzawodzera kapena kugona.
Behold, he that keepeth Israel shall neither slumber nor sleep.
5 Yehova ndiye amene amakusunga; Yehova ndiye mthunzi wako ku dzanja lako lamanja.
The LORD is thy keeper: the LORD is thy shade upon thy right hand.
6 Dzuwa silidzakupweteka nthawi ya masana, kapena mwezi nthawi ya usiku.
The sun shall not smite thee by day, nor the moon by night.
7 Yehova adzakuteteza ku zoyipa zonse; adzasunga moyo wako.
The LORD shall keep thee from all evil; he shall keep thy soul.
8 Yehova adzayangʼanira kutuluka kwako ndi kulowa kwako; kuyambira tsopano mpaka muyaya.
The LORD shall keep thy going out and thy coming in, from this time forth and for evermore.