< Masalimo 12 >

1 Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Monga mwa mayimbidwe seminiti. Salimo la Davide. Thandizeni Yehova pakuti palibe munthu wokhulupirika; okhulupirika akusowa pakati pa anthu.
برای سالار مغنیان برثمانی. مزمور داود ای خداوند نجات بده زیرا که مردمقدس نابود شده است و امناء از میان بنی آدم نایاب گردیده‌اند!۱
2 Aliyense amanamiza mʼbale wake; ndi pakamwa pawo pabodza amayankhula zachinyengo.
همه به یکدیگر دروغ می‌گویند؛ به لبهای چاپلوس و دل منافق سخن می‌رانند.۲
3 Inu Yehova tsekani milomo yonse yachinyengo ndi pakamwa paliponse podzikuza.
خداوند همه لبهای چاپلوس رامنقطع خواهد ساخت، و هر زبانی را که سخنان تکبرآمیز بگوید.۳
4 Pakamwa pamene pamati, “Ife tidzapambana ndi kuyankhula kwathu; pakamwapa ndi pathupathu, tsono mbuye wathu ndani?”
که می‌گویند: «به زبان خویش غالب می‌آییم. لبهای ما با ما است. کیست که بر ماخداوند باشد؟»۴
5 “Chifukwa cha kuponderezedwa kwa anthu opanda mphamvu ndi kubuwula kwa anthu osowa, Ine ndidzauka tsopano,” akutero Yehova, “Ndidzawateteza kwa owazunza.”
خداوند می‌گوید: «به‌سبب غارت مسکینان و ناله فقیران، الان برمی خیزم و او را در نجاتی که برای آن آه می‌کشد برپا خواهم داشت».۵
6 Ndipo mawu a Yehova ndi angwiro monga siliva oyengedwa mʼngʼanjo yadothi, oyengedwa kasanu nʼkawiri.
کلام خداوند کلام طاهر است، نقره مصفای در قال زمین که هفت مرتبه پاک شده است.۶
7 Inu Yehova mudzatitchinjiriza ndipo mudzatiteteza kwa anthu otere kwamuyaya.
تو‌ای خداوند ایشان را محافظت خواهی نمود؛ از این طبقه و تا ابدالاباد محافظت خواهی فرمود.۷
8 Oyipa amangoyendayenda ponseponse anthu akamayamikira zochita zawo.
شریران به هر جانب می‌خرامند، وقتی که خباثت در بنی آدم بلند می‌شود.۸

< Masalimo 12 >