< Masalimo 103 >
1 Salimo la Davide. Tamanda Yehova, iwe moyo wanga; ndi zonse zamʼkati mwanga zitamande dzina lake loyera.
Un salmo de David. Alaba, alma mía, al Señor; que todo mi ser alabe su santo nombre.
2 Tamanda Yehova, iwe moyo wanga, ndipo usayiwale zabwino zake zonse.
Alaba, alma mía, al Señor; y que no olvide mi ser las maravillosas cosas que él ha hecho por mí.
3 Amene amakhululuka machimo ako onse ndi kuchiritsa nthenda zako zonse,
Él perdona mis pecados, y cura todas mis enfermedades.
4 amene awombola moyo wako ku dzenje ndi kukuveka chikondi ndi chifundo chake ngati chipewa chaufumu,
Me salva de la muerte; me honra con su gran amor y misericordia.
5 amene akwaniritsa zokhumba zako ndi zinthu zabwino, kotero kuti umakhala wamphamvu zatsopano ngati mphungu.
Llena mi vida con todo lo que es bueno; me rejuvenece, y me hace fuerte como un águila.
6 Yehova amachita chilungamo ndipo amaweruza molungama onse opsinjika.
El Señor hace lo que está bien, y defiende a los que son abusados.
7 Iye anadziwitsa Mose njira zake, ntchito zake kwa Aisraeli.
Él explicó sus caminos a moisés: le dijo al pueblo de Israel lo que iba a hacer.
8 Yehova ndi wachifundo ndi wokoma mtima, wosakwiya msanga ndi wachikondi chochuluka.
El Señor es amable y lleno de gracia, y no rápido para la ira. Lleno de amor y justicia.
9 Iye sadzatsutsa nthawi zonse, kapena kusunga mkwiyo wake kwamuyaya;
Él no nos acusa; ni permanece para siempre airado con nosotros.
10 satichitira molingana ndi machimo athu, kapena kutibwezera molingana ndi mphulupulu zathu.
No nos castiga por nuestros pecados, como debería hacer; no nos devuelve todas las cosas malas que hacemos, aunque lo merezcamos.
11 Pakuti monga kumwamba kuli kutali ndi dziko lapansi, koteronso chikondi chake nʼchachikulu kwa iwo amene amamuopa;
Porque tan grande como los cielos que están sobre la tierra es su amor con los que le honran.
12 monga kummawa kutalikirana ndi kumadzulo, koteronso Iye watichotsera mphulupulu zathu kuti zikhale kutali nafe.
Tan lejos como el este está del oeste es como el Señor ha echado fuera nuestros pecados.
13 Monga bambo amachitira chifundo ana ake, choncho Yehova ali ndi chifundo ndi iwo amene amamuopa;
Como un padre amoroso, el Señor es amable y compasivo con quienes le siguen.
14 pakuti Iye amadziwa momwe tinawumbidwira, amakumbukira kuti ndife fumbi.
Porque él sabe cómo fuimos hechos; él recuerda que somos solo polvo.
15 Kunena za munthu, masiku ake ali ngati udzu, amaphuka ngati duwa la mʼmunda;
La vida de los seres humanos es como la grama: florecemos como plantas en un campo,
16 koma mphepo imawombapo ndipo silionekanso ndipo malo ake sakumbukirikanso.
pero entonces el viento sopla, y nos vamos, desapareciendo sin dejar rastro.
17 Koma kuchokera muyaya mpaka muyaya chikondi cha Yehova chili ndi iwo amene amamuopa, ndi chilungamo chake chili ndi ana a ana awo;
Pero el gran amor de Dios durará para toda la eternidad con aquellos que le siguen; su bondad perdurará por todas las generaciones,
18 iwo amene amasunga pangano lake ndi kukumbukira kumvera malangizo ake.
con aquellos que cumplen sus convenios y sus mandamientos.
19 Yehova wakhazikitsa mpando wake waufumu mmwamba ndipo ufumu wake umalamulira onse.
El Señor ha establecido su trono en los cielos, y gobierna sobre todas las cosas.
20 Tamandani Yehova, inu angelo ake, amphamvu inu amene mumachita zimene amalamula, amene mumamvera mawu ake.
¡Alaben al Señor, ángeles, ustedes poderosos que hacen lo que él dice, escuchando lo que él les ordena!
21 Tamandani Yehova, zolengedwa zonse zakumwamba, inu atumiki ake amene mumachita chifuniro chake.
¡Alaben al Señor, ustedes ejércitos celestiales que le sirven y cumplen su voluntad!
22 Tamandani Yehova, ntchito yake yonse kulikonse mu ulamuliro wake. Tamanda Yehova, iwe moyo wanga.
¡Alabe al Señor, toda cosa en su creación, todos bajo su gobierno! ¡Alaba, alma mía, al Señor!