< Masalimo 103 >

1 Salimo la Davide. Tamanda Yehova, iwe moyo wanga; ndi zonse zamʼkati mwanga zitamande dzina lake loyera.
“Of David.” Bless, O my soul, the Lord, and all that is within me, his holy name.
2 Tamanda Yehova, iwe moyo wanga, ndipo usayiwale zabwino zake zonse.
Bless, O my soul, the Lord, and forget not all his benefits:
3 Amene amakhululuka machimo ako onse ndi kuchiritsa nthenda zako zonse,
Who forgiveth all thy iniquities; who healeth all thy diseases;
4 amene awombola moyo wako ku dzenje ndi kukuveka chikondi ndi chifundo chake ngati chipewa chaufumu,
Who redeemeth from the pit thy life; who crowneth thee with kindness and mercies;
5 amene akwaniritsa zokhumba zako ndi zinthu zabwino, kotero kuti umakhala wamphamvu zatsopano ngati mphungu.
Who satisfieth with happiness thy spirit, so that thy youth is renewed like the eagle's [plumage].
6 Yehova amachita chilungamo ndipo amaweruza molungama onse opsinjika.
The Lord executeth righteousness, and justice for all that are oppressed.
7 Iye anadziwitsa Mose njira zake, ntchito zake kwa Aisraeli.
He made known his ways unto Moses, unto the children of Israel his acts.
8 Yehova ndi wachifundo ndi wokoma mtima, wosakwiya msanga ndi wachikondi chochuluka.
Merciful and gracious is the Lord, long-suffering and abundant in kindness.
9 Iye sadzatsutsa nthawi zonse, kapena kusunga mkwiyo wake kwamuyaya;
Not for all eternity will he contend; nor will he for ever retain his anger.
10 satichitira molingana ndi machimo athu, kapena kutibwezera molingana ndi mphulupulu zathu.
Not in accordance with our sins hath he dealt with us; nor according to our iniquities hath he requited us.
11 Pakuti monga kumwamba kuli kutali ndi dziko lapansi, koteronso chikondi chake nʼchachikulu kwa iwo amene amamuopa;
For as high as heaven is above the earth, so mighty is his kindness toward those that fear him.
12 monga kummawa kutalikirana ndi kumadzulo, koteronso Iye watichotsera mphulupulu zathu kuti zikhale kutali nafe.
As far as the east is from the west, so far hath he removed from us our transgressions.
13 Monga bambo amachitira chifundo ana ake, choncho Yehova ali ndi chifundo ndi iwo amene amamuopa;
As a father hath mercy on his children, so hath the Lord mercy on those that fear him.
14 pakuti Iye amadziwa momwe tinawumbidwira, amakumbukira kuti ndife fumbi.
For he knoweth our frame; he remembereth that we are dust.
15 Kunena za munthu, masiku ake ali ngati udzu, amaphuka ngati duwa la mʼmunda;
As for man, like the grass are his days: as the blossom of the field, so doth he bloom.
16 koma mphepo imawombapo ndipo silionekanso ndipo malo ake sakumbukirikanso.
When a wind but passeth over it, it is gone, and its place will recognize it no more.
17 Koma kuchokera muyaya mpaka muyaya chikondi cha Yehova chili ndi iwo amene amamuopa, ndi chilungamo chake chili ndi ana a ana awo;
But the kindness of the Lord is from everlasting to everlasting over those that fear him, and his righteousness unto children's children,
18 iwo amene amasunga pangano lake ndi kukumbukira kumvera malangizo ake.
To such as keep his covenant, and to those who remember his precepts to execute them.
19 Yehova wakhazikitsa mpando wake waufumu mmwamba ndipo ufumu wake umalamulira onse.
The Lord hath established in the heavens his throne; and his kingdom ruleth over all.
20 Tamandani Yehova, inu angelo ake, amphamvu inu amene mumachita zimene amalamula, amene mumamvera mawu ake.
Bless the Lord, ye his angels, mighty in strength, that execute his word, hearkening unto the voice of his word.
21 Tamandani Yehova, zolengedwa zonse zakumwamba, inu atumiki ake amene mumachita chifuniro chake.
Bless ye the Lord, all his hosts, ye his ministers, that execute his will.
22 Tamandani Yehova, ntchito yake yonse kulikonse mu ulamuliro wake. Tamanda Yehova, iwe moyo wanga.
Bless the Lord, all his works, in all the places of his dominion; bless, O my soul, the Lord.

< Masalimo 103 >