< Miyambo 22 >
1 Mbiri yabwino ndi yofunika kuposa chuma chambiri; kupeza kuyanja nʼkwabwino kuposa siliva kapena golide.
Ліпше добре ім'я́ за багатство велике, і ліпша милість за срі́бло та золото.
2 Wolemera ndi wosauka ndi ofanana; onsewa anawalenga ndi Yehova.
Багатий та вбогий стрічаються, — Господь їх обох створив.
3 Munthu wochenjera akaona choopsa amabisala, koma munthu wopusa amangopitirira ndipo amadzanongʼoneza bondo.
Мудрий бачить лихе — і ховається, а безумні йдуть і кара́ються.
4 Mphotho ya munthu wodzichepetsa ndi woopa Yehova ndi chuma, ulemu ndi moyo.
Заплата покори і стра́ху Господнього, — це багатство, і слава, й життя.
5 Mʼnjira za anthu oyipa muli minga ndi misampha, koma amene amasala moyo wake adzazipewa zonsezo.
Терни́на й пастки́ на дорозі лукавого, а хто стереже́ свою душу, віді́йде далеко від них.
6 Mwana muzimuphunzitsa njira yake, ndipo akadzakalamba sadzachokamo.
Привчай юнака́ до дороги його, і він, як поста́ріється, не усту́питься з неї.
7 Wolemera amalamulira wosauka, ndipo wokongola zinthu amakhala kapolo wa womukongozayo.
Багатий панує над бідними, а боржни́к — раб позича́льника.
8 Amene amafesa zoyipa amakolola mavuto, ndipo ndodo yaukali wake idzathyoka.
Хто сіє кри́вду, той жа́тиме лихо, а бич гніву його покінчи́ться.
9 Amene ali ndi diso lachifundo adzadalitsika, pakuti iye amagawana chakudya chake ndi anthu osauka.
Хто доброго ока, той поблагосло́влений буде, бо дає він убогому з хліба свого́.
10 Chotsani munthu wonyoza, ndipo kukangana kudzatha; mapokoso ndi zonyoza zidzaleka.
Глумли́вого вижени, — й вийде з ним сварка, і суперечка та га́ньба припи́няться.
11 Amene amakonda kukhala woyera mtima ndi kumayankhula mawu abwino, adzakhala bwenzi la mfumu.
Хто чистість серця кохає, той має хороше на устах, і другом йому буде цар.
12 Maso a Yehova amakhala pa anthu odziwa bwino zinthu, koma Iye adzalepheretsa mawu a anthu osakhulupirika.
Очі Господа оберігають знання́, а лукаві слова́ Він відкине.
13 Munthu waulesi amati, “Kunjaku kuli mkango. Ine ndidzaphedwa mʼmisewu!”
Лінивий говорить: „На вулиці лев, — серед майда́ну я буду забитий!“
14 Pakamwa pa mkazi wachigololo pali ngati dzenje lozama; amene Yehova wamukwiyira adzagwamo.
Уста коха́нки — яма глибока: на ко́го Господь має гнів, той впадає туди.
15 Uchitsiru umakhala mu mtima mwa mwana, koma ndodo yomulangira mwanayo idzachotsa uchitsiruwo.
До юнако́вого серця глупо́та прив'язана, та різка карта́ння відда́лить від нього її.
16 Amene amapondereza anthu osauka kuti awonjezere chuma chake, ndiponso amene amapereka mphatso kwa anthu olemera onsewa adzasauka.
Хто тисне убогого, щоб собі́ збагати́тись, і хто багаче́ві дає, — той певно збідніє.
17 Utchere khutu lako ndipo umvere mawu anzeru; uyike mtima wako pa zimene ndikukuphunzitsa kuti udziwe.
Нахили своє вухо, і послухай слів мудрих, і серце зверни до мого знання́,
18 Zidzakhala zokondweretsa ngati uzisunga mu mtima mwako ndi wokonzeka kuziyankhula.
бо гарне воно, коли будеш ти їх у своєму нутрі́ стерегти́, — хай стануть на устах твоїх вони ра́зом!
19 Ndakuphunzitsa zimenezi lero koma makamaka uziopa Yehova.
Щоб надія твоя була в Го́споді, я й сьогодні навчаю тебе.
20 Kodi suja ndinakulembera malangizo makumi atatu okuchenjeza ndi okupatsa nzeru,
Хіба ж не писав тобі три́чі з порадами та із знання́м,
21 malangizo okudziwitsa zolungama ndi zoona ndi kuti ukawayankhe zoona amene akutumawo?
щоб тобі завідо́мити правду, правдиві слова́, щоб ти істину міг відпові́сти тому, хто тебе запитає.
22 Mʼmphawi usamubere chifukwa ndi osauka, ndipo usawapondereze anthu osowa mʼbwalo la milandu,
Не грабу́й незамо́жнього, бо він незамо́жній, і не тисни убогого в брамі,
23 pakuti Yehova adzawateteza pa mlandu wawo ndipo adzalanda moyo onse amene amawalanda iwo.
бо Господь за їхню справу суди́тиметься, і грабіжникам їхнім ограбує Він душу.
24 Usapalane naye ubwenzi munthu wosachedwa kupsa mtima ndipo usayanjane ndi munthu amene sachedwa kukwiya
Не дружись із чоловіком гнівли́вим, і не ходи із люди́ною лютою,
25 kuopa kuti iwe ungadzaphunzire njira zake ndi kukodwa mu msampha.
щоб доріг її ти не навчи́вся, і тене́та не взяв для своєї душі.
26 Usakhale munthu wopereka chikole kapena kukhala mboni pa ngongole;
Не будь серед тих, хто пору́ку дає́, серед тих, хто пору́чується за борги́:
27 ngati ulephera kupeza njira yolipirira adzakulanda ngakhale bedi lako lomwe.
коли ти не матимеш чим заплатити, — нащо ві́зьмуть з-під тебе посте́лю твою?
28 Usasunthe mwala wamʼmalire akalekale amene anayikidwa ndi makolo ako.
Не пересува́й віково́ї границі, яку встановили батьки́ твої.
29 Kodi ukumuona munthu waluso pa ntchito yake? Iye adzatumikira mafumu; sadzatumikira anthu wamba.
Ти бачив люди́ну, мото́рну в занятті своїм? Вона перед царя́ми спокійно стоятиме, та не всто́їть вона перед про́стими.