< Miyambo 2 >

1 Mwana wanga, ngati ulandira mawu anga ndi kusunga malamulo anga mu mtima mwako,
Mein Sohn! Nimmst du jetzt meine Worte an und bewahrst du bei dir, was ich geboten,
2 ndiponso kutchera khutu lako ku nzeru ndi kuyikapo mtima pa kumvetsa zinthu;
und lauscht dein Ohr auf Weisheit und neigt dein Herz sich zur Vernunft
3 ngati upempha kuti uzindikire zinthu inde kupempha ndi mtima wonse kuti ukhale womvetsa zinthu,
und rufst nach Einsicht du und schreist du nach Verstand
4 ngati ufunafuna nzeruyo ngati siliva ndi kuyisakasaka ngati chuma chobisika,
und suchst du sie wie Silber und spürst ihr nach gleich wie verborgnen Schätzen,
5 ndiye udzamvetsa bwino tanthauzo la kuopa Yehova; ndipo udzapezanso tanthauzo la kumudziwa Yehova.
alsdann begreifst auch du die Furcht des Herrn, gewinnst Erkenntnis Gottes,
6 Pakuti Yehova ndiye amapereka nzeru, ndipo mʼkamwa mwake mumachokera chidziwitso ndi kumvetsa zinthu.
daß Weisheit nur der Herr verleiht, aus seinem Mund Erkenntnis und Vernunft herrühren,
7 Anthu olungama zinthu zimawayendera bwino chifukwa Yehova amakhala nawo. Paja Yehova ndiye chishango cha amene amayenda mwangwiro,
und daß er guten Rat für Rechtliche aufspart, ein Schild ist denen, die unsträflich wandeln,
8 pakuti ndiye mlonda wa njira zolungama. Iye amasamala mayendedwe a anthu ake okhulupirika.
die von des Rechtes Bahnen nicht abweichen, jedoch die Wege seiner Frommen gehen, -
9 Choncho udzamvetsa tanthauzo la ungwiro, chilungamo, kusakondera ndi njira iliyonse yabwino.
alsdann wirst du Gerechtigkeit und Recht verstehen, Geradheit, jede Bahn des Guten,
10 Pakuti nzeru idzalowa mu mtima mwako, kudziwa zinthu kudzakusangalatsa.
denn Weisheit kommt dir in das Herz und die Erkenntnis weilt in deiner Seele.
11 Kuganizira bwino za mʼtsogolo kudzakusunga; kumvetsa zinthu bwino kudzakuteteza.
Dann ist die Umsicht dir ein Schutz; Vernunft ist deine Hüterin.
12 Nzeru idzakupulumutsa ku mayendedwe oyipa, kwa anthu amabodza,
Sie rettet dich vor schlimmen Schurken, vor Lügenrednern,
13 amene amasiya njira zolungama namayenda mʼnjira zamdima,
die von des Lichtes Pfaden lassen und auf dem Weg des Finstern wandeln, -
14 amene amakondwera pochita zoyipa namasangalala ndi kuyipa kwa ntchito zawo zonyansa.
die freudig Böses tun und ob dem Untergang des Nächsten jubeln, -
15 Amenewa ndi anthu a njira zawo zokhotakhota, ndipo makhalidwe awo ndi achinyengo.
vor Leuten, deren Pfade krumm und deren Bahnen ganz verkehrt.
16 Nzeruyo idzakupulumutsanso kwa mkazi wachigololo; kwa mkazi wachilendo woyankhula moshashalika,
Sie rettet dich vor andern Weibern, vor einer Fremden voller Schmeichelreden,
17 amene wasiya mwamuna wa chitsikana wake ndi kuyiwala pangano limene anachita pamaso pa Mulungu wake.
die den Vertrauten ihrer Jugend läßt und den vor ihrem Gott geschlossenen Bund vergißt.
18 Pakuti nyumba yake imatsetserekera ku imfa; njira zake zimamufikitsa ku manda.
Dem Tode nahe steht ihr Haus, und zu den Schatten führen ihre Bahnen.
19 Opita kwa iye palibe ndi mmodzi yemwe amabwerera kapena kupezanso njira zamoyo.
Wer zu ihr eingeht, kehrt nicht wieder; betritt niemals des Lebens Pfade.
20 Choncho iwe uziyenda mʼnjira za anthu abwino, uzitsata njira za anthu ochita chilungamo.
Dann kannst du auf dem Weg der Guten wandeln und an der Frommen Pfad dich halten.
21 Pakuti anthu olungama ndiwo ati adzakhale mʼdziko ndipo anthu angwiro ndiwo ati adzakhazikike mʼmenemo;
Denn nur wer recht tut, darf im Lande wohnen; nur wer untadelig, drin übrigbleiben.
22 Koma anthu oyipa adzachotsedwa mʼdzikomo, ndipo anthu onyenga adzachotsedwamo.
Die Schlechten aber werden aus dem Land vertilgt und die Betrüger aus ihm ausgerissen.

< Miyambo 2 >