< Miyambo 2 >
1 Mwana wanga, ngati ulandira mawu anga ndi kusunga malamulo anga mu mtima mwako,
My son, if you accept what I say and value my instructions,
2 ndiponso kutchera khutu lako ku nzeru ndi kuyikapo mtima pa kumvetsa zinthu;
if you pay attention to wisdom and really try to understand;
3 ngati upempha kuti uzindikire zinthu inde kupempha ndi mtima wonse kuti ukhale womvetsa zinthu,
if you cry out for insight and call loudly for help in understanding;
4 ngati ufunafuna nzeruyo ngati siliva ndi kuyisakasaka ngati chuma chobisika,
if you look for it as if it were silver and search for it as if it were hidden treasure;
5 ndiye udzamvetsa bwino tanthauzo la kuopa Yehova; ndipo udzapezanso tanthauzo la kumudziwa Yehova.
then you will understand how to relate to the Lord and discover the truth about God.
6 Pakuti Yehova ndiye amapereka nzeru, ndipo mʼkamwa mwake mumachokera chidziwitso ndi kumvetsa zinthu.
The Lord is the source of wisdom; what he says provides knowledge that makes sense.
7 Anthu olungama zinthu zimawayendera bwino chifukwa Yehova amakhala nawo. Paja Yehova ndiye chishango cha amene amayenda mwangwiro,
He gives good judgment to those who live right; he defends those who have good sense.
8 pakuti ndiye mlonda wa njira zolungama. Iye amasamala mayendedwe a anthu ake okhulupirika.
He supports those who act fairly and protects those who trust in him.
9 Choncho udzamvetsa tanthauzo la ungwiro, chilungamo, kusakondera ndi njira iliyonse yabwino.
Then you will be able to recognize what is right and just and fair, in fact all that is good in the way you should live.
10 Pakuti nzeru idzalowa mu mtima mwako, kudziwa zinthu kudzakusangalatsa.
For wisdom will fill your mind, and knowledge will make you happy.
11 Kuganizira bwino za mʼtsogolo kudzakusunga; kumvetsa zinthu bwino kudzakuteteza.
Good decisions will keep you on track; thinking logically will keep you safe.
12 Nzeru idzakupulumutsa ku mayendedwe oyipa, kwa anthu amabodza,
Doing this will save you from the ways of evil, from men who tell twisted lies,
13 amene amasiya njira zolungama namayenda mʼnjira zamdima,
who turn away from following what is right to walk down paths of darkness.
14 amene amakondwera pochita zoyipa namasangalala ndi kuyipa kwa ntchito zawo zonyansa.
They happily do wrong; they love how twisted evil is.
15 Amenewa ndi anthu a njira zawo zokhotakhota, ndipo makhalidwe awo ndi achinyengo.
They live crooked lives doing deceitful things.
16 Nzeruyo idzakupulumutsanso kwa mkazi wachigololo; kwa mkazi wachilendo woyankhula moshashalika,
Doing this will also save you from a woman who acts immorally, from a woman who like a prostitute tries to seduce you with flattering words.
17 amene wasiya mwamuna wa chitsikana wake ndi kuyiwala pangano limene anachita pamaso pa Mulungu wake.
Such a woman has left her husband she married when she was young, forgetting the promises she made before God.
18 Pakuti nyumba yake imatsetserekera ku imfa; njira zake zimamufikitsa ku manda.
What happens in her house leads to death; following her way leads to the grave.
19 Opita kwa iye palibe ndi mmodzi yemwe amabwerera kapena kupezanso njira zamoyo.
No one who goes to her comes back; they don't ever find the way back to life again.
20 Choncho iwe uziyenda mʼnjira za anthu abwino, uzitsata njira za anthu ochita chilungamo.
So you should follow the way of the good, and make sure you stay on the paths of those who do right.
21 Pakuti anthu olungama ndiwo ati adzakhale mʼdziko ndipo anthu angwiro ndiwo ati adzakhazikike mʼmenemo;
For only people who live right will live in the land; only honest people will remain there.
22 Koma anthu oyipa adzachotsedwa mʼdzikomo, ndipo anthu onyenga adzachotsedwamo.
But the wicked will be thrown out of the land; those who are untrustworthy will be pulled out by the roots.