< Levitiko 16 >

1 Atafa ana awiri a Aaroni amene anaphedwa atapita pamaso pa Yehova mosayenera, Yehova anayankhula ndi Mose.
و خداوند موسی را بعد از مردن دو پسرهارون، وقتی که نزد خداوند آمدند ومردند خطاب کرده، گفت:۱
2 Yehova anawuza Mose kuti, “Uza mchimwene wako Aaroni kuti asamalowe ku Malo Wopatulika, kuseri kwa katani, pamaso pa chivundikiro cha Bokosi la Chipangano nthawi iliyonse imene akufuna kuopa kuti angadzafe, pakuti Ine ndimaoneka mu mtambo umene uli pamwamba pa chivundikiro cha Bokosi la Chipangano.
«پس خداوند به موسی گفت: برادر خود هارون را بگو که به قدس درون حجاب پیش کرسی رحمت که بر تابوت است همه وقت داخل نشود، مبادا بمیرد، زیرا که در ابر بر کرسی رحمت ظاهر خواهم شد.۲
3 “Aaroni azilowa Malo Wopatulika Kwambiri motere: azitenga mwana wangʼombe wamwamuna kuti akhale nsembe yopepesera machimo ndi nkhosa yayimuna kuti ikhale nsembe yopsereza.
و بااین چیزها هارون داخل قدس بشود، با گوساله‌ای برای قربانی گناه، و قوچی برای قربانی سوختنی.۳
4 Azivala mwinjiro wopatulika wa nsalu yosalala, azivalanso kabudula wa mʼkati wa nsalu yosalala, azimanga lamba wa nsalu yosalala, ndipo avalenso nduwira ya nsalu yosalala kumutu. Zimenezi ndi nsalu zopatulika ndipo atasamba thupi lonse azivala zimenezi.
و پیراهن کتان مقدس را بپوشد، و زیر جامه کتان بر بدنش باشد، و به کمربند کتان بسته شود، و به عمامه کتان معمم باشد. اینها رخت مقدس است. پس بدن خود را به آب غسل داده، آنها را بپوشد.۴
5 Kuchokera pa gulu la Aisraeli, Aaroni azitenga mbuzi zazimuna ziwiri kuti zikhale nsembe yopepesera machimo ndi nkhosa yayimuna kuti ikhale nsembe yopsereza.
و از جماعت بنی‌اسرائیل دو بز نرینه برای قربانی گناه، و یک قوچ برای قربانی سوختنی بگیرد.۵
6 “Aaroni apereke ngʼombe yayimuna kuti ikhale yopepesera machimo a iye mwini kuti achite mwambo wopepesera machimo ake pamodzi ndi a banja lake.
و هارون گوساله قربانی گناه را که برای خود اوست بگذراند، و برای خود و اهل خانه خود کفاره نماید.۶
7 Kenaka atenge mbuzi ziwiri zija ndipo aziyimike pamaso pa Yehova pa khomo la tenti ya msonkhano.
و دو بز را بگیرد و آنها را به حضور خداوند به در خیمه اجتماع حاضر سازد.۷
8 Aaroni ndiye achite maere pa mbuzi ziwirizo kuti imodzi ikhale ya Yehova, ndipo inayo ikhale ya Azazele.
و هارون بر آن دو بز قرعه اندازد، یک قرعه برای خداوند و یک قرعه برای عزازیل.۸
9 Aaroni abwere ndi mbuzi imene maere aonetsa kuti ndi ya Yehova, ndipo apereke kuti ikhale nsembe yopereka chifukwa cha tchimo.
و هارون بزی را که قرعه برای خداوند بر آن برآمد نزدیک بیاورد، و بجهت قربانی گناه بگذراند.۹
10 Koma mbuzi imene maere aonetsa kuti ndi yosenza machimo, apereke ya moyo pamaso pa Yehova, kuti achite mwambo wopepesera machimo pa mbuziyo poyitumiza ku chipululu kuti ikhale ya Azazele.
و بزی که قرعه برای عزازیل بر آن برآمد به حضور خداوندزنده حاضر شود، و بر آن کفاره نماید و آن را برای عزازیل به صحرا بفرستد.۱۰
11 “Aaroni apereke ngʼombe yayimuna kuti ikhale nsembe yopepesera machimo ake. Ndiye achite mwambo wopepesera machimo a iye mwini wake pamodzi ndi banja lake. Pambuyo pake aphe ngʼombe yopepesera machimo ake aja.
«و هارون گاو قربانی گناه را که برای خوداوست نزدیک بیاورد، و برای خود و اهل خانه خود کفاره نماید، و گاو قربانی گناه را که برای خود اوست ذبح کند.۱۱
12 Kenaka iye atenge chofukizira chodzaza ndi makala a moto ochokera pa guwa lansembe pamaso pa Yehova. Atengenso lubani wonunkhira ndi woperapera wokwanira manja awiri, ndipo alowe naye kuseri kwa katani.
و مجمری پر از زغال آتش از روی مذبح که به حضور خداوند است ودو مشت پر از بخور معطر کوبیده شده برداشته، به اندرون حجاب بیاورد.۱۲
13 Athire lubani pa moto pamaso pa Yehova kuti utsi wa lubaniyo uphimbe chivundikiro chimene chili pamwamba pa Bokosi la Chipangano, kuti Aaroniyo asafe.
و بخور را بر آتش به حضور خداوند بنهد تا ابر بخور کرسی رحمت راکه بر تابوت شهادت است بپوشاند، مبادا بمیرد.۱۳
14 Ndipo atenge magazi ena a ngʼombeyo, awawaze ndi chala chake pa chivundikiro cha kummawa; kenaka awaze magaziwo ndi chala chake kasanu ndi kawiri patsogolo pa chivundikirocho.
و از خون گاو گرفته، بر کرسی رحمت به انگشت خود به طرف مشرق بپاشد، و قدری ازخون را پیش روی کرسی رحمت هفت مرتبه بپاشد.۱۴
15 “Kenaka Aaroni aphe mbuzi ya nsembe yopepesera machimo a anthu, ndipo magazi ake alowe nawo kuseri kwa katani ndi kuchita chimodzimodzi monga anachitira ndi magazi a ngʼombe aja: Aaroni awaze magaziwo pa chivundikiro chija ndi patsogolo pa chivundikirocho.
پس بز قربانی گناه را که برای قوم است ذبح نماید، و خونش را به اندرون حجاب بیاورد، وبا خونش چنانکه با خون گاو عمل کرده بودعمل کند، و آن را بر کرسی رحمت و پیش روی کرسی رحمت بپاشد.۱۵
16 Pamenepo ndiye kuti wansembeyo wachita mwambo wopepesera ku Malo Wopatulika chifukwa cha kudetsedwa ndi kuwukira kwa Aisraeli pa machimo ena aliwonse amene achita. Achite chimodzimodzi ndi tenti ya msonkhano imenenso ili yodetsedwa chifukwa cha machimo awo.
و برای قدس کفاره نماید به‌سبب نجاسات بنی‌اسرائیل، و به‌سبب تقصیرهای ایشان با تمامی گناهان ایشان، و برای خیمه اجتماع که با ایشان در میان نجاسات ایشان ساکن است، همچنین بکند.۱۶
17 Mu tenti ya msonkhano musakhale munthu ndi mmodzi yemwe nthawi imene Aaroni akupita kukachita mwambo wopepesera ku Malo Wopatulika mpaka atatulukako. Musakhale munthu mu tenti ya msonkhano mpaka atachita mwambo wopepesera machimo a iye mwini wake, banja lake ndi gulu lonse la Aisraeli.
و هیچکس درخیمه اجتماع نباشد، و از وقتی که برای کردن کفاره داخل قدس بشود تا وقتی که بیرون آید، پس برای خود و برای اهل خانه خود و برای تمامی جماعت اسرائیل کفاره خواهد کرد.۱۷
18 “Kenaka, Aaroniyo akatuluka apite ku guwa limene lili pamaso pa Yehova ndi kulichitira mwambo wolipepesera. Atengeko magazi a ngʼombe yayimuna ndiponso magazi a mbuzi ndi kuwapaka pa nyanga zonse za guwa lansembe.
پس نزد مذبح که به حضور خداوند است بیرون آید، و برای آن کفاره نماید، و از خون گاو و ازخون بز گرفته، آن را بر شاخه های مذبح بهر طرف بپاشد.۱۸
19 Magazi ena awawaze pa guwalo ndi chala chake kasanu ndi kawiri kuliyeretsa ndi kulipatula kuchotsa zodetsa za Aisraeli.
و قدری از خون را به انگشت خود هفت مرتبه بر آن بپاشد و آن را تطهیر کند، و آن رااز نجاسات بنی‌اسرائیل تقدیس نماید.۱۹
20 “Aaroni akatsiriza mwambo wopepesera Malo Wopatulika, tenti ya msonkhano ndi guwa, azibwera ndi mbuzi yamoyo kudzayipereka nsembe.
«و چون از کفاره نمودن برای قدس و برای خیمه اجتماع و برای مذبح فارغ شود، آنگاه بززنده را نزدیک بیاورد.۲۰
21 Aaroni asanjike manja ake pa mutu wa mbuziyo ndipo awulule pa mbuziyo zoyipa zonse ndi zowukira zonse za Aisraeli, kutanthauza machimo awo onse. Machimowo awayike pa mutu wa mbuziyo. Kenaka munthu amene anasankhidwa athamangitsire mbuziyo ku chipululu.
و هارون دو دست خودرا بر سر بز زنده بنهد، و همه خطایای بنی‌اسرائیل و همه تقصیرهای ایشان را با همه گناهان ایشان اعتراف نماید، و آنها را بر سر بز بگذارد و آن را به‌دست شخص حاضر به صحرا بفرستد.۲۱
22 Mbuziyo isenze machimo awo onse ndi kupita nawo kutali ndipo munthuyo aleke mbuziyo kuti ipite ku chipululuko.
و بزهمه گناهان ایشان را به زمین ویران بر خودخواهد برد. پس بز را به صحرا رها کند.۲۲
23 “Pambuyo pake Aaroni alowe mu tenti ya msonkhano ndi kuvula zovala zosalala zija zimene anavala polowa ku Malo Wopatulika ndi kuzisiya komweko.
وهارون به خیمه اجتماع داخل شود، و رخت کتان را که در وقت داخل شدن به قدس پوشیده بودبیرون کرده، آنها را در آنجا بگذارد.۲۳
24 Asambe thupi lonse ku Malo Wopatulika ndi kuvala zovala zake za nthawi zonse. Kenaka atuluke ndi kukapereka nsembe yopsereza ya iye mwini, ndiponso nsembe yopsereza yoperekera anthu. Akatero ndiye kuti wachita mwambo wopepesera machimo a iye mwini wake ndi a anthu.
و بدن خود را در جای مقدس به آب غسل دهد، ورخت خود را پوشیده، بیرون آید، و قربانی سوختنی خود و قربانی سوختنی قوم را بگذراند، و برای خود و برای قوم کفاره نماید.۲۴
25 Mafuta a nyama yopepesera machimo awatenthe pa guwa lansembe.
و پیه قربانی گناه را بر مذبح بسوزاند.۲۵
26 “Tsono munthu amene anaperekeza mbuzi yosenza machimo ija achape zovala zake ndi kusamba. Pambuyo pake alowe ku msasa.
و آنکه بز رابرای عزازیل رها کرد رخت خود را بشوید و بدن خود را به آب غسل دهد، و بعد از آن به لشکرگاه داخل شود.۲۶
27 Ngʼombe ndi mbuzi zoperekera nsembe yopepesera machimo zimene magazi ake anabwera nawo kuti achitire mwambo wopepesera Malo Wopatulika, azitulutsire kunja kwa msasa. Koma zikopa zake, nyama yake ndi matumbo ake azitenthe.
و گاو قربانی گناه و بز قربانی گناه را که خون آنها به قدس برای کردن کفاره آورده شد، بیرون لشکرگاه برده شود، و پوست و گوشت و سرگین آنها را به آتش بسوزانند.۲۷
28 Munthu amene azitenthe achape zovala zake ndi kusamba. Pambuyo pake alowe mu msasa.
و آنکه آنهارا سوزانید رخت خود را بشوید و بدن خود را به آب غسل دهد، و بعد از آن به لشکرگاه داخل شود.۲۸
29 “Ili likhale lamulo lanu lamuyaya: Mwezi wachisanu ndi chiwiri, pa tsiku la khumi la mwezi, mugonje pamaso pa Yehova. Musamagwire ntchito iliyonse, kaya ndinu mbadwa kapena mlendo amene akukhala pakati panu,
«و این برای شما فریضه دائمی باشد، که درروز دهم از ماه هفتم جانهای خود را ذلیل سازید، و هیچ کار مکنید، خواه متوطن خواه غریبی که درمیان شما ماوا گزیده باشد.۲۹
30 chifukwa tsiku limeneli kudzachitika mwambo wopepesera machimo anu, kukuyeretsani kuti mukhale oyeretsedwa ku machimo anu pamaso pa Yehova.
زیرا که در آن روزکفاره برای تطهیر شما کرده خواهد شد، و ازجمیع گناهان خود به حضور خداوند طاهرخواهید شد.۳۰
31 Limeneli ndi tsiku lanu la Sabata lopumula, ndipo muzigonja pamaso pa Yehova. Limeneli ndi lamulo lanu la muyaya.
این سبت آرامی برای شماست، پس جانهای خود را ذلیل سازید. این است فریضه دائمی.۳۱
32 Wansembe amene wadzozedwa ndi kupatulidwa kuti akhale wansembe kulowa mʼmalo mwa abambo ake ndiye azichita mwambo wopepesera machimo atavala zovala zake zosalala ndi zopatulika.
و کاهنی که مسح شده، و تخصیص شده باشد، تا در جای پدر خود کهانت نمایدکفاره را بنماید. و رختهای کتان یعنی رختهای مقدس را بپوشد.۳۲
33 Adzachite mwambo wopepesera machimo Malo Wopatulika, tenti ya msonkhano ndi guwa lansembe. Adzachitenso mwambo wopepesera anzake ndi gulu lonse la anthu.
و برای قدس مقدس کفاره نماید، و برای خیمه اجتماع و مذبح کفاره نماید، و برای کهنه و تمامی جماعت قوم کفاره نماید.۳۳
34 “Ili likhale lamulo lanu lamuyaya. Mwambo wopepesera machimo uzichitika kamodzi pa chaka chifukwa cha machimo a anthu onse.” Ndipo Mose anachita monga momwe Yehova analamulira.
و این برای شما فریضه دائمی خواهد بود تابرای بنی‌اسرائیل از تمامی گناهان ایشان یک مرتبه هر سال کفاره شود.» پس چنانکه خداوندموسی را امر فرمود، همچنان بعمل آورد.۳۴

< Levitiko 16 >