< Yoswa 2 >

1 Tsono Yoswa mwana wa Nuni anatuma anthu awiri okazonda dziko mwachinsinsi kuchokera ku Sitimu. Iye anawawuza kuti, “Pitani mukaone dzikolo makamaka mzinda wa Yeriko.” Kotero iwo anapita ndipo anakafika ku nyumba ya mkazi wadama dzina lake Rahabe, ndipo anagona kumeneko.
Then Ioshua the sonne of Nun sent out of Shittim two men to spie secretly, saying, Go, view the land, and also Iericho: and they went, and came into an harlots house, named Rahab, and lodged there.
2 Mfumu ya Yeriko inawuzidwa kuti, “Aisraeli ena afika mu mzinda muno usiku uno kudzazonda dziko.”
Then report was made to the King of Iericho, saying, Beholde, there came men hither to night, of the children of Israel, to spie out the countrey.
3 Choncho Mfumu ya Yeriko inatumiza uthenga kwa Rahabe kuti, “Atulutse anthu amene abwera ku nyumba kwakowo chifukwa iwo abwera kuti adzazonde dzikoli.”
And the King of Iericho sent vnto Rahab, saying, Bring foorth the men that are come to thee, and which are entred into thine house: for they be come to search out all the land.
4 Koma pa nthawiyi nʼkuti mkaziyo atatenga amuna awiriwo ndi kuwabisa. Tsono anayankha kuti, “Inde, anthuwo anafikadi ku nyumba kuno. Koma sindinadziwe kumene anachokera.
(But ye woman had taken the two men, and hid them) Therefore saide she thus, There came men vnto me, but I wist not whence they were.
5 Iwo achoka kuno ndi chisisira, chipata cha mzinda chili pafupi kutsekedwa. Ndiye sindidziwa kumene alowera. Koma mukawalondola msanga muwapeza.”
And when they shut the gate in the darke, the men went out, whither the men went I wote not: follow ye after them quickly, for ye shall ouertake them.
6 Koma nʼkuti atawakweza pa denga azondiwo ndi kuwabisa pansi pa mapesi a thonje amene iye anawayika pa dengapo.
(But she had brought them vp to the roofe of the house, and hidde them with the stalkes of flaxe, which she had spread abroad vpon the roofe)
7 Nthumwi za mfumu zija zitatuluka ndipo chipata chinatsekedwa. Nthumwizo zinapita kukawafunafuna azondi aja mpaka ku dooko la Yorodani.
And certaine men pursued after them, the way to Iorden, vnto the foordes, and as soone as they which pursued after them, were gone out, they shut the gate.
8 Azondiwo asanagone, Rahabe anakwera pa denga
And before they were a sleepe, she came vp vnto them vpon the roofe,
9 ndipo anawawuza kuti, “Ine ndikudziwa kuti Yehova wakupatsani dziko lino ndipo tili ndi mantha. Anthu onse a mʼdziko lino ali ndi mantha chifukwa cha inu.
And saide vnto the men, I knowe that the Lord hath giuen you the land, and that the feare of you is fallen vpon vs, and that all the inhabitants of the land faint because of you.
10 Ife tinamva mmene Yehova anawumitsira madzi a Nyanja Yofiira inu mukufika pamene munatuluka mʼdziko la Igupto. Tamvanso zimene munachita kwa Sihoni ndi Ogi, mafumu awiri a Aamori amene ali kummawa kwa Yorodani. Inu munawawononga kotheratu.
For we haue heard, howe the Lord dried vp the water of the redde Sea before you, when you came out of Egypt, and what you did vnto the two Kings of the Amorites, that were on the other side Iorden, vnto Sihon and to Og, whom ye vtterly destroyed:
11 Titamva zimenezi, ife tinataya mtima ndipo aliyense wa ife ali ndi mantha chifukwa cha inu. Tikudziwa kuti Yehova Mulungu wanu ndi Mulungu wa kumwamba ndi dziko lapansi.
And when wee heard it, our heartes did faint, and there remained no more courage in any because of you: for the Lord your God, he is the God in heauen aboue, and in earth beneath.
12 Choncho mulumbire pamaso pa Yehova ndi kundipatsa chizindikiro choti mudzachitadi zimene mwalonjeza, kuti monga inu ndakuchitirani chifundo, inunso mudzachitira chifundo a pa banja la abambo anga.
Now therefore, I pray you, sweare vnto me by the Lord; that as I haue shewed you mercie, ye will also shewe mercie vnto my fathers house, and giue me a true token,
13 Inu mulonjeze kuti simudzapha abambo anga ndi amayi anga, abale anga ndi alongo anga ndi mabanja awo omwe.”
And that yee will saue aliue my father and my mother, and my brethren, and my sisters, and all that they haue: and that yee will deliuer our soules from death.
14 Anthuwo anamuyankha kuti, “Ife ndife okonzeka kufa chifukwa cha inu. Ngati iwe sudzawulula zimene tachitazi, ndiye kuti ife tidzakukomera mtima ndi kusunga pangano lathu ndi iwe, Yehova akadzatipatsa dziko lino.”
And the men answered her, Our life for you to die, if ye vtter not this our businesse: and when the Lord hath giuen vs the lande, we will deale mercifully and truely with thee.
15 Popeza nyumba ya Rahabe inali pa linga la mzindawo, azondi aja anatulukira pa zenera. Rahabe anawatsitsa pansi ndi chingwe.
Then she let them downe by a corde thorowe the windowe: for her house was vpon the towne wall, and she dwelt vpon the wall.
16 Iye anawawuza kuti, “Pitani ku mapiri kuti okuthamangiraniwo asakupezeni. Mukabisale kumeneko masiku atatu mpaka iwo atabwerera, ndipo kenaka muzikapita kwanu.”
And she said vnto them, Goe you into the mountaine, least the pursuers meete with you, and hide your selues there three dayes, vntill the pursuers be returned: then afterwarde may yee goe your way.
17 Anthuwo anati kwa iye, “Lonjezo limene watichititsa ifeli tidzalisungadi
And the men said vnto her, We will be blamelesse of this thine othe, which thou hast made vs sweare.
18 tikadzalowa mʼdzikoli, iwe udzamangirire kansalu kofiira pa zenera limene unatitulutsira, ndi kusonkhanitsa abambo ako, amayi ako, abale ako ndi banja lako lonse mʼnyumba muno.
Behold, when we come into the land, thou shalt bind this cord of red threde in the window, whereby thou lettest vs downe, and thou shalt bring thy father and thy mother, and thy brethren, and all thy fathers houshold home to thee.
19 Ngati wina aliyense adzatuluka mʼnyumbamo kuti azikayendayenda mu msewu, magazi ake adzakhala pamutu pake, ife sitidzapalamula kanthu. Koma wina aliyense wokhala mʼnyumba mwakomo akadzaphedwa, mlandu udzakhala wathu.
And whosoeuer then doeth goe out at the doores of thine house into the streete, his blood shalbe vpon his head, and we will be giltlesse: but whosoeuer shall be with thee in the house, his blood shalbe on our head, if any hande touch him:
20 Komanso iwe ukangowulula zimene ife tikuchitazi ndiye kuti ife sitidzasunga zimene talonjezazi.”
And if thou vtter this our matter, we will be quite of thine othe, which thou hast made vs sweare.
21 Rahabe anayankha kuti, “Zikhale monga mwaneneramo.” Kenaka iye anawatulutsa ndipo iwowo anapita. Pambuyo pake Rahabe anamangirira kansalu kofiira pa zenera paja.
And she answered, According vnto your wordes, so be it: then she sent them away, and they departed, and she bound the red cord in ye window.
22 Azondi aja anachoka napita ku mapiri ndipo anakhalako masiku atatu. Apa nʼkuti otumidwa ndi mfumu aja atawafunafuna ponseponse nʼkubwerera osawapeza.
And they departed, and came into the mountaine, and there abode three dayes, vntil the pursuers were returned: and the pursuers sought them throughout all the way, but founde them not.
23 Pambuyo pake azondi awiri aja anayamba ulendo wobwerera kwawo. Anatsika ku mapiri kuja, nawoloka mtsinje mpaka anakafika kwa Yoswa mwana wa Nuni. Ndipo anamuwuza zonse zimene zinawachitikira.
So the two men returned, and descended from the mountaine, and passed ouer, and came to Ioshua the sonne of Nun, and tolde him all things that came vnto them.
24 Iwo anati kwa Yoswa, “Ndithu, Yehova wapereka dziko lonse mʼmanja mwathu. Anthu onse kumeneko akuchita nafe mantha.”
Also they saide vnto Ioshua, Surely the Lord hath deliuered into our handes all the lande: for euen all the inhabitants of the countrey faint because of vs.

< Yoswa 2 >